< Isaiah 36 >

1 And it was don in the fourtenthe yeer of kyng Ezechie, Sennacherib, the kyng of Assiriens, stiede on alle the stronge citees of Juda, and took tho.
Chaka cha khumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya ku Yuda, nayilanda.
2 And the kyng of Assiriens sente Rapsases fro Lachis to Jerusalem, to kyng Ezechie, with greet power; and he stood at the watir cundit of the hiyere sisterne, in the weie of the feeld of a fullere.
Kenaka mfumu ya ku Asiriya inatuma kazembe wake wankhondo pamodzi ndi gulu lalikulu lankhondo kuchokera ku Lakisi kupita kwa mfumu Hezekiya ku Yerusalemu. Tsono kazembeyo anayima pafupi ndi ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe lakumtunda pa msewu wopita ku malo a munda wa mmisiri wochapa zovala.
3 And Eliachym, the sone of Elchie, that was on the hous, yede out to hym, and Sobna, the scryuen, and Joae, the sone of Asaph, the chaunceler.
Panali anthu atatu. Woyamba anali Eliyakimu mwana wa Hilikiya komanso ndiye woyangʼanira nyumba ya mfumu. Wachiwiri anali Sebina amene anali mlembi wa bwalo; ndipo wachitatu anali Yowa mwana wa Asafu komanso anali wolemba zochitika. Anthu awa anatuluka kukakumana ndi kazembe wa ankhondo uja.
4 And Rapsases seide to hem, Seie ye to Ezechie, The greet king, the king of Assiriens, seith these thingis, What is the trist, in which thou tristist?
Kazembe wa ankhondo anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?
5 ethir bi what councele ether strengthe disposist thou for to rebelle? on whom hast thou trist, for thou hast go awei fro me?
Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
6 Lo! thou tristist on this brokun staf of rehed, on Egipt, on which if a man restith, it schal entre in to his hoond, and schal perse it; so doith Farao, the kyng of Egipt, to alle men that tristen in hym.
Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.
7 That if thou answerist to me, We tristen in oure Lord God; whether it is not he, whose hiye places and auteris Esechie dide awei, and he seide to Juda and to Jerusalem, Ye schulen worschipe bifore this auter?
Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, ‘Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu,’ kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake, Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe ili?’
8 And now bitake thee to my lord, the kyng of Assiriens, and Y schal yyue to thee twei thousynde of horsis, and thou maist not yyue of thee stieris of tho horsis.
“Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: Ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
9 And hou schalt thou abide the face of the iuge of o place of the lesse seruauntis of my lord? That if thou tristist in Egipt, and in cartis, and in knyytis;
Iwe ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo.
10 and now whethir Y stiede to this lond with out the Lord, that Y schulde distrie it? The Lord seide to me, Stie thou on this lond, and distrie thou it.
Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga dziko lino popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.”
11 And Eliachym, and Sobna, and Joae, seiden to Rapsaces, Speke thou to thi seruauntis bi the langage of Sirie, for we vndurstonden; speke thou not to vs bi the langage of Jewis in the eeris of the puple, which is on the wal.
Pamenepo Eliyakimu, Sebina ndi Yowa anawuza kazembeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
12 And Rapsaces seide to hem, Whether mi lord sente me to thi lord, and to thee, that Y schulde speke alle these wordis, and not rathere to the men that sitten on the wal, that thei ete her toordis, and drynke the pisse of her feet with you?
Koma kazembeyo anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
13 And Rapsaces stood, and criede with greet vois in the langage of Jewis, and seide, Here ye the wordis of the greet kyng, the kyng of Assiriens.
Tsono kazembeyo anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
14 The kyng seith these thingis, Esechie disseyue not you, for he may not delyuere you;
Zimene mfumu ikunena ndi izi: Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni!
15 and Ezechie yyue not to you trist on the Lord, and seie, The Lord delyuerynge schal delyuere vs; this citee schal not be youun in to the hoond of the kyng of Assiriens.
Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
16 Nyle ye here Ezechie. For whi the kyng of Assiriens seith these thingis, Make ye blessyng with me, and go ye out to me; and ete ye ech man his vyner, and ech man his fige tre, and drynke ye ech man the water of his cisterne,
“Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
17 til Y come, and take awei you to a lond which is as youre lond; to a lond of whete and of wyn, to a lond of looues and of vyneris.
mpaka mfumuyo itabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanulo, dziko limene lili ndi tirigu ndi vinyo watsopano, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
18 Ezechie disturble not you, and seie, The Lord schal delyuere vs. Whether the goddis of folkis delyuereden ech his lond fro the hond of the kyng of Assiriens?
“Inu musalole kuti Hezekiya akusocheretseni pamene iye akuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’ Kodi alipo mulungu wa anthu a mtundu wina amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
19 Where is the god of Emath, and of Arphat? Where is the god of Sepharuaym? Whethir thei delyueriden Samarie fro myn hond?
Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
20 Who is of alle goddis of these londis, that delyueride his lond fro myn hond, that the Lord delyuere Jerusalem fro myn hond?
Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
21 And thei weren stille, and answeriden not to hym a word. For whi the kyng comaundide to hem, and seide, Answere ye not to him.
Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
22 And Eliachym, the sone of Elchie, that was on the hous, and Sobna, the scryueyn, and Joae, the sone of Asaph, chaunceler, entriden with to-rent clothis to Ezechie, and telde to hym the wordis of Rapsaces.
Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu; Sebina mlembi wa bwalo; ndi Yowa, mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza zonse zimene anayankhula kazembe uja.

< Isaiah 36 >