< Jeremiah 48 >

1 To Moab the Lord of oostis, God of Israel, seith these thingis. Wo on Nabo, for it is destried, and schent; Cariathiarym is takun, the stronge citee is schent, and tremblide.
Ponena za Mowabu: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa. Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa; linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.
2 And ful out ioiyng is no more in Moab, thei thouyten yuel ayens Esebon. Come ye, and leese we it fro folk. Therfor thou beynge stille, schalt be stille, and swerd schal sue thee.
Palibenso amene akutamanda Mowabu; ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa: ‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’ Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete; ankhondo adzakupirikitsani.
3 A vois of cry fro Oronaym, distriynge, and greet sorewe.
Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu. Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’
4 Moab is defoulid, telle ye cry to litil children therof.
Mowabu wawonongeka; ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.
5 For a man wepynge stiede with wepyng bi the stiyng of Luyth, for in the comyng doun of Oronaym enemyes herden the yellyng of sorewe.
Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti, akulira kwambiri pamene akupita. Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka pa njira yotsikira ku Horonaimu.
6 Fle ye, saue ye youre lyues; and ye schulen be as bromes in desert.
Thawani! Dzipulumutseni; khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.
7 For that that thou haddist trist in thi strengthis, and in thi tresouris, also thou schalt be takun. And Chamos schal go in to passyng ouer, the preestis therof and the princes therof togidere.
Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu, nanunso mudzatengedwa ukapolo, ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.
8 And a robbere schal come to ech citee, and no citee schal be sauyd; and valeis schulen perische, and feeldi places schulen be distried, for the Lord seide.
Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse, ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke. Chigwa chidzasanduka bwinja ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa monga Yehova wayankhulira.
9 Yyue ye the flour of Moab, for it schal go out flourynge; and the citees therof schulen be forsakun, and vnhabitable.
Mtsineni khutu Mowabu chifukwa adzasakazika; mizinda yake idzasanduka mabwinja, wopanda munthu wokhalamo.
10 He is cursid, that doith the werk of God gilefuli; and he is cursid, that forbedith his swerd fro blood.
“Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika! Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!
11 Moab was plenteuouse fro his yong wexynge age, and restide in hise drastis, nether was sched out fro vessel in to vessel, and yede not in to passyng ouer; therfor his taaste dwellide in hym, and his odour is not chaungid.
“Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake, ngati vinyo wokhazikika pa masese ake, osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina; iye sanatengedwepo ukapolo. Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja ndipo fungo lake silinasinthe.
12 Therfor lo! daies comun, seith the Lord, and Y schal sende to it ordeynours, and arayeris of potels; and thei schulen araye it, and thei schulen waste the vessels therof, and hurtle togidere the potels of hem.
Nʼchifukwa chake masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko ndipo adzamukhutula; adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.
13 And Moab schal be schent of Chamos, as the hous of Israel was schent of Bethel, in which it hadde trist.
Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi, monga momwe Aisraeli anachitira manyazi ndi Beteli amene ankamukhutulira.
14 Hou seien ye, We ben stronge, and stalworthe men to fiyte?
“Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali. Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’
15 Moab is distried, and thei han brent the citees therof, and the chosun yonge men therof yeden doun in to sleynge, seith the kyng, the Lord of oostis is his name.
Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake; anyamata ake okongola apita kukaphedwa,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 The perischyng of Moab is nyy, that it come, and the yuel therof renneth ful swiftli.
Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi; masautso ake akubwera posachedwa.
17 Alle ye that ben in the cumpas therof, coumforte it; and alle ye that knowen the name therof, seie, Hou is the stronge yerde brokun, the gloriouse staaf?
Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira, inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake; nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija, taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”
18 Thou dwellyng of the douytir of Dibon, go doun fro glorie, sitte thou in thirst; for the distriere of Moab schal stie to thee, and he schal destrie thi strengthis.
“Tsikani pa ulemerero wanu ndipo khalani pansi powuma, inu anthu okhala ku Diboni, pakuti wowononga Mowabu wabwera kudzamenyana nanu, wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.
19 Thou dwellyng of Aroer, stonde in the weie, and biholde; axe thou hym that fleeth, and hym that ascapide; seie thou, What bifelle?
Inu amene mumakhala ku Aroeri, imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera. Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka, afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’”
20 Moab is schent, for he is ouercomun; yelle ye, and crye; telle ye in Arnon, that Moab is destried.
Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika. Lirani mwachisoni ndipo fuwulani! Lengezani ku mtsinje wa Arinoni kuti Mowabu wawonongedwa.
21 And doom is comun to the lond of the feeld, on Elon, and on Jesa, and on Mephat, and on Dibon,
Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri, ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,
22 and on Nabo, and on the hous of Debalthaym,
Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,
23 and on Cariathiarym, and on Bethgamul, and on Bethmaon, and on Scarioth,
Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,
24 and on Bosra, and on alle the citees of the lond of Moab, that ben fer, and that ben niy.
Keriyoti ndi Bozira ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.
25 The horn of Moab is kit awei, and the arm therof is al to-brokun, seith the Lord.
Mphamvu za Mowabu zawonongeka; mkono wake wathyoka,” akutero Yehova.
26 Fille ye him greetli, for he is reisid ayens the Lord; and he schal hurtle doun the hond of Moab in his spuyng, and he also schal be in to scorn.
“Muledzeretseni Mowabu, chifukwa anadzikuza powukira Yehova. Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake; mulekeni akhale chinthu chomachiseka.
27 For whi, Israel, he was in to scorn to thee, as if thou haddist founde hym among theues; therfor for thi wordis whiche thou spakist ayens hym, thou schalt be led prisoner.
Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka? Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba kuti nthawi zonse poyankhula za iye, iwe uzimupukusira mutu momunyoza?
28 Ye dwelleris of Moab, forsake citees, and dwelle in the stoon, and be ye as a culuer makynge nest in the hiyeste mouth of an hool.
Inu amene mumakhala ku Mowabu, siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe. Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake pa khomo la phanga.
29 We han herd the pride of Moab; he is ful proud.
“Tamva za kunyada kwa Mowabu, kunyada kwake nʼkwakukulu. Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula. Ali ndi mtima wodzikweza.
30 Y knowe, seith the Lord, the hiynesse therof, and pride in word, and pride in beryng, and the hiynesse of herte, and the boost therof, and that the vertu therof is not niy, ethir lijk it, nethir it enforside to do bi that that it miyte.
Ine ndikuzidziwa ntchito zake, akutero Yehova. Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.
31 Therfor Y schal weile on Moab, and Y schal crie to al Moab, to the men of the erthene wal, that weilen.
Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu, ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu, ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.
32 Of the weilyng of Jaser Y schal wepe to thee, thou vyner of Sabama; thi siouns passiden the see, tho camen `til to the see of Jazer; a robbere felle in on thi ripe corn, and on thi vyndage.
Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri. Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja; zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri. Wowononga wasakaza zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.
33 Ful out ioye and gladnesse is takun awei fro Carmele, and fro the lond of Moab, and Y haue take awei wyn fro pressouris; a stampere of grape schal not synge a customable myri song.
Chimwemwe ndi chisangalalo zatha ku minda ya zipatso ya ku Mowabu. Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa; palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa. Ngakhale kufuwula kulipo, koma sikufuwula kwa chimwemwe.
34 Of the cry of Esebon `til to Eleale and Jesa thei yauen her vois, fro Segor `til to Oronaym a cow calf of thre yeer; forsothe the watris of Nemrym schulen be ful yuele.
“A ku Hesiboni ndi Eleali akulira ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi, kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya. Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.
35 And Y schal take awei fro Moab, seith the Lord, him that offrith in hiy places, and him that makith sacrifice to the goddis therof.
Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,” akutero Yehova.
36 Therfor myn herte schal sowne as a pipe of bras to Moab, and myn herte schal yyue sown of pipis to the men of the erthene wal; for it dide more than it myyte, therfor thei perischiden.
“Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro. Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro chifukwa chuma chimene anachipata chatha.
37 For whi ech heed schal be ballidnesse, and ech beerd schal be schauun; in alle hondis schal be bindyng togidere, and an heir schal be on ech bak.
Aliyense wameta mutu wake ndi ndevu zake; manja a munthu aliyense ndi ochekacheka, ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.
38 And al weilyng schal be on alle the roouys of Moab, and in the stretis therof, for Y haue al to-broke Moab as an vnprofitable vessel, seith the Lord.
Pa madenga onse a ku Mowabu ndiponso mʼmisewu yake anthu akungolira, pakuti ndaphwanya Mowabu ngati mtsuko wopanda ntchito,” akutero Yehova.
39 Hou is it ouercomun, and thei yelliden? hou hath Moab cast doun the nol, and is schent? And Moab schal be in to scorn, and in to ensaumple to alle men in his cumpas.
“Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira! Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi. Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka, chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”
40 The Lord seith these thingis, Lo! as an egle he schal fle out, and he schal stretche forth hise wyngis to Moab.
Yehova akuti, “Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
41 Carioth is takun, and stronge holdis ben takun; and the herte of stronge men of Moab schal be in that dai, as the herte of a womman trauelynge of child.
Mizinda idzagwidwa ndipo malinga adzalandidwa. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
42 And Moab schal ceesse to be a puple, for it hadde glorie ayens the Lord.
Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu chifukwa unadzikuza powukira Yehova.
43 Drede, and diche, and snare is on thee, thou dwellere of Moab, seith the Lord.
Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira inu anthu a ku Mowabu,” akutero Yehova.
44 He that fleeth fro the face of drede, schal falle in to a diche; and thei that stien fro the dyche, schulen be takun with a snare. For Y schal brynge on Moab the yeer of the visitacioun of hem, seith the Lord.
“Aliyense wothawa zoopsa adzagwera mʼdzenje, aliyense wotuluka mʼdzenje adzakodwa mu msampha. Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu pa nthawi ya chilango chake,” akutero Yehova.
45 Men fleynge fro the snare stoden in the schadewe of Esebon, for whi fier yede out of Esebon, and flawme fro the myddis of Seon; and deuouride a part of Moab, and the cop of the sones of noise.
“Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni chifukwa chotopa. Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni, malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni. Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu, dziko la anthu onyada.
46 Moab, wo to thee; thou puple of Chamos, hast perischid, for whi thi sones and thi douytris ben takun in to caitiftee.
Tsoka kwa iwe Mowabu! Anthu opembedza Kemosi awonongeka. Ana ako aamuna ndi aakazi atengedwa ukapolo.
47 And Y schal conuerte the caitiftee of Moab in the laste daies, seith the Lord. Hidur to ben the domes of Moab.
“Komabe masiku akutsogolo ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,” akutero Yehova. Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.

< Jeremiah 48 >