< Jeremiah 32 >

1 The word that was maad of the Lord to Jeremye, in the tenthe yeer of Sedechie, kyng of Juda; thilke is the eiytenthe yeer of Nabugodonosor.
Yehova anayankhula ndi Yeremiya mʼchaka chakhumi cha Zedekiya mfumu ya Yuda, chimene chinalinso chaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara.
2 Thanne the oost of the kyng of Babiloyne bisegide Jerusalem; and Jeremye, the profete, was closid in the porche of the prisoun, that was in the hous of the kyng of Juda.
Pa nthawi imeneyi nʼkuti ankhondo a mfumu ya ku Babuloni atazinga Yerusalemu, ndipo mneneri Yeremiya ndiye anamutsekera mʼbwalo la alonda mʼnyumba yaufumu ya ku Yuda.
3 For whi Sedechie, the kyng of Juda, hadde closid hym, and seide, Whi profesiest thou, seiynge, The Lord seith these thingis, Lo! Y schal yyue this citee in the hond of the kyng of Babyloyne, and he schal take it; and Sedechie,
Tsono Zedekiya mfumu ya Yuda nʼkuti itamutsekera mʼmenemo, ndipo inati, “Nʼchifukwa chiyani ukulosera motero? Iwe ukunena kuti, ‘Yehova akuti: Ndidzapereka mzinda uno kwa mfumu ya ku Babuloni, ndipo idzawulanda.
4 the kyng of Juda, schal not ascape fro the hond of Caldeis, but he schal be bitake in to the hond of the kyng of Babiloyne; and his mouth schal speke with the mouth of hym, and hise iyen schulen se the iyen of hym;
Zedekiya mfumu ya Yuda sidzapulumuka mʼmanja mwa Ababuloni, koma idzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni. Adzayankhula naye ndi kuonana naye maso ndi maso.
5 and he schal lede Sedechie in to Babiloyne, and he schal be there, til Y visyte hym, seith the Lord; forsothe if ye fiyten ayens Caldeis, ye schulen haue no thing in prosperite?
Zedekiya adzatengedwa kupita naye ku Babuloni, kumene adzakhale mpaka nditamukhawulitsa, akutero Yehova. Ngakhale iye adzamenyane ndi Babuloni, koma sadzapambana.’”
6 And Jeremye seide, The word of the Lord was maad to me, and seide, Lo!
Yeremiya anati, “Yehova wandiwuza kuti:
7 Ananeel, the sone of Sellum, the sone of thi fadris brothir, schal come to thee, and seie, Bi thou to thee my feeld, which is in Anathot; for it bifallith to thee by niy kynrede, that thou bie it.
Taonani, Hanameli mwana wa Salumu, amalume ako akubwera ndipo adzakuwuza kuti, ‘Gula munda wanga wa ku Anatoti, chifukwa iwe ndiwe mʼbale wanga ndipo ndiwe woyenera kuwuwombola.’”
8 And Ananeel, the sone of my fadris brothir, cam to me, bi the word of the Lord, to the porche of the prisoun, and seide to me, Welde thou my feeld, which is in Anathot, in the lond of Beniamyn; for whi the erytage bifallith to thee, and thou art the next of blood, that thou welde it. Forsothe Y vndirstood, that it was the word of the Lord.
Ndipo monga momwe Yehova ananenera, Hanameli, msuweni wanga anabweradi ku bwalo la alonda ndipo anati, “Gula munda wanga wa ku Anatoti mʼdziko la Benjamini. Popeza ndiwe woyenera kuwugula ndi kukhala wako, gula munda umenewu kuti ukhale wako.” “Ine ndinadziwa kuti amenewa anali mawu a Yehova aja;
9 And Y bouyte the feeld, which is in Anathot, of Ananeel, the sone of my fadris brothir. And Y paiede to hym siluer, seuene stateris, and ten platis of siluer;
choncho ndinagula munda wa ku Anatoti kwa Hanameli msuweni wanga, ndipo ndinamupatsa masekeli asiliva 17.
10 and Y wroot in a book, and Y seelide, and Y yaf witnessis. And Y weiede siluer in a balaunce;
Ndinasayina panganolo ndikulimata pamaso pa mboni, kenaka ndinayeza ndalama zasilivazo pa sikelo.”
11 and Y took the book aseelid of possessioun, and axingis and answerys of the seller and bier, and couenauntis, and seelis withoutforth.
Pambuyo pake ndinatenga makalata anga a pangano, imodzi yomatidwa mʼmene munali malamulo onse a panganolo ndi ina yosamatidwa.
12 And Y yaf the book of possessioun to Baruc, the sone of Neri, sone of Maasie, bifore the iyen of Ananeel, the sone of my fadris brother, and bifore the iyen of witnessis that weren writun in the book of biyng, bifore the iyen of alle Jewis, that saten in the porche of the prisoun.
Ndinapereka makalatawo kwa Baruki mwana wa Neriya, mdzukulu wa Maseya pamaso pa Hanameli msuweni wanga, pamaso pa mboni zimene zinasayina panganoli ndiponso pamaso pa Ayuda onse okhala mʼbwalo la alonda.
13 And Y comaundide to Baruc bifore hem,
“Ndinamulangiza Baruki pamaso pa onsewo kuti,
14 and Y seide, The Lord of oostis, God of Israel, seith these thingis, Take thou these bookis, this seelid book of biyng, and this book which is opyn, and putte thou tho in an erthen vessel, that tho moun dwelle bi many daies.
‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Tenga makalata awa a umboni wapangano, iyi yokhala ndi chizindikiro ndi yopanda chizindikiro, uwasunge mʼmbiya kuti akhale nthawi yayitali.
15 For whi the Lord of oostis, God of Israel, seith these thingis, Yit housis, and feeldis, and vynes schulen be weldid in this lond.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Anthu adzagulanso nyumba, minda ndi mitengo yamphesa mʼdziko lino.’”
16 And Y preiede to the Lord, aftir that Y bitook the book of possessioun to Baruc, the sone of Nery; and Y seide, Alas!
Nditamupatsa makalata a panganowa Baruki mwana wa Neriya, ndinapemphera kwa Yehova:
17 alas! alas! Lord God, Lord, thou madist heuene and erthe in thi greet strengthe, and in thin arm stretchid forth; ech word schal not be hard to thee;
“Aa, inu Ambuye Yehova, munalenga dziko lakumwamba ndi dziko lapansi. Munazilenga ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo palibe chokulakani.
18 which doist merci in thousyndis, and yeldist the wickidnesse of fadris in to the bosum of her sones aftir hem. Thou strongeste, greet, myyti, Lord of oostis is name to thee;
Mumaonetsa chikondi chanu kwa anthu osawerengeka koma mumalanga ana chifukwa cha machimo a makolo awo. Inu ndinu Mulungu Wamkulu ndi Wamphamvu. Dzina lanu ndinu Yehova Wamphamvuzonse.
19 greet in councel, and vncomprehensible in thouyt, whose iyen ben open on alle the weies of the sones of Adam, that thou yelde to ech aftir hise weies, and aftir the fruyt of hise fyndyngis;
Zolinga zanu ndi zazikulu ndipo zochita zanu ndi zamphamvu. Maso anu amaona zonse zimene anthu amachita. Mumapereka mphotho kwa munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndi ntchito zake.
20 which settidist signes and greet woundris in the lond of Egipt, `til to this dai, bothe in Israel and in men; and madist to thee a name, as this dai is.
Inu munachita zizindikiro zozizwitsa ku Igupto, ndipo mwakhala mukuzichita mpaka lero, pakati pa Aisraeli ndiponso pakati pa anthu onse. Choncho mwadzitchukitsa mpaka lero lino.
21 And thou leddist thi puple Israel out of the lond of Egipt, in signes and in greet woundris, and in a strong hond, and in an arm holdun forth, and in greet dreed; and thou yauest to hem this lond,
Munatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu pochita zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene zinaopseza adani anu.
22 which thou sworist to the fadris of hem, that thou woldist yyue to hem, a lond flowynge with milk and hony.
Munawapatsa dziko lino limene munalonjeza mwalumbiro kulipereka kwa makolo awo, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
23 And thei entriden, and hadden it in possessioun; and thei obeieden not to thi vois, and thei yeden not in thi lawe; alle thingis whiche thou comaundidist to hem to do, thei diden not; and alle these yuels bifellen to hem.
Iwo analowa nʼkulitenga kukhala lawo, koma sanamvere Inu kapena kutsatira lamulo lanu; ndipo sanachite zomwe munawalamula. Choncho inu mwawagwetsera masautso onsewa.”
24 Lo! strengthis ben bildid ayens the citee, that it be takun, and the citee is youun in to the hondis of Caldeis, and in to the hondis of the kyng of Babiloyne, that fiyten ayens it, of the face of swerd, and of hungur, and of pestilence; and what euer thingis thou spakest, bifellen, as thou thi silf seest.
“Onani momwe adani azingira ndi mitumbira yankhondo mzindawu kuti awulande ndipo akuwuthira nkhondo. Chifukwa cha lupanga, njala ndi mliri. Mzindawu udzaperekedwa kwa Ababuloni anthu atafowoka ndi nkhondo, njala ndi mliri. Zimene munkanena zija zachitikadi monga mukuzionera tsopano.
25 And Lord God, thou seist to me, Bie thou a feeld for siluer, and yyue thou witnessis, whanne the citee is youun in the hondis of Caldeis.
Ngakhale mzindawu udzaperekedwa kwa Ababuloni, komabe Inu Ambuye Yehova, munandiwuza kuti, ‘Gula munda ndi siliva ndipo upereke ndalamazo pali mboni.’”
26 And the word of the Lord was maad to Jeremye, and seide, Lo!
Tsono Yehova anawuza Yeremiya kuti,
27 Y am the Lord God of `al fleisch. Whether ony word schal be hard to me?
“Taonani, Ine ndine Yehova, Mulungu wa anthu onse. Kodi chilipo chinthu choti Ine nʼkundikanika?
28 Therfor the Lord seith these thingis, Lo! Y schal bitake this citee in to the hondis of Caldeis, and in to the hond of the kyng of Babiloyne, and he schal take it.
Nʼchifukwa chake ine Yehova ndikuti: Ndidzawupereka mzinda uno kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulanda.
29 And Caldeis schulen come, and fiyte ayens this citee, and thei schulen brenne it with fier, and thei schulen brenne it, and housis, in whose rooues thei sacrifieden to Baal, and offriden moist sacrifices to alien goddis, to terre me to wraththe.
Ndipo Ababuloni amene akuwuthira nkhondo mzinda uno adzalowa ndi kuwutentha; adzatentha ndi kugwetsa nyumba zimene pa denga pake anthu ankandipsetsa mtima pofukiza lubani kwa Baala ndi popereka chopereka cha chakumwa kwa milungu ina.
30 For whi the sones of Israel and the sones of Juda diden yuel contynueli, fro her yonge waxynge age, bifore myn iyen, the sones of Israel, whiche `til to now wraththen me bi the werk of her hondis, seith the Lord.
“Aisraeli ndi Ayuda akhala akuchita zoyipa zokhazokha pamaso panga kuyambira ubwana wawo. Kunena zoona Aisraeli akumandikwiyitsa ndi ntchito zawo zoyipa, akutero Yehova.
31 For whi this citee is maad to me in my strong veniaunce and indignacioun, fro the day in which thei bildiden it, `til to this dai, in which it schal be takun awei fro my siyt;
Kuyambira tsiku limene mzindawu unamangidwa mpaka lero, wakhala ukuwutsa mkwiyo wanga ndi ukali wanga. Nʼchifukwa chake ndiyenera kuwuchotsa pamaso panga.
32 for the malice of the sones of Israel, and of the sones of Juda, which thei diden, terrynge me to wrathfulnesse, thei, and the kyngis of hem, the princes of hem, and the prestis, and profetis of hem, the men of Juda, and the dwelleris of Jerusalem.
Aisraeli ndi Ayuda, anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, mafumu awo, nduna zawo, ansembe ndi aneneri awo anandikwiyitsa ndi ntchito zawo zoyipa.
33 And thei turneden to me the backis, and not the faces, whanne Y tauyte, and enformede hem erli; and thei nolden here, that thei schulden take techyng.
Anandifulatira ndipo ngakhale ndinakhala ndikuwaphunzitsa kawirikawiri, sanamve kapena kuphunzirapo kanthu.
34 And thei settiden her idols in the hous, in which my name is clepid to help, that thei schulden defoule it.
Iwo anayika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi dzina langa ndipo anayipitsa.
35 And thei bildiden hiy thingis to Baal, that ben in the valei of the sones of Ennon, that thei schulden halewe her sones and her douytris to Moloc, which thing Y comaundide not to hem, nether it stiede in to myn herte, that thei schulden do this abhomynacioun, and brynge Juda in to synne.
Anamanga malo opembedzerapo Baala mʼChigwa cha Hinomu kuti aziperekapo ana awo aamuna ndi aakazi ngati nsembe kwa Moleki. Ine sindinawalamulire kutero, ndipo sindinaganizepo nʼkomwe kuti iwo angachite chinthu chonyansa chotero, ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda.
36 And now for these thingis, the Lord God of Israel seith these thingis to this citee, of whiche ye seien, that it schal be bitakun in to the hondis of the kyng of Babiloyne, in swerd, and in hungur, and in pestilence, Lo!
“Anthu ponena za mzindawu akuti udzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni mwa nkhondo, njala ndi mliri, koma Yehova Mulungu wa Israeli akuti,
37 Y schal gadere hem fro alle londis, to whiche Y castide hem out in my strong veniaunce, and in my wraththe, and in greet indignacioun; and Y schal brynge hem ayen to this place, and Y schal make hem to dwelle tristili.
Ine ndidzawasonkhanitsadi anthuwa kuchokera ku mayiko onse kumene ndinawapirikitsira ndili wokwiya ndi waukali kwambiri. Ndidzabwera nawo ku malo ano ndipo ndidzawalola kukhala mwamtendere.
38 And thei schulen be in to a puple to me, and Y schal be in to God to hem.
Iwo adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
39 And Y schal yyue to hem oon herte and o soule, that thei drede me in alle daies, and that it be wel to hem, and to her sones aftir hem.
Ndidzawapatsa mtima umodzi ndi khalidwe limodzi kotero kuti azidzandiopa nthawi zonse ndipo iwo pamodzi ndi zidzukulu zawo zinthu zidzawayendera bwino.
40 And Y schal smyte to hem a couenaunt euerlastynge, and Y schal not ceese to do wel to hem, and Y schal yyue my drede in the herte of hem, that thei go not awey fro me.
Ndidzachita nawo pangano losatha: sindidzaleka kuwachitira zabwino, ndipo ndidzawapatsa mtima woti azidzandiopa, kuti asadzandisiyenso.
41 And Y schal be glad on hem, whanne Y schal do wel to hem; and Y schal plaunte hem in this lond in treuthe, in al myn herte, and in al my soule.
Ndidzakondwera powachitira zabwino, ndipo ndidzawakhazikitsa ndithu mʼdziko lino ndi mtima wanga wonse ndi moyo wanga wonse.
42 For the Lord seith these thingis, As Y brouyte on this puple al this greet yuel, so Y schal brynge on hem al the good, which Y schal speke to hem.
“Yehova akuti: Monga momwe ndinagwetsera masautso aakulu onsewa pa anthuwa, momwemonso ndidzawapatsa zinthu zonse zabwino zimene ndinawalonjeza.
43 And feeldis schulen be weldid in this lond, of which ye seien, that it is desert, for no man and beeste is left; and it is youun in to the hondis of Caldeis.
Adzagulanso minda mʼdziko muno, limene inu mukuti, ‘Ndi dziko losiyidwa, lopanda anthu kapena nyama, pakuti linaperekedwa kwa Ababuloni.’
44 Feeldis schulen be bouyt for money, and schulen be writun in a book, and a seel schal be preentid; and witnessis schulen be youun, in the lond of Beniamyn, and in the cumpas of Jerusalem, and in the citees of Juda, and in the citees in hilli places, and in the citees in feeldi places, and in the citees that ben at the south; for Y schal turne the caitiftee of hem, seith the Lord.
Adzagula minda ndi ndalama zasiliva, ndipo achita pangano, ndi kumata pamaso pa mboni. Izi zidzachitika mʼdziko la Benjamini, ku malo ozungulira Yerusalemu, mʼmizinda ya Yuda, mʼmizinda ya ku mapiri, mʼmizinda ya kuchigwa ndi yakummwera ku Negevi. Zoona, ndidzabwezera ufulu wawo, akutero Yehova.”

< Jeremiah 32 >