< Job 15 >

1 Forsothe Eliphat Themanytes answeride, and seide,
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 Whether a wise man schal answere, as spekynge ayens the wynd, and schal fille his stomac with brennyng, `that is, ire?
“Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
3 For thou repreuest hym bi wordis, which is not lijk thee, and thou spekist that, that spedith not to thee.
Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
4 As myche as is in thee, thou hast avoidid drede; and thou hast take awey preyeris bifor God.
Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
5 For wickidnesse hath tauyt thi mouth, and thou suest the tunge of blasfemeris.
Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
6 Thi tunge, and not Y, schal condempne thee, and thi lippis schulen answere thee.
Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
7 Whether thou art borun the firste man, and art formed bifor alle little hillis?
“Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
8 Whether thou herdist the counsel of God, and his wisdom is lower than thou?
Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
9 What thing knowist thou, whiche we knowen not? What thing vndurstondist thou, whiche we witen not?
Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
10 Bothe wise men and elde, myche eldre than thi fadris, ben among vs.
Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
11 Whether it is greet, that God coumforte thee? But thi schrewid wordis forbeden this.
Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
12 What reisith thin herte thee, and thou as thenkynge grete thingis hast iyen astonyed?
Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
13 What bolneth thi spirit ayens God, that thou brynge forth of thi mouth siche wordis?
moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
14 What is a man, that he be with out wem, and that he borun of a womman appere iust?
“Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
15 Lo! noon among hise seyntis is vnchaungable, and heuenes ben not cleene in his siyt.
Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
16 How myche more a man abhomynable and vnprofitable, that drynkith wickidnesse as water?
nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
17 I schal schewe to thee, here thou me; Y schal telle to thee that, that Y siy.
“Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
18 Wise men knoulechen, and hiden not her fadris.
zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
19 To whiche aloone the erthe is youun, and an alien schal not passe bi hem.
(Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
20 A wickid man is proud in alle hise daies; and the noumbre of hise yeeris and of his tirauntrie is vncerteyn.
Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
21 The sown of drede is euere in hise eeris, and whanne pees is, he supposith euere tresouns.
Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
22 He bileueth not that he may turne ayen fro derknessis to liyt; and biholdith aboute on ech side a swerd.
Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
23 Whanne he stirith hym to seke breed, he woot, that the dai of derknessis is maad redi in his hond.
Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
24 Tribulacioun schal make hym aferd, and angwisch schal cumpas hym, as a kyng which is maad redi to batel.
Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
25 For he helde forth his hond ayens God, and he was maad strong ayens Almyyti God.
chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
26 He ran with neck reisid ayens God, and he was armed with fat nol.
Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
27 Fatnesse, that is, pride `comyng forth of temporal aboundaunce, hilide his face, `that is, the knowyng of vndurstondyng, and outward fatnesse hangith doun of his sidis.
“Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
28 He schal dwelle in desolat citees, and in deseert, `ethir forsakun, housis, that ben turned in to biriels.
munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
29 He schal not be maad riche, nether his catel schal dwelle stidefastli; nether he schal sende his roote in the erthe,
Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
30 nether he schal go awei fro derknessis. Flawme schal make drie hise braunchis, and he schal be takun a wey bi the spirit of his mouth.
Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
31 Bileue he not veynli disseyued bi errour, that he schal be ayenbouyt bi ony prijs.
Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
32 Bifor that hise daies ben fillid, he schal perische, and hise hondis schulen wexe drye;
Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
33 he schal be hirt as a vyne in the firste flour of his grape, and as an olyue tre castinge awei his flour.
Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
34 For the gaderyng togidere of an ipocrite is bareyn, and fier schal deuoure the tabernaclis of hem, that taken yiftis wilfuli.
Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
35 He conseyuede sorewe, and childide wickidnesse, and his wombe makith redi tretcheries.
Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”

< Job 15 >