< Isaiah 4 >
1 And seuene wymmen schulen catche o man in that dai, and schulen seie, We schulen ete oure breed, and we schulen be hilid with oure clothis; oneli thi name be clepid on vs, do thou awei oure schenschip.
Tsiku limenelo akazi asanu ndi awiri adzagwira mwamuna mmodzi, nʼkunena kuti, “Ife tizidya chakudya chathuchathu, ndi kuvala zovala zathu; inu mungotilola kuti tidziyitanidwa ndi dzina lanu. Tichotseni manyazi aumbeta!”
2 In that dai the buriownyng of the Lord schal be in greet worschip and glorie; and the fruyt of erthe schal be hiy, and ful out ioye `schal be to hem that schulen be sauyd of Israel.
Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli.
3 And it schal be, ech that is left in Sion, and is resydue in Jerusalem, schal be clepid hooli; ech that is writun in lijf in Jerusalem;
Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu.
4 if the Lord waischith awei the filthis of the douytris of Sion, and waischith the blood of Jerusalem fro the myddis therof, in the spirit of doom, and in the spirit of heete.
Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto.
5 And the Lord made on ech place of the hille of Sion, and where he was clepid to help, a cloude bi dai, and smoke, and briytnesse of fier flawmynge in the niyt; for whi hilyng schal be aboue al glorie.
Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova.
6 And a tabernacle schal be in to a schadewynge place of the dai, fro heete, and in to sikirnesse and in to hidyng, fro whirlewynd and fro reyn.
Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.