< Jeremiah 40 >

1 The word that was maad of the Lord to Jeremye, aftir that he was delyuered of Nabusardan, maister of chyualrie, fro Rama, whanne he took hym boundun with chaynes, in the myddis of alle men that passiden fro Jerusalem, and fro Juda, and weren led in to Babyloyne.
Yehova anayankhula ndi Yeremiya pamene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anamasula Yeremiyayo ku Rama. Anamupeza Yeremiya ali womangidwa ndi unyolo pamodzi ndi amʼndende ena onse a ku Yerusalemu ndi a ku Yuda amene ankapita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
2 Therfor the prince of chyualrie took Jeremye, and seide to hym, Thi Lord God spak this yuel on this place,
Mtsogoleriyu anamupeza Yeremiya, anamuwuza kuti, “Yehova Mulungu wako analengeza kale zakuti malo ano adzawonongedwa.
3 and the Lord hath brouyt, and hath do, as he spak; for ye synneden to the Lord, and herden not the vois of hym, and this word is doon to you.
Ndipo tsopano Yehova wachitadi zimenezi monga mmene ananenera. Izi zonse zachitika chifukwa anthu inu munachimwira Yehova ndipo simunamumvere.
4 Now therfor lo! Y haue releessid thee to dai fro the chaynes that ben in thin hondis; if it plesith thee to come with me in to Babiloyne, come thou, and Y schal sette myn iyen on thee; sotheli if it displesith thee to come with me in to Babiloyne, sitte thou here; lo! al the lond is in thi siyt, that that thou chesist, and whidur it plesith thee to go, thidur go thou,
Koma tsopano taona, lero ndikukumasula unyolo umene unali mʼmanja mwako. Ngati ukufuna kupita nane ku Babuloni, tiye ndipo adzakusamala bwino. Koma ngati sukufuna kupita, ndiye usapite. Dziko ndi limeneli monga ukulioneramo. Uli ndi ufulu kupita kulikonse kumene ukufuna.”
5 and nyle thou come with me. But dwelle thou with Godolie, sone of Aicham, sone of Saphan, whom the kyng of Babiloyne made souereyn to the citees of Juda; therfor dwelle thou with hym in the myddis of the puple, ether go thou, whidir euer it plesith thee to go. And the maister of chyualrie yaf to hym metis, and yiftis, and lefte hym.
Yeremiya asanayankhe, Nebuzaradani anamuwuzanso kuti, “Ngati supita ndiye pita, ubwerere kwa Gedaliya, mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani, amene mfumu ya ku Babuloni inamusankha kuti akhale bwanamkubwa wa Yuda. Ukakhale naye pakati pa anthu, kapena upite kulikonse ukufuna.” Ndipo mtsogoleri uja anamupatsa Yeremiya chakudya ndi mphatso zina ndi kumulola kuti apite.
6 Forsothe Jeremye cam to Godolie, sone of Aicham, in to Masphat, and dwellide with hym, in the myddis of the puple that was left in the lond.
Motero Yeremiya anapita kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu ku Mizipa ndipo anakakhala naye kumeneko pakati pa anthu amene anatsala mʼdzikomo.
7 And whanne alle princes of the oost hadden herd, that weren scatered bi cuntreis, thei and the felowis of hem, that the kyng of Babiloyne hadde maad Godolie souereyn of the lond, the sone of Aicham, and that he hadde bitake to Godolie men, and wymmen, and litle children, and of pore men of the lond, that weren not translatid in to Babiloyne,
Panali atsogoleri ena a nkhondo ndi anthu awo amene sanadzipereke nawo. Iwowa anamva kuti mfumu ya ku Babuloni inasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu kukhala bwanamkubwa wa dzikolo ndipo kuti yamuyika kukhala wolamulira amuna, akazi ndi ana amene anali osauka kwambiri mʼdzikomo, amene sanawagwire ukapolo kupita nawo ku Babuloni.
8 thei camen to Godolie in Masphat; and Ismael, the sone of Nathanye, and Johannan, the sone of Caree, and Jonathan, and Sareas, the sone of Tenoemeth, and the sones of Offi, that weren of Nethophati, and Jeconye, the sone of Machati; bothe thei and her men camen to Godolie.
Iwowa anapita ku Mizipa kwa Gedaliya. Amene anapitawo ndi awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani ndi Yonatani ana a Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti, ana a Efai a ku Netofa, ndi Yezaniya mwana wa Maaka, iwowo pamodzi ndi anthu awo.
9 And Godolie, sone of Aicham, sone of Saphan, swoor to hem, and to the felowis of hem, and seide, Nyle ye drede to serue Caldeis; but dwelle ye in the lond, and serue ye the kyng of Babiloyne, and it schal be wel to you.
Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani, anawalonjeza iwo pamodzi ndi anthuwo mwalumbiro. Ndipo anati, “Musaope kuwatumikira Ababuloni. Khalani mʼdziko muno, tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
10 Lo! Y dwelle in Mesphath, for to answere to the comaundement of Caldeis, that ben sent to vs; forsothe gadere ye vyndage, and ripe corn, and oile, and kepe ye in youre vessels, and dwelle ye in youre citees whiche ye holden.
Ine ndidzakhala ku Mizipa kuti ndizikuyimirirani kwa Ababuloni amene azidzabwera kwa ife, koma inu muzikolola vinyo wanu, zipatso zanu, mafuta anu ndi kuzisunga mʼmitsuko yanu, nʼkumakhala mʼmizinda imene mwalandayo.”
11 But also alle the Jewis, that weren in Moab, and in the oostis of Amon, and in Ydumee, and in alle the cuntreis, whanne it is herd, that the kyng of Babiloyne hadde youe residues, ether remenauntis, in Judee, and that he hadde maad souereyn on hem Godolie, the sone of Aicham, sone of Saphan,
Nawonso Ayuda onse a ku Mowabu, ku Amoni, ku Edomu ndi a ku mayiko ena onse anamva kuti mfumu ya ku Babuloni inasiyako anthu ena ku Yuda ndipo kuti inasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala bwanamkubwa wawo.
12 sotheli alle Jewis turneden ayen fro alle places, to whiche thei hadden fled; and thei camen in to the lond of Juda, to Godolie in Masphat, and gaderiden wyn and ripe corn ful myche.
Tsono Ayuda onsewo anabwerera ku Yuda, ku Mizipa kwa Gedaliya, kuchokera ku mayiko onse kumene anabalalikira. Ndipo anakolola zipatso zochuluka ndi vinyo wambiri.
13 Forsothe Johannan, the sone of Caree, and alle the princes of the oost, that weren scaterid in the cuntreis, camen to Godolie in Masphath,
Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri a ankhondo onse amene sanadzipereke aja anabwera ku Mizipa kwa Gedaliya
14 and seiden to hym, Wite thou, that Bahalis, kyng of the sones of Amon, hath sent Ismael, the sone of Nathanye, to smyte thi lijf. And Godolie, the sone of Aicham, bileuyde not to hem.
ndipo anamufunsa kuti, “Kodi sukudziwa kuti Baalisi mfumu ya Aamoni watuma Ismaeli mwana wa Netaniya kuti akuphe?” Koma Gedaliya mwana wa Ahikamu sanawankhulupirire.
15 Forsothe Johannan, the sone of Caree, seide to Godolie asidis half in Masphath, and spak, Y schal go, and sle Ismael, the sone of Nathanye, while no man knowith, lest he sle thi lijf, and alle the Jewis ben scatered, that ben gaderid to thee, and the remenauntis of Juda schulen perische.
Tsono Yohanani mwana wa Kareya, mwamseri anawuza Gedaliya ku Mizipa kuti, “Loleni ndipite ndikaphe Ismaeli mwana wa Netaniya, ndipo palibe amene ati adziwe. Akuphereninji ndi kuchititsa Ayuda onse, amene akuzungulirani kuti abalalike ndi kuti otsala a ku Yuda awonongeke?”
16 And Godolie, the sone of Aicham, seide to Johannan, the sone of Caree, Nyle thou do this word, for thou spekist fals of Ismael.
Koma Gedaliya mwana wa Ahikamu anawuza Yohanani mwana wa Kareya kuti, “Usachite zimenezo! Zimene ukunena za Ismaeli ndi zabodza.”

< Jeremiah 40 >