< Isaiah 52 >

1 Rise thou, Sion, rise thou, be thou clothid in thi strengthe; Jerusalem, the citee of the hooli, be thou clothid in the clothis of thi glorie; for a man vncircumcidid and a man vncleene schal no more leie to, that he passe by thee.
Dzambatuka, dzambatuka iwe Ziyoni, vala zilimbe. Vala zovala zako zokongola, iwe Yerusalemu, mzinda wopatulika. Pakuti kuyambira tsopano anthu osachita mdulidwe ndi odetsedwa sadzalowanso pa zipata zako.
2 Jerusalem, be thou schakun out of dust; rise thou, sitte thou; thou douyter of Sion, prisoner, vnbynde the boondis of thi necke.
Sasa fumbi lako; imirira nukhale pa mpando waufumu, iwe Yerusalemu. Inu omangidwa a ku Ziyoni, masulani maunyolo amene ali mʼkhosi mwanumo.
3 For the Lord seith these thingis, Ye ben seeld without cause, and ye schulen be ayenbouyt with out siluer.
Pakuti Yehova akuti, “Sindinalandirepo kanthu pamene ndinakugulitsani, choncho mudzawomboledwa wopanda ndalama.”
4 For the Lord God seith these thingis, Mi puple in the bigynnyng yede doun in to Egipt, that it schulde be there `an erthe tiliere, and Assur falsli calengide it with out ony cause.
Pakuti Ambuye Yehova akuti, “Poyamba paja anthu anga anapita kukakhala ku Igupto; nawonso Asiriya awapondereza popanda chifukwa.”
5 And now what is to me here? seith the Lord; for my puple is takun awei with out cause; the lordis therof doen wickidli, seith the Lord, and my name is blasfemyd contynueli al dai.
Tsopano Ine Yehova ndikuti, “Kodi nditani pakuti anthu anga atengedwa ukapolo osaperekapo kanthu, amene amawalamulira amawanyoza,” akutero Yehova. “Ndipo tsiku lonse, akungokhalira kuchita chipongwe dzina langa.
6 For this thing my puple schal knowe my name in that day, for lo! Y my silf that spak, am present.
Tsono tsiku limenelo anthu anga adzadziwa dzina langa; kotero adzadziwa kuti ndi Ine amene ndikuyankhula, Indedi, ndine.”
7 Ful faire ben the feet of hym that tellith, and prechith pees on hillis, of hym that tellith good, of hym that prechith helthe, and seith, Sion, thi God schal regne.
Ngokongoladi mapazi a amithenga obweretsa nkhani yabwino amene akuyenda pa mapiri. Iwo akukubweretserani nkhani zabwino za mtendere, chisangalalo ndi chipulumutso. Iwo akubwera kudzawuza anthu a ku Ziyoni kuti, “Mulungu wako ndi mfumu!”
8 The vois of thi biholderis; thei reisiden the vois, thei schulen herie togidere; for thei schulen se with iye to iye, whanne the Lord hath conuertid Sion.
Mverani! Alonda anu akukweza mawu awo; akuyimba pamodzi mwachimwemwe. Popeza akuona chamaso kubwera kwa Yehova ku Yerusalemu.
9 The forsakun thingis of Jerusalem, make ye ioie, and herie ye togidere; for the Lord hath coumfortid his puple, he hath ayenbouyt Jerusalem.
Imbani pamodzi mofuwula nyimbo zachimwemwe, inu mabwinja a Yerusalemu, pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, wapulumutsa Yerusalemu.
10 The Lord hath maad redi his hooli arm in the iyen of alle folkis, and alle the endis of the erthe schulen se the helthe of oure God.
Yehova wagwiritsa ntchito mphamvu zake zopatulika pamaso pa anthu a mitundu yonse, ndipo anthu onse a dziko lapansi adzaona chipulumutso cha Mulungu wathu.
11 Go ye awei, go ye awei, go ye out fro thennus; nyle ye touche defoulid thing, go ye out fro the myddis therof; be ye clensid, that beren the vessels of the Lord.
Nyamukani, nyamukani, chokaniko ku Babuloniko! Musakhudze kanthu kodetsedwa! Inu amene mumanyamula ziwiya za Yehova tulukanimo ndipo mudziyeretse.
12 For ye schulen not go out in noyse, nether ye schulen haaste in fleynge awei; for whi the Lord schal go bifore you, and the God of Israel schal gadere you togidere.
Koma simudzachoka mofulumira kapena kuchita chothawa; pakuti Yehova adzayenda patsogolo panu, Mulungu wa Israeli adzakutetezani kumbuyo kwanu.
13 Lo! my seruaunt schal vndirstonde, and he schal be enhaunsid, and he schal be reisid, and he schal be ful hiy.
Taonani, mtumiki wanga adzapambana pa ntchito yake adzakwezedwa ndi kulemekezedwa ndipo adzalandira ulemu waukulu kwambiri.
14 As many men wondriden on hym, so his biholdyng schal be with out glorie among men, and the fourme of hym among the sones of men.
Anthu ambiri atamuona anadzidzimuka, chifukwa nkhope yake inali itasakazika; sinalinso ngati ya munthu. Ndipo thupi lake linasakazika; silinalinso ngati la munthu.
15 He schal bisprenge many folkis; kyngis schulen holde togidere her mouth on him; for thei schulen se, to whiche it was not teld of hym, and thei that herden not, bihelden.
Momwemonso anthu a mitundu yonse adzadodoma naye, ndipo mafumu adzatseka pakamwa pawo kusowa chonena chifukwa cha iye. Pakuti zinthu zimene iwo sanawuzidwepo, adzaziona, ndipo zimene sanazimvepo, adzazimvetsa.

< Isaiah 52 >