< Job 3 >

1 Aftir these thingis Joob openyde his mouth,
Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
2 and curside his dai, and seide, Perische the dai in which Y was borun,
Ndipo Yobu anati:
3 and the nyyt in which it was seid, The man is conceyued.
“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
4 Thilke dai be turnede in to derknessis; God seke not it aboue, and be it not in mynde, nethir be it liytned with liyt.
Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
5 Derknessis make it derk, and the schadewe of deeth and myist occupie it; and be it wlappid with bittirnesse.
Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
6 Derk whirlwynde holde that niyt; be it not rikynyd among the daies of the yeer, nethir be it noumbrid among the monethes.
Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
7 Thilke nyyt be soleyn, and not worthi of preisyng.
Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
8 Curse thei it, that cursen the dai, that ben redi to reise Leuyathan.
Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
9 Sterris be maad derk with the derknesse therof; abide it liyt, and se it not, nethir the bigynnyng of the morwetid risyng vp.
Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
10 For it closide not the doris of the wombe, that bar me, nethir took awei yuels fro min iyen.
Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
11 Whi was not Y deed in the wombe? whi yede Y out of the wombe, and perischide not anoon?
“Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
12 Whi was Y takun on knees? whi was Y suclid with teetis?
Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
13 For now Y slepynge schulde be stille, and schulde reste in my sleep,
Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
14 with kyngis, and consuls of erthe, that bilden to hem soleyn places;
pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
15 ethir with prynces that han gold in possessioun, and fillen her housis with siluer;
pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
16 ethir as a `thing hid not borun Y schulde not stonde, ethir whiche conseyued sien not liyt.
Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
17 There wickid men ceessiden of noise, and there men maad wery of strengthe restiden.
Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
18 And sum tyme boundun togidere with out disese thei herden not the voys of the wrongful axere.
A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
19 A litil man and greet man be there, and a seruaunt free fro his lord.
Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
20 Whi is liyt youun to the wretche, and lijf to hem that ben in bitternesse of soule?
“Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
21 Whiche abiden deeth, and it cometh not;
kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
22 as men diggynge out tresour and ioien greetly, whanne thei han founde a sepulcre?
amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
23 Whi is liyt youun to a man, whos weie is hid, and God hath cumpassid hym with derknessis?
Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
24 Bifore that Y ete, Y siyhe; and as of watir flowynge, so is my roryng.
Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
25 For the drede, which Y dredde, cam to me; and that, that Y schamede, bifelde.
Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
26 Whether Y dissymilide not? whether Y was not stille? whether Y restide not? and indignacioun cometh on me.
Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”

< Job 3 >