< Jeremiah 45 >
1 The word that Jeremye, the profete, spak to Baruc, the sone of Nerie, whanne he hadde write these wordis in the book, of the mouth of Jeremye, in the fourthe yeer of Joachym, the sone of Josie, kyng of Juda,
Uwu ndi uthenga umene mneneri Yeremiya anawuza Baruki mwana wa Neriya mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa mwana ya Yosiya kuti alembe mʼbuku.
2 and seide, The Lord God of Israel seith these thingis to thee, Baruc.
“Yehova Mulungu wa Israeli, akunena kwa iwe Baruki kuti:
3 Thou seidist, Wo to me wretche, for the Lord encreesside sorewe to my sorewe; Y trauelide in my weilyng, and Y foond not reste.
Iwe unati, ‘Kalanga ine! Yehova wawonjezera chisoni pa mavuto anga. Ine ndatopa ndi kubuwula ndipo sindikupeza mpumulo.’”
4 The Lord seith these thingis, Thus thou schalt seye to hym, Lo! Y distrie hem, whiche Y bildide, and Y drawe out hem, whiche Y plauntide, and al this lond.
Koma Yehova akukuwuza kuti, “Ndidzagwetsa chimene ndinamanga ndipo ndidzazula chimene ndinadzala. Ndidzachita zimenezi mʼdziko lonse.
5 And sekist thou grete thingis to thee? nyle thou seke, for lo! Y schal brynge yuel on ech man, seith the Lord, and Y schal yyue to thee thi lijf in to helthe, in alle places, to whiche euer places thou schalt go.
Kodi tsono ukudzifunira wekha zinthu zazikulu? Usadzifunire. Pakuti ndidzagwetsa mavuto pa anthu onse, koma ndidzasunga moyo wako kulikonse kumene ungadzapite.”