< Isaiah 35 >

1 The forsakun Judee and with outen weie schal be glad, and wildirnesse schal make ful out ioye, and schal floure as a lilie.
Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala; dziko lowuma lidzakondwa ndi kuchita maluwa.
2 It buriownynge schal buriowne, and it glad and preisynge schal make ful out ioie. The glorie of Liban is youun to it, the fairnesse of Carmele and of Saron; thei schulen se the glorie of the Lord, and the fairnesse of oure God.
Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe. Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni, maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni. Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova, ukulu wa Mulungu wathu.
3 Coumforte ye comelid hondis, and make ye strong feble knees.
Limbitsani manja ofowoka, limbitsani mawondo agwedegwede;
4 Seie ye, Men of litil coumfort, be ye coumfortid, and nyle ye drede; lo! oure God schal brynge the veniaunce of yeldyng, God hym silf schal come, and schal saue vs.
nenani kwa a mitima yamantha kuti; “Limbani mtima, musachite mantha; Mulungu wanu akubwera, akubwera kudzalipsira; ndi kudzabwezera chilango adani anu; akubwera kudzakupulumutsani.”
5 Thanne the iyen of blynde men schulen be openyd, and the eeris of deef men schulen be opyn.
Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
6 Thanne a crokid man schal skippe as an hert, and the tunge of doumbe men schal be openyd; for whi watris ben brokun out in desert, and stremes in wildirnesse.
Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala, ndipo osayankhula adzayimba mokondwera. Akasupe adzatumphuka mʼchipululu ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
7 And that that was drie, is maad in to a poond, and the thirsti is maad in to wellis of watris. Grenenesse of rehed, and of spier schal growe in dennes, in whiche dwelliden dragouns bifore. And a path and a weie schal be there,
mchenga wotentha udzasanduka dziwe, nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe. Pamene panali mbuto ya ankhandwe padzamera udzu ndi bango.
8 and it schal be clepid an hooli weie, he that is defoulid schal not passe therbi; and this schal be a streiyt weie to you, so that foolis erre not therbi.
Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu; ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika. Anthu odetsedwa sadzayendamo mʼmenemo; zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
9 A lioun schal not be there, and an yuel beeste schal not stie therbi, nether schal be foundun there.
Kumeneko sikudzakhala mkango, ngakhale nyama yolusa sidzafikako; sidzapezeka konse kumeneko. Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
10 And thei schulen go, that ben delyuered and ayenbouyt of the Lord; and thei schulen be conuertid, and schulen come in to Sion with preisyng; and euerlastynge gladnesse schal be on the heed of hem; thei schulen haue ioie and gladnesse, and sorewe and weilyng schulen fle awei.
Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera. Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba; kumeneko adzakondwa mpaka muyaya. Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe, ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.

< Isaiah 35 >