< Jeremiah 20 >

1 And Phassur, the sone of Emyner, the preest, that was ordeyned prince in the hous of the Lord, herde Jeremye profesiynge these wordis.
Wansembe Pasuri mwana wa Imeri, woyangʼanira wamkulu wa Nyumba ya Yehova, anamva Yeremiya akulosera zinthu zimenezi.
2 And Phassur smoot Jeremye, the profete, and sente hym in to the stockis, that weren in the hiyere yate of Beniamyn, in the hous of the Lord.
Tsono iye analamula kuti mneneri Yeremiyayo amenyedwe ndi kuyikidwa mʼndende pa Chipata chakumtunda kwa Benjamini ku Nyumba ya Yehova.
3 And whanne it was cleer in the morewe, Phassur ledde Jeremye out of the stockis. And Jeremye seide to hym, The Lord clepide not Phassur thi name, but Drede on ech side.
Mmawa mwake, Pasuri anatulutsa Yeremiya mʼndende, ndipo Yeremiyayo anamuwuza kuti, “Pasuri, Yehova sadzakutchulanso dzina lako kuti Pasuri koma Zoopsa pa Mbali Zonse.
4 For the Lord seith these thingis, Lo! Y schal yyue thee and alle thi freendis in to drede, and thei schulen falle doun bi the swerd of her enemyes; and thin iyen schulen se; and Y schal yyue al Juda in the hond of the king of Babiloyne, and he schal lede hem ouer in to Babiloyne, and he schal smyte hem bi swerd.
Pakuti Yehova akuti, ‘Ndidzakusandutsa choopsa kwa mwiniwakewe ndi kwa abwenzi ako onse; iweyo ukuona. Anthu a ku Yuda ndidzawapereka onse mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ena adzatengedwa ukapolo ku Babuloni ndipo ena adzaphedwa pa nkhondo.
5 And Y schal yyue al the catel of this citee, and al the trauel therof, and al the prijs; and Y schal yyue alle the tresours of the kingis of Juda in the hond of her enemyes; and thei schulen rauysche tho, and schulen take, and lede forth in to Babiloyne.
Ndidzapereka kwa adani awo chuma chonse cha mu mzinda uno, phindu lonse la ntchito yake, zinthu zake zonse za mtengowapatali ndiponso katundu yense wa mafumu a ku Yuda. Iwo adzazitenga monga zinthu zolanda ku nkhondo ndi kupita nazo ku Babuloni.
6 Forsothe thou, Phassur, and alle the dwelleris of thin hous, schulen go in to caitifte; and thou schalt come in to Babiloyne, and thou schalt die there; and thou schalt be biried there, thou and alle thi freendis, to whiche thou profesiedist a leesyng.
Ndipo iwe, Pasuri, pamodzi ndi onse a pa banja pako mudzapita ku ukapolo ku Babuloni. Mudzafera kumeneko ndi kuyikidwa mʼmanda, iweyo pamodzi ndi abwenzi ako amene unawalosera zabodza.’”
7 Lord, thou disseyuedist me, and Y am disseyued; thou were strongere than Y, and thou haddist the maistrie; Y am maad in to scorn al dai.
Inu Yehova, mwandinamiza, ndipo ndinapusadi; Inu ndi wamphamvu kuposa ine ndipo munandipambana. Anthu akundinyoza tsiku lonse. Aliyense akundiseka kosalekeza.
8 Alle men bymowen me, for now a while ago Y speke criynge wickidnesse, and Y criede distriynge. And the word of the Lord is maad to me in to schenschip, and in to scorn al dai.
Nthawi iliyonse ndikamayankhula, ndimafuwula kunena kuti, ziwawa kuno! Tikuwonongeka! Mawu anu Yehova andisandutsa chinthu chonyozeka ndipo ndimachitidwa chipongwe tsiku lonse.
9 And Y seide, Y schal not haue mynde on hym, and Y schal no more speke in his name. And the word of the Lord was maad, as fier swalynge in myn herte, and cloosid in my boonys; and Y failide, not suffryng to bere.
Koma ndikanena kuti, “Sindidzalalikiranso za Iye kapena kuyankhulanso mʼdzina lake,” mawu anu amayaka ngati moto mu mtima mwanga, amakhaladi ngati moto wotsekeredwa mʼmafupa anga. Ndapirira kusunga mawu anu mu mtima mwanga osawatulutsa, koma sindingathe kupirirabe.
10 For Y herde dispisyngis of many men, and drede in cumpas, Pursue ye, and pursue we hym, of alle men that weren pesible to me, and kepynge my side; if in ony maner he be disseyued, and we haue the maistrie ayens hym, and gete veniaunce of hym.
Ndimamva anthu ambiri akunongʼona kuti, “Zoopsa ku mbali zonse! Kamunenezeni! Tiyeni tikamuneneze!” Onse amene anali abwenzi anga akuyembekezera kuti ndigwa pansi, akumanena kuti, “Mwina mwake adzanyengedwa; tidzamugwira ndi kulipsira pa iye.”
11 Forsothe the Lord as a stronge werriour is with me, therfor thei that pursuen me schulen falle, and schulen be sijk; and thei schulen be schent greetli, for thei vndurstoden not euerlastynge schenschip, that schal neuere be don awei.
Koma Yehova ali nane, ndiye wankhondo wamphamvu. Nʼchifukwa chake ondizunza adzalephera ndipo sadzandipambana. Adzachita manyazi kwambiri chifukwa sadzapambana. Manyazi awo sadzayiwalika konse.
12 And thou, Lord of oostis, the preuere of a iust man, which seest the reynes and herte, Y biseche, se Y thi veniaunce of hem; for Y haue schewid my cause to thee.
Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumayesa anthu molungama ndipo mupenya za mu mtima mwa munthu. Ndiloleni kuti ndione kuti mwalipsira adani anga popeza ndapereka mlandu wanga kwa Inu.
13 Synge ye to the Lord, herie ye the Lord, for he delyueride the soule of a pore man fro the hond of yuel men.
Imbirani Yehova! Mutamandeni Yehova! Iye amapulumutsa wosauka mʼmanja mwa anthu oyipa.
14 Cursid be the dai where ynne Y was borun, the dai where ynne my modir childide me, be not blessid.
Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa! Tsiku limene amayi anga anandibereka lisatamandidwe!
15 Cursid be the man, that telde to my fadir, and seide, A knaue child is borun to thee, and made hym glad as with ioye.
Wotembereredwa munthu amene anapita kukasangalatsa abambo anga ndi uthenga woti: “Kwabadwa mwana wamwamuna!”
16 Thilke man be as the citees ben, whiche the Lord distriede, and it repentide not hym;
Munthu ameneyo akhale ngati mizinda imene Yehova anayiwononga mopanda chisoni. Amve mfuwu mmawa, phokoso la nkhondo masana.
17 he that killide not me fro the wombe, here cry eerli, and yellynge in the tyme of myddai; that my modir were a sepulcre to me, and hir wombe were euerlastinge conseyuyng.
Chifukwa sanandiphere mʼmimba, kuti amayi anga asanduke manda anga, mimba yawo ikhale yayikulu mpaka kalekale.
18 Whi yede Y out of the wombe, that Y schulde se trauel and sorewe, and that mi daies schulen be waastid in schenschipe?
Kodi ndinabadwira mavuto ndi chisoni kuti moyo wanga ukhale wamanyazi wokhawokha?

< Jeremiah 20 >