< Isaiah 29 >

1 Wo! Ariel, Ariel, the citee which Dauid ouercam; yeer is addid to yeer, solempnytees ben passyd.
Tsoka kwa iwe, Arieli, Arieli, mzinda umene Davide anakhazikitsamo zithando za nkhondo! Papite chaka chimodzi kapena ziwiri ndipo masiku a zikondwerero zanu azipitirirabe ndithu.
2 And Y schal cumpasse Ariel, and it schal be soreuful and morenynge; and Jerusalem schal be to me as Ariel.
Komatu Ine ndidzathira nkhondo Arieli ndipo kudzakhala kulira ndi kudandaula, mzindawo udzasanduka ngati ngʼanjo ya guwa lansembe.
3 And Y schal cumpasse as a round trendil in thi cumpasse, and Y schal caste erthe ayens thee, and Y schal sette engynes in to thi bisegyng.
Ine ndidzamanga misasa ya nkhondo kulimbana ndi mzindawo; ndidzakuzungulira ndi nsanja za nkhondo ndi kumanga mitumbira yanga ya nkhondo kulimbana nawe.
4 Thou schalt be maad low, thou schalt speke of erthe, and thi speche schal be herd fro the erthe; and thi vois schal be as the vois of a deed man reisid bi coniuring, and thi speche schal ofte grutche of the erthe.
Utagwetsedwa pansi, iwe udzayankhula kuchokera mʼnthaka, mawu ako adzatuluka uli mʼfumbi, adzamveka ngati a mzukwa. Mawu ako adzamveka ngati onongʼona kuchokera mʼfumbi.
5 And the multitude of hem that wyndewen thee, schal be as thynne dust; and the multitude of hem that hadden the maistrie ayens thee, schal be as a deed sparcle passynge.
Koma chigulu cha adani ako chidzasanduka chifwirimbwiti. Chigulu cha ankhondo achilendo chidzabalalika ngati mungu wowuluzika ndi mphepo. Mwadzidzidzi ndi mosayembekezereka,
6 And it schal be sudenli, anoon it schal be visitid of the Lord of oostis, in thundur, and in mouyng of the erthe, and in greet vois of whirlwynd, and of tempest, and of flawme of fier deuowrynge.
Yehova Wamphamvuzonse adzabwera ndi mabingu ndi chivomerezi ndi phokoso lalikulu, kamvuluvulu ndi namondwe ndi malawi a moto wonyeketsa.
7 And the multitude of alle folkis that fouyten ayens Ariel schal be as the dreem of a nyytis visioun; and alle men that fouyten, and bisegiden, and hadden the maistrie ayens it.
Tsono chigulu chankhondo cha mitundu ina yonse chimene chikulimbana ndi mzinda wa Arieli nʼkumathira nkhondo mzindawo, malinga ake ndi kuwuzinga, chigulu chonsecho chidzazimirira ngati maloto, gati zinthu zoziona mʼmasomphenya usiku.
8 And as an hungry man dremyth, and etith, but whanne he is awakid, his soule is voide; and as a thirsti man dremeth, and drynkith, and after that he is awakid, he is weri, and thirstith yit, and his soule is voide, so schal be the multitude of alle folkis, that fouyten ayens the hil of Sion.
Chidzakhala ngati munthu wanjala wolota akudya, koma podzuka ali nayobe njala; kapena ngati munthu waludzu wolota akumwa, koma podzuka, ali nalobe ludzu, kummero kwake kuli gwaa. Izi zidzachitika pamene chigulu cha nkhondo cha mitundu ina yonse chikunthira nkhondo Phiri la Ziyoni.
9 Be ye astonyed, and wondre; wake ye, and douyte ye; be ye drunken, and not of wyn; be ye moued, and not with drunkenesse.
Pitirizani kuledzera ndipo mudzakhala opusa. Dzitsekeni mʼmaso ndipo mukhale osapenya, ledzerani, koma osati ndi vinyo, dzandirani, koma osati ndi mowa.
10 For the Lord hath meddlid to you the spirit of sleep; he schal close youre iyen, and schal hile youre profetis, and princes that sien visiouns.
Yehova wakugonetsani tulo tofa nato. Watseka maso anu, inu aneneri; waphimba mitu yanu, inu alosi.
11 And the visioun of alle profetis schal be to you as the wordis of a book aseelid; which whanne thei schulen yyue to hym that kan lettris, thei schulen seie, Rede thou this book; and he schal answere, Y may not, for it is aseelid.
Kwa inu mawu onsewa ali ngati buku lotsekedwa, ndipo ngati lipatsidwa kwa wina wodziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde tawerengani bukuli,” iye adzati, “Sindingathe popeza ndi lomatidwa.”
12 And the book schal be youun to him that kan not lettris, and it schal be seid to hym, Rede thou; and he schal answere, Y kan no lettris.
Kapena ngati lipatsidwa kwa amene sadziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde werenga bukuli,” iye adzayankha kuti, “Ine sindidziwa kuwerenga.”
13 And the Lord seide, For that this puple neiyeth with her mouth, and glorifieth me with her lippis, but her herte is fer fro me; and thei dredden me for the comaundement and techyngis of men, therfor lo!
Ambuye akuti, “Anthu awa amandipembedza Ine ndi pakamwa pawo, ndi kundilemekeza Ine ndi milomo yawo, koma mitima yawo ili kutali ndi Ine. Kundipembedza kwawo ndi kwa chiphamaso. Amandipembedza motsata malamulo a anthu amene anaphunzitsidwa.
14 Y schal adde, that Y make wondryng to this puple, in a greet myracle and wondurful; for whi wisdom schal perische fro wise men therof, and the vndurstondyng of prudent men therof schal be hid.
Nʼchifukwa chakenso Ine ndidzapitirira kuwachitira ntchito zodabwitsa; nzeru za anthu anzeru zidzatha, luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
15 Wo to you that ben hiye of herte, that ye hide counsel fro the Lord; the werkis of whiche ben in derknessis, and thei seien, Who seeth vs, and who knowith vs?
Tsoka kwa amene amayesetsa kubisira Yehova maganizo awo, amene amachita ntchito zawo mu mdima nʼkumanena kuti, “Ndani amene akundiona kapena ndani akudziwa zimene ndikuchita?”
16 This thouyt of you is weiward, as if cley thenke ayens a pottere, and the werk seie to his makere, Thou madist not me; and a thing `that is maad, seie to his makere, Thou vndurstondist not.
Inu mumazondotsa zinthu ngati kuti dothi lasanduka wowumba mbiya. Kodi chinthu chopangidwa chingawuze wochipanga kuti “Sunandipange ndi iwe?” Kapena mʼphika kunena kwa amene anawuwumba kuti, “Iwe sudziwa chilichonse?”
17 Whether not yit in a litil time and schort the Liban schal be turned in to Chermel, and Chermel schal be arettid in to the forest?
Kodi Lebanoni posachedwapa sadzasanduka munda wachonde, ndipo kodi munda wachondewo ngati nkhalango?
18 And in that dai deef men schulen here the wordis of the book, and the iyen of blynde men schulen se fro derknessis and myisty;
Tsiku limenelo anthu osamva adzamva mawu a mʼbuku, ndipo anthu osaona amene ankakhala mu mdima adzapenya.
19 and mylde men schulen encreesse gladnesse in the Lord, and pore men schulen make ful out ioie in the hooli of Israel.
Anthu odzichepetsa adzakhalanso ndi chimwemwe mwa Yehova; ndipo anthu osowa adzakondwa chifukwa cha Woyerayo wa Israeli.
20 For he that hadde the maistrie, failide, and the scornere is endid, and alle thei ben kit doun that walkiden on wickidnesse;
Koma anthu ankhanza adzazimirira, oseka anzawo sadzaonekanso, ndipo onse okopeka ndi zoyipa adzawonongedwa.
21 whiche maden men to do synne in word, and disseyueden a repreuere in the yate, and bowiden awey in veyn fro a iust man.
Yehova adzalanga amene amasinjirira munthu kuti apezeke wolakwa, kapena kuphophonyetsa anthu ozenga mlandu ndi umboni wonama kuti osalakwa asaweruzidwe mwachilungamo.
22 For this thing the Lord, that ayen bouyte Abraham, seith these thingis to the hous of Jacob, Jacob schal not be confoundid now, nether now his cheer schal be aschamed; but whanne he schal se hise sones,
Choncho Yehova amene anawombola Abrahamu, akunena kwa zidzukulu za Yakobo kuti, “Anthu anga sadzachitanso manyazi; nkhope zawo sizidzagwanso ndi manyazi.
23 the werkis of myn hondis, halewynge my name in the myddis of hym. And thei schulen halewe the hooli of Jacob, and thei schulen preche God of Israel;
Akadzaona ana awo ndi ntchito ya manja anga pakati pawo, adzatamanda dzina langa loyera; adzazindikira kuyera kwa Woyerayo wa Yakobo, ndipo adzachita naye mantha Mulungu wa Israeli.
24 and thei that erren in spirit, schulen knowe vndurstondyng, and idil men schulen lerne the lawe.
Anthu opusa adzapeza nzeru; onyinyirika adzalandira malangizo.”

< Isaiah 29 >