< Job 21 >

1 Forsothe Joob answeride, and seide,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Y preye, here ye my wordis, and do ye penaunce.
“Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
3 Suffre ye me, that Y speke; and leiye ye aftir my wordis, if it schal seme worthi.
Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
4 Whether my disputyng is ayens man, that skilfuli Y owe not to be sori?
“Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
5 Perseyue ye me, and be ye astonyed; and sette ye fyngur on youre mouth.
Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
6 And whanne Y bithenke, Y drede, and tremblyng schakith my fleisch.
Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
7 Whi therfor lyuen wickid men? Thei ben enhaunsid, and coumfortid with richessis.
Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
8 Her seed dwellith bifor hem; the cumpeny of kynesmen, and of sones of sones dwellith in her siyt.
Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
9 Her housis ben sikur, and pesible; and the yerde of God is not on hem.
Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
10 The cow of hem conseyuede, and caluede not a deed calf; the cow caluyde, and is not priued of hir calf.
Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
11 Her litle children goen out as flockis; and her yonge children `maken fulli ioye with pleies.
Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
12 Thei holden tympan, and harpe; and ioien at the soun of orgun.
Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
13 Thei leden in goodis her daies; and in a point thei goen doun to hellis. (Sheol h7585)
Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
14 Whiche men seiden to God, Go thou awei fro us; we nylen the kunnyng of thi weies.
Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
15 Who is Almiyti God, that we serue him? and what profitith it to vs, if we preien him?
Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
16 Netheles for her goodis ben not in her hond, `that is, power, the counsel of wickid men be fer fro me.
Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
17 Hou ofte schal the lanterne of wickid men be quenchid, and flowing schal come on hem, and God schal departe the sorewis of his stronge veniaunce?
“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
18 Thei schulen be as chaffis bifor the face of the wynd; and as a deed sparcle, whiche the whirlewynd scaterith abrood.
Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
19 God schal kepe the sorewe of the fadir to hise sones; and whanne he hath yoldun, thanne he schal wite.
Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
20 Hise iyen schulen se her sleyng; and he schal drynke of the stronge veniaunce of Almyyti God.
Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
21 For whi what perteyneth it to hym of his hows aftir hym, thouy the noumbre of his monethis be half takun awey?
Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
22 Whether ony man schal teche God kunnyng, which demeth hem that ben hiye?
“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
23 This yuel man dieth strong and hool, riche and blesful, `that is, myrie.
Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
24 Hise entrails ben ful of fatnesse; and hise boonys ben moistid with merowis.
thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
25 Sotheli anothir wickid man dieth in the bittirnesse of his soule, and with outen ony richessis.
Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
26 And netheles thei schulen slepe togidere in dust, and wormes schulen hile hem.
Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
27 Certis Y knowe youre wickid thouytis, and sentensis ayens me.
“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
28 For ye seien, Where is the hows of the prince? and where ben the tabernaclis of wickid men?
Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
29 Axe ye ech of `the weie goeris; and ye schulen knowe, that he vndurstondith these same thingis,
Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
30 that an yuel man schal be kept in to the dai of perdicioun, and schal be led to the dai of woodnesse.
Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
31 Who schal repreue hise weies bifor hym? and who schal yelde to hym tho thingis, whiche he hath doon?
Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
32 He schal be led to the sepulcris; and he schal wake in the heep of deed men.
Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
33 He was swete to the `stoonys, ether filthis, of helle; and drawith ech man aftir hym, and vnnoumbrable men bifor him.
Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
34 Hou therfor coumforten ye me in veyn, sithen youre answeris ben schewid to `repugne to treuthe?
“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”

< Job 21 >