< Job 16 >

1 Forsothe Joob answeride, and seide, Y `herde ofte siche thingis;
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 alle ye ben heuy coumfortouris.
“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
3 Whether wordis ful of wynd schulen haue an ende? ether ony thing is diseseful to thee, if thou spekist?
Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
4 Also Y myyte speke thingis lijk to you, and `Y wolde, that youre soule were for my soule; and Y wolde coumfort you by wordis, and Y wolde moue myn heed on you;
Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
5 Y wolde make you stronge bi my mouth, and Y wolde moue lippis as sparynge you.
Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
6 But what schal Y do? If Y speke, my sorewe restith not; and if Y am stille, it goith not awei fro me.
“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
7 But now my sorewe hath oppressid me, and alle my lymes ben dryuun in to nouyt.
Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
8 My ryuelyngis seien witnessyng ayens me, and a fals spekere is reisid ayens my face, and ayenseith me.
Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
9 He gaderide togidere his woodnesse in me, and he manaasside me, and gnastide ayens me with his teeth; myn enemye bihelde me with ferdful iyen.
Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
10 Thei openyden her mouthis on me, and thei seiden schenschip, and smytiden my cheke; and thei ben fillid with my peynes.
Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
11 God hath closid me togidere at the wickid, and hath youe me to the hondis of wickid men.
Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
12 Y thilke riche man and famouse sum tyme, am al to brokun sudeynli; `he helde my nol; he hath broke me, and hath set me as in to a signe.
Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
13 He hath cumpasside me with hise speris, he woundide togidere my leendis; he sparide not, and schedde out myn entrails in to the erthe.
anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
14 He beet me with wounde on wounde; he as a giaunt felde in on me.
Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
15 Y sewide togidere a sak on my skyn; and Y hilide my fleisch with aische.
“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
16 My face bolnyde of wepynge, and myn iyeliddis wexiden derke.
Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
17 Y suffride these thingis with out wickidnesse of myn hond, `that is, werk, whanne Y hadde cleene preieris to God.
komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
18 Erthe, hile thou not my blood, and my cry fynde not in thee a place of hidyng.
“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
19 `For, lo! my witnesse is in heuene; and the knowere of my consience is in hiye places.
Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
20 A! my frendis, ful of wordis, myn iye droppith to God.
Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
21 And `Y wolde, that a man were demed so with God, as the sone of man is demed with his felowe.
iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
22 `For lo! schorte yeeris passen, and Y go a path, bi which Y schal not turne ayen.
“Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”

< Job 16 >