< Isaiah 54 >

1 Thou bareyn, that childist not, herie; thou that childist not, synge heriyng, and make ioie; for whi many sones ben of the forsakun `womman more than of hir that hadde hosebonde, seith the Lord.
“Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
2 Alarge thou the place of thi tente, and stretche forth the skynnes of thi tabernaclis; spare thou not, make longe thi roopis, and make sad thi nailis.
Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
3 For thou schalt perse to the riytside and to the leftside; and thi seed schal enherite hethene men, and schal dwelle in forsakun citees.
Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
4 Nile thou drede, for thou schal not be schent, nether thou schalt be aschamed. For it schal not schame thee; for thou schalt foryete the schenschipe of thi yongthe, and thou schalt no more thenke on the schenschipe of thi widewehod.
“Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
5 For he that made thee, schal be lord of thee; the Lord of oostis is his name; and thin ayenbiere, the hooli of Israel, schal be clepid God of al erthe.
Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
6 For the Lord hath clepid thee as a womman forsakun and morenynge in spirit, and a wijf, `that is cast awei fro yongthe.
Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
7 Thi Lord God seide, At a poynt in litil tyme Y forsook thee, and Y schal gadere thee togidere in greete merciful doyngis.
“Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
8 In a moment of indignacioun Y hidde my face a litil fro thee, and in merci euerlastynge Y hadde merci on thee, seide thin ayenbiere, the Lord.
Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
9 As in the daies of Noe, this thing is to me, to whom Y swoor, that Y schulde no more bringe watris of the greet flood on the erthe; so Y swoor, that Y be no more wrooth to thee, and that Y blame not thee.
“Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
10 Forsothe hillis schulen be mouyd togidere, and litle hillis schulen tremble togidere; but my merci schal not go a wei fro thee, and the boond of my pees schal not be mouyd, seide the merciful doere, the Lord.
Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
11 Thou litle and pore, drawun out bi tempest, with outen ony coumfort, lo! Y schal strewe thi stoonys bi ordre, and Y schal founde thee in safiris;
“Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
12 and Y schal sette iaspis thi touris, and thi yatis in to grauun stoonys, and alle thin eendis in to desirable stoonys.
Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
13 `Y schal make alle thi sones tauyt of the Lord; and the multitude of pees to thi sones,
Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
14 and thou schalt be foundid in riytfulnesse. Go thou awei fer fro fals caleng, for thou schalt not drede; and fro drede, for it schal not neiye to thee.
Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
15 Lo! a straunger schal come, that was not with me; he, that was sum tyme thi comelyng, schal be ioyned to thee.
Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
16 Lo! Y made a smyth blowynge coolis in fier, and bringynge forth a vessel in to his werk; and Y haue maad a sleere, for to leese.
“Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
17 Ech vessel which is maad ayens thee, schal not be dressid; and in the doom thou schalt deme ech tunge ayenstondynge thee. This is the eritage of the seruauntis of the Lord, and the riytfulnesse of hem at me, seith the Lord.
palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.

< Isaiah 54 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark