< Isaiah 3 >

1 For lo! the lordli gouernour, the Lord of oostis, schal take awei fro Jerusalem and fro Juda a myyti man, and strong, and al the strengthe of breed, and al the strengthe of watir;
Taonani tsopano, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yuda zinthu pamodzi ndi thandizo; adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse,
2 a strong man, and a man a werriour, and a domesman, and a profete, and a false dyuynour in auteris, and an elde man,
anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo, oweruza ndi aneneri, anthu olosera ndi akuluakulu,
3 a prince ouer fifti men, and a worschipful man in cheer, and a counselour, and a wijs man of principal crafti men, and a prudent man of mystik, ethir goostli, speche.
atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka, aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera.
4 And Y schal yyue children the princes of hem, and men of wymmens condiciouns schulen be lordis of hem.
Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo; ana akhanda ndiwo adzawalamulire.
5 And the puple schal falle doun, a man to a man, ech man to his neiybore; a child schal make noyse ayens an eld man, and an vnnoble man ayens a noble man.
Anthu adzazunzana, munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake. Anthu wamba adzanyoza akuluakulu.
6 For a man schal take his brother, the meneal of his fadir, and schal seie, A clooth is to thee, be thou oure prince; forsothe this fallyng be vndur thin hond.
Munthu adzagwira mʼbale wake mʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati, “Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu; lamulira malo opasuka ano!”
7 And he schal answere in that dai, and seie, Y am no leche, and nether breed, nether cloth is in myn hous; nyle ye make me prince of the puple.
Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti, “Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake. Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga; musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.”
8 For whi Jerusalem felle doun, and Juda felle doun togidere; for the tunge of hem, and the fyndingis of hem weren ayens the Lord, for to terre to wraththe the iyen of his mageste.
Yerusalemu akudzandira, Yuda akugwa; zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova, sakulabadira ulemerero wa Mulungu.
9 The knowyng of her cheer schal answere to hem; and thei prechiden her synne, as Sodom dide, and hidden not. Wo to the soule of hem, for whi yuels ben yoldun to hem.
Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa; amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu; salibisa tchimo lawolo. Tsoka kwa iwo odziputira okha mavuto.
10 Seie ye to the iust man, that it schal be to hym wel; for he schal ete the fruyt of hise fyndyngis.
Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino, pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo.
11 Wo to the wickid man in to yuel; for whi the yeldyng of hise hondis schal be maad to hym.
Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo! Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita.
12 The wrongful axeris of my puple robbiden it, and wymmen weren lordis therof. Mi puple, thei that seien thee blessid, disseyuen thee, and distrien the weie of thi steppis.
Achinyamata akupondereza anthu anga, ndipo amene akuwalamulira ndi akazi. Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani; akukuchotsani pa njira yanu.
13 The Lord stondith for to deme, and `the Lord stondith for to deme puplis;
Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu; wakonzeka kuti aweruze anthu ake.
14 the Lord schal come to doom, with the eldere men of his puple, and with hise princes; for ye han wastid my vyner, and the raueyn of a pore man is in youre hous.
Yehova akuwazenga milandu akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake: “Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa; nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi.
15 Whi al to-breken ye my puple, and grynden togidere the faces of pore men? seith the Lord God of oostis.
Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga, nʼkudyera masuku pamutu amphawi?” Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
16 And the Lord God seide, For that that the douytris of Syon weren reisid, and yeden with a necke stretchid forth, and yeden bi signes of iyen, and flappiden with hondis, and yeden, and with her feet yeden in wel araied goyng,
Yehova akunena kuti, “Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri, akuyenda atakweza makosi awo, akukopa amuna ndi maso awo akuyenda monyangʼama akuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo
17 the Lord schal make ballyd the nol of the douytris of Sion, and the Lord schal make nakid the heer of hem.
Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo; Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.”
18 In that dai the Lord schal take awei the ournement of schoon, and goldun litle bellis lijk the moone,
Tsiku limenelo Ambuye adzawachotsera zodzikongoletsera zawo: za mʼmiyendo, za ku mutu za mʼkhosi,
19 and ribans, and brochis, and ournementis of armes nyy the schuldris, and mytris, ether chapelettis,
ndolo ndi zibangiri, nsalu zophimba pa nkhope,
20 and coombis, and ournementis of armes niy the hondis, and goldun ourenementis lijk laumpreis, and litil vessels of oynementis,
maduku, zigwinjiri za mʼmiyendo ndi malamba, mabotolo a zonunkhira ndi zithumwa,
21 and eere ryngis, and ryngis, and preciouse stoonys hangynge in the forheed,
mphete ndi zipini,
22 and chaungynge clothis, and mentils, and schetis, ether smockis, and needlis,
zovala za pa mphwando, zipewa ndi mwinjiro, zikwama,
23 and myrouris, and smal lynun clothis aboute the schuldris, and kercheues, and roketis.
magalasi oyangʼanira, zovala zosalala, nduwira ndiponso nsalu za mʼmapewa.
24 And stynk shal be for swete odour, and a corde for the girdil; ballidnesse schal be for crispe heer, and an heire for a brest girdil.
Mʼmalo mwa kununkhira azidzanunkha, mʼmalo mwa lamba, adzavala chingwe; mʼmalo mwa tsitsi lopesa bwino, adzakhala ndi dazi; mʼmalo mwa zovala zabwino, adzavala chiguduli; mʼmalo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.
25 Also thi faireste men schulen falle bi swerd, and thi stronge men schulen falle in batel.
Iwe Yerusalemu anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga, asilikali ako adzafera ku nkhondo.
26 And the yatis therof schulen weile, and morene; and it schal sitte desolat in erthe.
Pa zipata za Ziyoni padzakhala kubuma ndi kulira; Iweyo udzasakazidwa nʼkukhala pansi, ukugubuduzika pa fumbi.

< Isaiah 3 >