< Isaiah 5 >

1 I schal synge for my derlyng the song of myn vnclis sone, of his vyner. A vyner was maad to my derlyng, in the horne in the sone of oile.
Ndidzamuyimbira bwenzi langa nyimbo yokamba za munda wake wa mpesa: Wokondedwa wanga anali ndi munda wamphesa pa phiri la nthaka yachonde.
2 And he heggide it, and chees stoonys therof, and plauntide a chosun vyner; and he bildide a tour in the myddis therof, and rerede a presse ther ynne; and he abood, that it schulde bere grapis, and it bare wielde grapis.
Anatipula nachotsa miyala yonse ndipo anawokamo mipesa yabwino kwambiri. Anamanga nsanja yolondera pakati pa mundawo ndipo anasemanso mopsinyira mphesa mʼmundamo. Ndipo iye anayembekezera kuti mundawo udzabala mphesa zabwino, koma ayi, unabala mphesa zosadya.
3 Now therfor, ye dwelleris of Jerusalem, and ye men of Juda, deme bitwixe me and my viner.
“Tsopano, inu amene mumakhala mu Yerusalemu ndi inu anthu a ku Yuda, weruzani pakati pa ine ndi munda wanga wa mpesawu.
4 What is it that Y ouyt to do more to my vyner, and Y dide not to it? whether that Y abood, that it schulde bere grapis, and it bare wielde grapis?
Kodi nʼchiyaninso china chimene ndikanachitira munda wanga wa mpesa kupambana chomwe ndawuchitira kale? Pamene ndinkayembekezera kuti udzabala mphesa zabwino, bwanji unabala mphesa zosadya?
5 And now Y schal schewe to you, what Y schal do to my vyner. Y schal take awei the hegge therof, and it schal be in to rauyschyng; Y schal caste doun the wal therof, and it schal be in to defoulyng; and Y schal sette it desert,
Tsopano ndikuwuzani chimene ndidzawuchitire munda wanga wa mpesa: ndidzachotsa mpanda wake, ndipo mundawo udzawonongeka; ndidzagwetsa khoma lake, ndipo nyama zidzapondapondamo.
6 ether forsakun. It schal not be kit, and it schal not be diggid, and breris and thornes schulen `growe vp on it; and Y schal comaunde to cloudis, that tho reyne not reyn on it.
Ndidzawusandutsa tsala, udzakhala wosatengulira ndi wosalimira ndipo mudzamera mkandankhuku ndi minga ina. Ndidzalamula mitambo kuti isagwetse mvula pa mundapo.”
7 Forsothe the vyner of the Lord of oostis is the hous of Israel, and the men of Juda ben the delitable buriownyng of hym. Y abood, that it schal make doom, and lo! wickidnesse; and that it schulde do riytfulnesse, and lo! cry.
Munda wamphesa wa Yehova Wamphamvuzonse ndi Aisraeli, ndipo anthu a ku Yuda ndiwo minda yake yomukondweretsa. Ndipo Iye ankayembekezera chiweruzo cholungama, mʼmalo mwake anaona kuphana; mʼmalo mwa chilungamo Iye anamva kulira kwa anthu ozunzika.
8 Wo to you that ioynen hows to hous, and couplen feeld to feeld, `til to the ende of place. Whether ye aloone schulen dwelle in the myddis of the lond?
Tsoka kwa inu amene mumangokhalira kulumikiza nyumba, ndipo mumangokhalira kuwonjezera minda, mpaka mutalanda malo onse kuti muzikhalamo nokha mʼdzikomo.
9 These thingis ben in the eeris of me, the Lord of oostis; if many housis ben not forsakun, grete housis and faire, with outen dwellere, bileue ye not to me.
Yehova Wamphamvuzonse wayankhula ine ndikumva kuti, “Ndithudi nyumba zambirizo zidzasanduka mabwinja, nyumba zazikulu zokongolazo zidzakhala zopanda anthu.
10 For whi ten acris of vynes schulen make a potel, and thretti buschels of seed schulen make thre buschels.
Munda wamphesa wa maekala khumi udzatulutsa vinyo wodzaza mbiya imodzi, kufesa madengu khumi a mbewu, zokolola zake zidzangodzaza dengu limodzi.”
11 Wo to you that risen togidere eerli to sue drunkennesse, and to drinke `til to euentid, that ye brenne with wyn.
Tsoka kwa iwo amene amadzuka mmamawa nathamangira chakumwa choledzeretsa, amene amamwa mpaka usiku kufikira ataledzera kotheratu.
12 Harpe, and giterne, and tympan, and pipe, and wyn ben in youre feestis; and ye biholden not the werk of the Lord, nether ye biholden the werkis of hise hondis.
Pa maphwando awo pamakhala azeze, apangwe, matambolini, zitoliro ndi vinyo, ndipo sasamala ntchito za Yehova, salemekeza ntchito za manja ake.
13 Therfor my puple is led prisoner, for it hadde not kunnyng; and the noble men therof perischiden in hungur, and the multitude therof was drye in thirst.
Motero anthu anga adzatengedwa ukapolo chifukwa cha kusamvetsa zinthu; atsogoleri awo olemekezeka adzafa ndi njala, ndipo anthu wamba ochuluka adzafa ndi ludzu.
14 Therfor helle alargide his soule, and openyde his mouth with outen ony ende; and strong men therof, and the puple therof, and the hiy men, and gloriouse men therof, schulen go doun to it. (Sheol h7585)
Nʼchifukwa chake ku manda sikukhuta ndipo kwayasama kwambiri kukamwa kwake; mʼmandamo mudzagweranso anthu otchuka a mu Yerusalemu pamodzi ndi anthu wamba ochuluka; adzagweramo ali wowowo, nʼkuledzera kwawoko. (Sheol h7585)
15 And a man schal be bowid doun, and a man of age schal be maad low; and the iyen of hiy men schulen be pressid doun.
Ndipo munthu aliyense adzatsitsidwa, anthu onse adzachepetsedwa, anthu odzikuza adzachita manyazi.
16 And the Lord of oostis schal be enhaunsid in doom, and hooli God schal be halewid in riytfulnesse.
Koma Yehova Wamphamvuzonse adzalemekezedwa chifukwa cha chiweruzo chake cholungama. Ndipo Mulungu woyera adzadzionetsa kuti ndi woyera pochita chilungamo chake.
17 And lambren schulen be fed bi her ordre, and comelyngis schulen ete desert places turned in to plentee.
Tsono nkhosa zidzadya pamenepo ngati pabusa pawo; ana ankhosa adzadya mʼmabwinja a anthu olemera.
18 Wo to you that drawen wickydnesse in the cordis of vanyte, and drawen synne as the boond of a wayn; and ye seien,
Tsoka kwa amene amadzikokera tchimo ndi zingwe zachinyengo, ndipo amadzikokera zoyipa ndi zingwe zokokera ngolo,
19 The werk of hym haaste, and come soone, that we se; and the counsel of the hooli of Israel neiy, and come, and we schulen knowe it.
amene amanena kuti, “Yehova afulumire, agwire ntchito yake mwamsanga kuti ntchitoyo tiyione. Ntchito zionekere, zimene Woyerayo wa Israeli akufuna kuchita, zichitike kuti tizione.”
20 Wo to you that seien yuel good, and good yuel; and putten derknessis liyt, and liyt derknessis; and putten bittir thing in to swete, and swete thing in to bittir.
Tsoka kwa amene zoyipa amaziyesa zabwino ndipo zabwino amaziyesa zoyipa, amene mdima amawuyesa kuwala ndipo kuwala amakuyesa mdima, amene zowawasa amaziyesa zotsekemera ndipo zotsekemera amaziyesa zowawasa.
21 Wo to you that ben wise men in youre iyen, and ben prudent bifor you silf.
Tsoka kwa amene amadziona ngati anzeru ndipo amadziyesa ochenjera.
22 Wo to you that ben myyti to drynke wyn, and ben stronge to meddle drunkenesse;
Tsoka kwa zidakwa zimene zimayika mtima pa vinyo ndipo ndi akatswiri posakaniza zakumwa,
23 and ye iustifien a wickid man for yiftis, and ye taken awei the riytfulnesse of a iust man fro hym.
amene amamasula olakwa chifukwa cha chiphuphu koma amayipitsa mlandu wa munthu wosalakwa.
24 For this thing, as the tunge of fier deuourith stobil, and the heete of flawme brenneth, so the roote of hem schal be as a deed sparcle, and the seed of hem schal stie as dust; for thei castiden awei the lawe of the Lord of oostis, and blasfemyden the speche of the hooli of Israel.
Nʼchifukwa chake monga momwe moto umawonongera chiputu ndipo monga momwe udzu wowuma umapsera mʼmalawi a moto, momwemonso mizu yawo idzawola ndipo maluwa awo adzafota ndi kuwuluka ngati fumbi; chifukwa akana malamulo a Yehova Wamphamvuzonse, ndipo anyoza mawu a Woyerayo wa Israeli.
25 Therfor the strong veniaunce of the Lord was wrooth ayens his puple, and he stretchide forth his hond on it, and smoot it; and hillis weren disturblid, and the deed bodies of hem weren maad as a toord in the myddis of stretis. In alle these thingis the stronge vengeaunce of him was not turned awei, but yit his hond was stretchid forth.
Nʼchifukwa chake mkwiyo wa Yehova wayakira anthu ake; watambasula dzanja lake pa anthuwo ndipo akuwakantha Mapiri akugwedezeka, ndipo mitembo ya anthu yangoti mbwee mʼmisewu ngati zinyalala. Komabe ngakhale watero, mkwiyo wake sunaleke, dzanja lake likanali chitambasulire;
26 And he schal reise a signe among naciouns afer, and he schal hisse to hym fro the endis of erthe; and lo! he schal haaste, and schal come swiftli.
Yehova wakweza mbendera kuyitana mtundu wa anthu akutali, akuyitana anthuwo ndi likhweru kuti abwere kuchokera ku mathero a dziko lapansi. Awo akubwera, akubweradi mofulumira kwambiri!
27 Noon is failynge nethir trauelynge in that oost; he schal not nappe, nether slepe, nether the girdil of his reynes schal be vndo, nether the lace of his scho schal be brokun.
Palibe ndi mmodzi yemwe amene akutopa kapena kupunthwa, palibe amene akusinza kapena kugona; palibe lamba wa mʼchiwuno amene akumasuka, palibe chingwe cha nsapato chimene chaduka.
28 Hise arowis ben scharpe, and alle hise bowis ben bent; the houys of hise horsis ben as a flynt, and hise wheelis ben as the feersnesse of tempest.
Mivi yawo ndi yakuthwa, mauta awo onse ndi okoka, ziboda za akavalo awo nʼzolimba ngati mwala wansagalabwi, magaleta awo ndi aliwiro ngati kamvuluvulu.
29 His roryng schal be as of lioun; he schal rore as the whelpis of liouns; and he schal gnaste, and schal holde prey, and schal biclippe, and noon schal be, that schal delyuere.
Kufuwula kwawo kuli ngati kubangula kwa mkango, amabangula ngati misona ya mkango; imadzuma pamene ikugwira nyama ndipo imapita nayo popanda ndi mmodzi yemwe woyipulumutsa.
30 And he schal sowne on it in that dai, as doith the soun of the see; we schulen biholde in to the erthe, and lo! derknessis of tribulacioun, and liyt is maad derk in the derknesse therof.
Tsiku limenelo mitundu ya anthu idzabangula ngati mkokomo wa madzi a mʼnyanja. Ndipo wina akakayangʼana dzikolo adzangoona mdima ndi zovuta; ngakhale kuwala kudzasanduka mdima chifukwa cha mitambo.

< Isaiah 5 >