< Jeremiah 26 >

1 In the bigynnyng of the rewme of Joachym, the sone of Josie, kyng of Juda, this word was maad of the Lord, and seide,
Yehoyakimu, mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda atayamba kulamulira, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 The Lord seide these thingis, Stonde thou in the porche of the hous of the Lord, and thou schalt speke to alle the citees of Juda, fro whiche thei comen for to worschipe in the hous of the Lord, alle the wordis whiche Y comaundide to thee, that thou speke to hem; nyle thou withdrawe a word;
“Kayime mʼbwalo la Nyumba ya Yehova. Ndipo ukayankhule kwa anthu onse okhala mʼmizinda ya ku Yuda amene amabwera kudzapembedza ku Nyumba ya Yehova. Ukawawuze zonse zomwe ndakulamula; usakasiyeko ndi mawu amodzi omwe.
3 if perauenture thei heren, and ben conuertid, ech man fro his yuele weie, and it repente me of the yuel which Y thouyte to do to hem for the malices of her studies.
Mwina mwake adzamvera, ndipo aliyense adzatembenuka kuleka njira yake yoyipa. Ndiye ine ndidzaleka osapatsa chilango chimene ndinakonzekera kuti ndiwalange nacho chifukwa cha ntchito zawo zoyipa.
4 And thou schalt seie to hem, The Lord seith these thingis, If ye heren not me, that ye go in my lawe which Y yaf to you,
Ukawawuze kuti, ‘Yehova akuti: Ngati simundimvera Ine ndi kuleka kutsatira malamulo anga, amene ndakupatsani,
5 that ye here the wordis of my seruauntis, profetis, whiche Y risynge bi niyte, and dressynge, sente to you, and ye herden not;
ndipo ngati simumvera mawu a atumiki anga, aneneri amene ndakhala ndikukutumizirani, ngakhale kuti simunawamvere,
6 Y schal yyue this hous as Silo, and Y schal yyue this citee in to cursyng to alle folkis of erthe.
ndiye kuti Ine ndidzasandutsa Nyumba ino kukhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.’”
7 And the prestis, and profetis, and al the puple herden Jeremye spekynge these wordis in the hous of the Lord.
Ansembe, aneneri ndi anthu onse anamva Yeremiya akuyankhula mawu amenewa mʼNyumba ya Yehova.
8 And whanne Jeremye hadde fillid spekynge alle thingis, whiche the Lord hadde comaundid to hym, that he schulde speke to al the puple, the prestis, and profetis, and al the puple token hym, and seiden, Die he bi deeth;
Yeremiya atangotsiriza kuwawuza anthu aja zonse zimene Yehova anamulamula kuti ayankhule, ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse anamugwira ndipo anati, “Uyenera kuphedwa!
9 whi profesiede he in the name of the Lord, and seide, This hous schal be as Silo, and this citee schal be desolat, for no dwellere is? And al the puple was gaderid togidere ayens Jeremye, in the hous of the Lord.
Chifukwa chiyani walosera mʼdzina la Yehova kuti Nyumba ino idzakhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala wopanda anthu ngati chipululu?” Anthu onse anamuzungulira Yeremiya mʼNyumba ya Yehova.
10 And the princes of Juda herden alle these wordis; and thei stieden fro the kyngis hous in to the hous of the Lord, and saten in the entryng of the newe yate of the hous of the Lord.
Koma nduna za ku Yuda zitamva zomwe zinachitikazi, zinanyamuka kuchokera ku nyumba yaufumu kupita ku Nyumba ya Yehova, nakakhala pamalo pawo, pa Chipata Chatsopano cha Nyumba ya Yehova.
11 And the prestis and profetis spaken to the princes, and to al the puple, and seiden, Doom of deth is to this man, for he profesiede ayens this citee, as ye herden with youre eeris.
Pamenepo ansembe ndi aneneri anawuza ndunazo pamodzi ndi anthu onse kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa chifukwa amalosera zoyipira mzinda uno. Inu mwadzimvera nokha zimenezi!”
12 And Jeremye seide to alle the princes, and to al the puple, `and seide, The Lord sente me, that Y schulde prophesie to this hous, and to this citee, alle the wordis whiche ye herden.
Ndipo Yeremiya anawuza nduna zija ndi anthu onse kuti, “Yehova anandituma kunenera mawu onse amene mwawamva otsutsa Nyumba ino ndi mzinda uno.
13 Now therfor make ye good youre weies, and youre studies, and here ye the vois of youre Lord God; and it schal repente the Lord of the yuel which he spak ayens you.
Tsopano konzani njira zanu ndi zochita zanu ndipo mverani Yehova Mulungu wanu. Mukatero ndiye kuti Yehova adzaleka osakupatsani chilango chimene ankati akupatseni.
14 Lo! forsothe Y am in youre hondis; do ye to me, as it is good and riytful bifore youre iyen.
Kunena za ine, ndili mʼmanja mwanu; mundichite chilichonse chimene mukuganiza kuti ndi chabwino ndi choyenera.
15 Netheles wite ye, and knowe, that if ye sleen me, ye schulen bitraie innocent blood ayens you silf, and ayens this citee, and the dwelleris therof; for in trewthe the Lord sente me to you, that Y schulde speke in youre eeris alle these wordis.
Komatu dziwani kuti ngati mundipha, inu pamodzi ndi mzinda uno ndi onse amene amakhala muno, mudzapalamula mlandu wokhetsa magazi a munthu wosalakwa. Ndithudi Yehova anandituma kuti ndidzayankhule mawu onsewa inu mukumva.”
16 And the princes and al the puple seiden to the preestis and profetis, Doom of deth is not to this man; for he spak to vs in the name of oure Lord God.
Pamenepo ndunazo pamodzi ndi anthu onse anawuza ansembe ndi aneneri kuti, “Munthu uyu sayenera kuphedwa! Pakuti wayankhula kwa ife mʼdzina la Yehova Mulungu wathu.”
17 Therfor men of the eldere men of the lond rysiden vp, and seiden to al the cumpanye of the puple,
Akuluakulu ena a mʼdzikomo anayimirira ndi kuwuza gulu lonse la anthu kuti,
18 and spaken, Mychee of Morasten was a profete in the daies of Ezechie, king of Juda; and he seide to al the puple of Juda, and seide, The Lord of oostis seith these thingis, Sion schal be erid as a feeld, and Jerusalem schal be in to an heep of stoonys, and the hil of the hous of the Lord schal be in to hiy thingis of woodis.
“Mʼmasiku a Hezekiya mfumu ya ku Yuda, Mika wa ku Moreseti ankalosera. Iye ankawuza anthu kuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “‘Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.’
19 Whether Ezechie, kyng of Juda, and al Juda condempnede hym bi deth? Whether thei dredden not the Lord, and bisouyten the face of the Lord? and it repentide the Lord of the yuel which he spak ayens hem. Therfor do we not greet yuel ayens oure soulis.
Kodi Hezekiya mfumu ya ku Yuda ndi anthu onse anamupha amene uja? Kodi suja mfumu inaopa Yehova ndi kupempha kuti ayikomere mtima? Ndipo suja Yehova anasintha maganizo ake nʼkuleka kuwalanga monga mʼmene anakonzera? Ifetu tikudziyitanira tsoka lalikulu!”
20 Also Vrye, the sone of Semey, of Cariathiarym, was a man profesiynge in the name of the Lord; and he profesiede ayens this citee, and ayens this lond, bi alle the wordis of Jeremye.
(Panalinso munthu wina, Uriya mwana wa Semaya wa ku Kiriati-Yeyarimu, amene ankalosera mʼdzina la Yehova. Iyeyu analosera za mzinda uno ndi dziko lino monga mmene wachitira Yeremiya.
21 And kyng Joachym, and alle the myyti men, and princes of hem, herden these wordis; and the kyng souyte to sle hym; and Vrye herde, and dredde, and he fledde, and entride in to Egipt.
Mfumu Yehoyakimu, ankhondo ake onse ndi nduna zake anamva mawu akewo, ndipo anafuna kumupha. Koma Uriya atamva zimenezi, anachita mantha nathawira ku Igupto.
22 And kyng Joachym sente men in to Egipt, Elnathan, the sone of Achobor, and men with hym, in to Egipt;
Komabe Mfumu Yehoyakimu anatuma Elinatani mwana wa Akibori pamodzi ndi anthu ena, ku Igupto.
23 and thei ledden Vrye out of Egipt, and brouyten hym to kyng Joachym; and the kyng killide hym bi swerd, and castide forth his careyn in the sepulcris of the comyn puple vnnoble.
Iwo anakamutenga Uriya ku Igupto kuja nabwera naye kwa Mfumu Yehoyakimu. Iye anamupha ndi lupanga ndipo mtembo wake anakawutaya ku manda a anthu wamba).
24 Therfor the hond of Aicham, sone of Saphan, was with Jeremye, that he was not bitakun in to the hondis of the puple, and that it killide not hym.
Koma Ahikamu mwana wa Safani ndiye anateteza Yeremiya, motero sanamupereke kwa anthu kuti amuphe.

< Jeremiah 26 >