< Isaiah 40 >

1 My puple, be ye coumfortid, be ye coumfortid, seith youre Lord God.
Atonthozeni, atonthozeni anthu anga, akutero Mulungu wanu.
2 Speke ye to the herte of Jerusalem, and clepe ye it, for the malice therof is fillid, the wickidnesse therof is foryouun; it hath resseyued of the hond of the Lord double thingis for alle hise synnes.
Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu ndipo muwawuzitse kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha, tchimo lawo lakhululukidwa. Ndawalanga mokwanira chifukwa cha machimo awo onse.
3 The vois of a crier in desert, Make ye redi the weie of the Lord, make ye riytful the pathis of oure God in wildirnesse.
Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti, “Konzani njira ya Yehova mʼchipululu; wongolani njira zake; msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.
4 Ech valey schal be enhaunsid, and ech mounteyn and litil hil schal be maad low; and schrewid thingis schulen be in to streiyt thingis, and scharpe thingis schulen be in to pleyn weies.
Chigwa chilichonse achidzaze. Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse; Dziko lokumbikakumbika alisalaze, malo azitundazitunda awasandutse zidikha.
5 And the glorie of the Lord schal be schewid, and ech man schal se togidere, that the mouth of the Lord hath spoke.
Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera, ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona, pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”
6 The vois of God, seiynge, Crie thou. And Y seide, What schal Y crie? Ech fleisch is hei, and al the glorie therof is as the flour of the feeld.
Wina ananena kuti, “Lengeza.” Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani? “Pakuti anthu onse ali ngati udzu ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.
7 The hei is dried vp, and the flour felle doun, for the spirit of the Lord bleew therynne.
Udzu umanyala ndipo maluwa amafota chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.” Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.
8 Verely the puple is hey; the hey is dried vp, and the flour felle doun; but the word of the Lord dwellith with outen ende.
Udzu umanyala ndipo maluwa amafota, koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”
9 Thou that prechist to Sion, stie on an hiy hil; thou that prechist to Jerusalem, enhaunse thi vois in strengthe; enhaunse thou, nyle thou drede; seie thou to the citees of Juda, Lo! youre God.
Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni, kwera pa phiri lalitali. Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu, fuwula kwambiri, kweza mawu, usachite mantha; uza mizinda ya ku Yuda kuti, “Mulungu wanu akubwera!”
10 Lo! the Lord God schal come in strengthe, and his arm schal holde lordschipe; lo! his mede is with hym, and his werk is bifore hym.
Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu, ndipo dzanja lake likulamulira, taonani akubwera ndi mphotho yake watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.
11 As a scheepherd he schal fede his flok, he schal gadere lambreen in his arm, and he schal reise in his bosom; he schal bere scheep `with lomb.
Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa: Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.
12 Who mat watris in a fist, and peiside heuenes with a spanne? Who peiside the heuynesse of the erthe with thre fyngris, and weide mounteyns in a weihe, and litle hillis in a balaunce?
Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake, kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake? Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu, kapena kuyeza kulemera kwa mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?
13 Who helpide the Spirit of the Lord, ether who was his councelour, and schewide to hym?
Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?
14 With whom took he councel, and who lernyde hym, and tauyte hym the path of riytfulnesse, and lernyde hym in kunnyng, and schewyde to him the weie of prudence?
Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya, kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru? Iye anapempha nzeru kwa yani ndi njira ya kumvetsa zinthu?
15 Lo! folkis ben as a drope of a boket, and ben arettid as the tunge of a balaunce; lo!
Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko. Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo; mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.
16 ylis ben as a litil dust, and the Liban schal not suffice to brenne his sacrifice, and the beestis therof schulen not suffice to brent sacrifice.
Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe, ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.
17 Alle folkis ben so bifore hym, as if thei ben not; and thei ben rettid as no thing and veyn thing to hym.
Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake; Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu ndi cha chabechabe.
18 To whom therfor maden ye God lijk? ether what ymage schulen ye sette to hym?
Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani? Kodi mungamufanizire ndi chiyani?
19 Whether a smyth schal welle togidere an ymage, ether a gold smyth schal figure it in gold, and a worchere in siluer schal diyte it with platis of siluer?
Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide naliveka mkanda wasiliva.
20 A wijs crafti man chees a strong tre, and vnable to be rotun; he sekith how he schal ordeyne a symylacre, that schal not be mouyd.
Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere amasankha mtengo umene sudzawola, nafunafuna mʼmisiri waluso woti amupangire fano limene silingasunthike.
21 Whether ye witen not? whether ye herden not? whether it was not teld to you fro the begynnynge? whether ye vndurstoden not the foundementis of erthe?
Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe? Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?
22 Which sittith on the cumpas of erthe, and the dwelleris therof ben as locustis; which stretchith forth heuenes as nouyt, and spredith abrood tho as a tabernacle to dwelle.
Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi, Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala. Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga, nayikunga ngati tenti yokhalamo.
23 Which yyueth the sercheris of priuytees, as if thei be not, and made the iugis of erthe as a veyn thing.
Amatsitsa pansi mafumu amphamvu nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.
24 And sotheli whanne the stok of hem is nether plauntid, nether is sowun, nether is rootid in erthe, he bleew sudenli on hem, and thei drieden vp, and a whirle wynd schal take hem awei as stobil.
Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene kapena kufesedwa chapompano, ndi kungoyamba kuzika mizu kumene ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.
25 And to what thing `ye han licned me, and han maad euene? seith the hooli.
Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani? Kapena kodi alipo wofanana nane?”
26 Reise youre iyen an hiy, and se ye, who made these thingis of nouyt; which ledith out in noumbre the kniythod of tho, and clepith alle bi name, for the multitude of his strengthe, and stalworthnesse, and vertu; nether o residue thing was.
Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani. Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi? Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo, nayitana iliyonse ndi dzina lake. Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri, palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.
27 Whi seist thou, Jacob, and spekist thou, Israel, My weie is hid fro the Lord, and my doom passide fro my God?
Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti, “Yehova sakudziwa mavuto anga, Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”
28 Whether thou knowist not, ether herdist thou not? God, euerlastynge Lord, that made of nouyt the endis of erthe, schal not faile, nether schal trauele, nether enserchyng of his wisdom is.
Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Yehova ndiye Mulungu wamuyaya, ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi. Iye sadzatopa kapena kufowoka ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.
29 That yyueth vertu to the weeri, and strengthe to hem that ben not, and multiplieth stalworthnesse.
Iye amalimbitsa ofowoka ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.
30 Children schulen faile, and schulen trauele, and yonge men schulen falle doun in her sikenesse.
Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka, ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;
31 But thei that hopen in the Lord, schulen chaunge strengthe, thei schulen take fetheris as eglis; thei schulen renne, and schulen not trauele; thei schulen go, and schulen not faile.
koma iwo amene amakhulupirira Yehova adzalandira mphamvu zatsopano. Adzawuluka ngati chiwombankhanga; adzathamanga koma sadzalefuka, adzayenda koma sadzatopa konse.

< Isaiah 40 >