< Job 10 >

1 Yt anoieth my soule of my lijf; Y schal lete my speche ayens me, Y schal speke in the bitternesse of my soule.
“Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
2 Y schal seie to God, Nyle thou condempne me; schewe thou to me, whi thou demest me so.
Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
3 Whether it semeth good to thee, if thou `falsli chalengist and oppressist me, the werk of thin hondis; and if thou helpist the counsel of wickid men?
Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
4 Whethir fleischli iyen ben to thee, ethir, as a man seeth, also thou schalt se?
Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
5 Whether thi daies ben as the daies of man, and `thi yeeris ben as mannus tymes;
Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
6 that thou enquere my wickidnesse, and enserche my synne?
kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
7 And wite, that Y haue do no `wickid thing; sithen no man is, that may delyuere fro thin hond?
ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
8 Thin hondis han maad me, and han formed me al in cumpas; and thou castist me doun so sodeynli.
“Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
9 Y preye, haue thou mynde, that thou madist me as cley, and schalt brynge me ayen in to dust.
Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
10 Whether thou hast not mylkid me as mylk, and hast cruddid me togidere as cheese?
Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
11 Thou clothidist me with skyn and fleisch; thou hast ioyned me togidere with boonys and senewis.
Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
12 Thou hast youe lijf and mercy to me, and thi visiting hath kept my spirit.
Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
13 Thouy thou helist these thingis in thin herte, netheles Y woot, that thou hast mynde of alle thingis.
“Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
14 If Y dide synne, and thou sparidist me at an our; whi suffrist thou not me to be cleene of my wickidnesse?
Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
15 And if Y was wickid, wo is to me; and if Y was iust, Y fillid with turment and wretchidnesse `schal not reise the heed.
Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
16 And if Y reise `the heed for pride, thou schalt take me as a lionesse; and thou turnest ayen, and turmentist me wondirli.
Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
17 Thou gaderist in store thi witnessis ayens me, and thou multipliest thin yre, `that is, veniaunce, ayens me; and peynes holden knyythod in me.
Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
18 Whi hast thou led me out of the wombe? `And Y wolde, that Y were wastid, lest an iye `schulde se me.
“Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
19 That Y hadde be, as if Y were not, and `were translatid, ethir borun ouer, fro the wombe to the sepulcre.
Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
20 Whether the fewnesse of my daies schal not be endid in schort? Therfor suffre thou me, that Y biweile `a litil my sorewe,
Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
21 bifor that Y go, and turne not ayen, to the derk lond, and hilid with the derknesse of deth, to the lond of wrecchidnesse and of derknessis;
ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
22 where is schadewe of deeth, and noon ordre, but euerlastynge hidousnesse dwellith.
ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”

< Job 10 >