< Isaiah 28 >

1 Wo to the coroun of pride, to the drunkun men of Effraym, and to the flour fallynge doun of the glorie of the ful out ioiyng therof, that weren in the cop of the fatteste valei, and erriden of wyn.
Tsoka ufumu wonyada wa zidakwa za ku Efereimu. Tsoka kwa ulemerero wake wokongola umene ukufota ngati duwa limene lili pa mutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde.
2 Lo! the myyti and strong Lord, as the feersnesse of hail, a whirlwynd brekynge togidere, as the fersnesse of many watris flowynge, and sent out on a large lond.
Taonani, ambuye ali naye wina wamphamvu ndi nyonga. Iye adzabwera ngati mkuntho wamatalala ndi namondwe wowononga, ngati madzi amphamvu osefukira a mvula yamkuntho; ndipo adzawagwetsa pansi mwankhanza.
3 The coroun of pride of the drunken men of Effraym schal be defoulid with feet,
Ulamuliro wa atsogoleri oledzera a ku Efereimu adzawuthetsa.
4 and the flour of glorie of the ful out ioiyng of hym, that is on the cop of valei of fat thingis, schal be fallyng doun, as a tymeli thing bifore the ripenesse of heruest; which whanne a man seynge biholdith, anoon as he takith with hond, he schal deuoure it.
Ndipo ulemerero wokongola wa mzinda umene uli ngati duwa lofota pamutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde uja, udzakhala ngati nkhuyu yoyambirira kupsa imene munthu akangoyiona amayithyola nthawi yokolola isanakwane.
5 In that dai the Lord of oostis schal be a coroun of glorie, and a garlond of ful out ioiyng, to the residue of his puple;
Tsiku limenelo Yehova Wamphamvuzonse adzakhala ngati nkhata yaufumu, chipewa chokongola kwa anthu ake otsala.
6 and a spirit of doom to hym that sittith on the trone, and strengthe to hem that turnen ayen fro batel to the yate.
Iye adzapereka mtima wachilungamo kwa oweruza, adzakhala chilimbikitso kwa amene amabweza adani pa zipata za mzinda.
7 But also thei knewen not for wyn, and erriden for drunkenesse; the preest and profete knewen not for drunkenesse; thei weren sopun up of wyn, thei erriden in drunkenesse; thei knewen not a profete, thei knewen not doom.
Nawonso awa ali dzandidzandi chifukwa cha vinyo ndipo akusochera chifukwa cha mowa: ansembe ndi aneneri akudzandira chifukwa cha mowa ndipo akusokonezeka chifukwa cha vinyo; akusochera chifukwa cha mowa, akudzandira pamene akuona masomphenya, kupunthwa pamene akupereka chigamulo.
8 For whi alle bordis weren fillid with spuyng and filthis, so that ther was no more place.
Pa matebulo onse pali masanzi okhaokha ndipo palibenso malo wopanda zonyansa.
9 Whom schal he teche kunnyng, and whom schal he make to vndurstonde heryng? Men wenyd fro mylk, men drawun awei fro tetis.
Iwo akuti, “Kodi munthu ameneyu akufuna aphunzitse ndani? Uthengawu akufuna kufotokozera yani? Ndi kwa ana amene aleka kuyamwa, kwa makanda ongowachotsa kumene ku bere?
10 For whi comaunde thou, comaunde thou ayen; comaunde thou, comaunde thou ayen; abide thou, abide thou ayen; abide thou, abide thou ayen; a litil there, a litil there.
Akuyesa kumatiphunzitsa pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Zonsezi akungoti apa pangʼono apa pangʼono.”
11 For whi in speche of lippe, and in other langage he schal speke to this puple,
Mulungu adzayankhula kwa anthu ake kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo, ziyankhulo zosamveka bwino. Mulungu adzayankhula kwa anthu awa, amene
12 to which he seide, This is my reste; refreische ye a weri man, and this is my refreischyng; and thei nolden here.
anakuwuzani kuti, “Malo opumulira ndi ano, otopa apumule, malo owusira ndi ano.” Koma inu simunamvere.
13 And the word of the Lord schal be to hem, Sende thou, sende thou ayen; send thou, sende thou ayen; abide thou, abide thou ayen; abide thou, abide thou ayen; a litil there, a litil there; that thei go, and falle backward, and be al to-brokun, and be snarid, and be takun.
Choncho Yehova adzakuphunzitsani pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Kotero mudzayenda ndi kugwa chambuyo, adzapweteka ndi kukodwa mu msampha ndipo adzakutengani ku ukapolo.
14 For this thing, ye men scorneris, that ben lordis ouer my puple which is in Jerusalem, here the word of the Lord.
Nʼchifukwa chake imvani mawu a Yehova, inu anthu achipongwe amene mumalamulira anthu awa mu Yerusalemu.
15 For ye seiden, We han smyte a boond of pees with deth, and we han maad couenaunt with helle; a scourge flowynge whanne it schal passe, schal not come on vs, for we han set a leesyng oure hope, and we ben kyuered with a leesyng. (Sheol h7585)
Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa, ife tachita mgwirizano ndi manda. Pamene mliri woopsa ukadzafika sudzatikhudza ife, chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.” (Sheol h7585)
16 Therfor the Lord God seith these thingis, Lo! Y schal sende in the foundementis of Sion a corner stoon preciouse, preuyd, foundid in the foundement; he that bileueth, schal not haaste.
Tsono zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi: “Taonani, ndikuyika mwala wovomerezeka ndi amisiri ngati maziko mu Ziyoni, mwala wapangodya, wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu; munthu amene awukhulupirira sadzagwedezeka.
17 And Y schal sette doom in weiyte, and riytfulnesse in mesure; and hail schal distrie the hope of leesyng, and watris schulen flowe on proteccioun. And youre boond of pees with deth schal be don awei,
Ntchito zolungama zidzakhala ngati chingwe choyezera maziko ake, ndipo chilungamo chidzakhala chowongolera mzere; matalala adzawononga malo anu othawirapo, amene ndi mabodza, ndipo madzi adzamiza malo anu obisalako.
18 and youre couenaunt with helle schal not stonde; whanne the scourge flowynge schal passe, ye schulen be to it in to defoulyng. (Sheol h7585)
Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa; mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa. Pakuti mliri woopsa udzafika, ndipo udzakugonjetsani. (Sheol h7585)
19 Whanne euer it schal passe, it schal take awei yow; for whi erli in the grey morewtid it schal passe, in dai and niyt; and oonli trauel aloone schal yyue vndurstondyng to heryng.
Ndipo ukadzangofika udzakutengani. Udzafika mmawa uliwonse, usiku ndi usana.” Anthu akadzamvetsetsa uthenga umenewu adzaopsedwa kwambiri.
20 Forsothe the bed is streit, so that the tother falle doun; and a schort mentil schal not hile euer either.
Mudzakhala ngati munthu wogona pa bedi lalifupi kwambiri kuti sangathe kutambalitsapo miyendo; ndiponso mudzakhala ngati munthu amene wafunda bulangeti lochepa kwambiri kuti sangathe nʼkufunda komwe.
21 For as in the hil of departyngis the Lord schal stonde, as in the valei, which is in Gabaon, he schal be wroth, that he do his werk; his werk alien, that he worche his werk; his werk is straunge fro hym.
Yehova adzamenya nkhondo monga anachitira ku phiri la Perazimu adzakalipa monga anachitira ku chigwa cha Gibiyoni; adzagwira ntchito yake yooneka ngati yachilendo, ndipo zimene ati adzachite zidzakhala ngati zodabwitsa.
22 And now nyle ye scorne, lest perauenture youre boondis be maad streit togidere; for Y herde of the Lord God of oostis, endyng and abreggyng on al erthe.
Tsopano lekani kunyoza, mukapanda kutero maunyolo anu adzakuthinani kwambiri; Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse wandiwuza kuti, “Ndagamula kuti ndidzawononga dziko lapansi.”
23 Perseyue ye with eeris, and here ye my vois; perseyue ye, and here ye my speche.
Tcherani khutu ndipo mumve mawu anga; mvetserani ndipo mumve zimene ndikunena.
24 Whether he that erith, schal ere al dai, for to sowe, and schal be kerue, and purge his londe?
Kodi mlimi wofuna kudzala mbewu amangokhalira kutipula kokhakokha? Kodi amangokhalira kugawula ndi kugalawuza kokhakokha?
25 Whether whanne he hath maad euene the face therof, schal he not sowe gith, and sprenge abrood comyn? and he schal not sette wheete bi ordre, and barli, and mylium, and fetchis in his coostis?
Pamene iye wasalaza mundawo, kodi samafesa mawere ndi chitowe? Kodi suja samadzala tirigu ndi barele mʼmizere yake, nadzala mchewere mʼphepete mwa mundawo?
26 And his God schal teche hym, in doom he schal teche hym.
Mulungu wake amamulangiza ndi kumuphunzitsa njira yabwino.
27 Forsothe gith schal not be threischid in sawis, and a wheel of a wayn schal not cumpasse on comyn; but gith schal be betun out with a yerd, and comyn with a staf.
Mawere sapunthira chopunthira cha galeta lopanda mikombero, kapena chitowe sapuntha popondetsapo mikombero ya galeta; mawere amapuntha ndi ndodo ndipo chitowe amapuntha ndi kamtengo.
28 Sotheli breed schal be maad lesse, but he that threischith schal not threische it with outen ende, nether schal trauele it with a wheel of a wayn, nether schal make it lesse with hise clees.
Tirigu ayenera kusinjidwa kuti apangire buledi, komabe munthu samangokhalira kupuntha tiriguyo osalekeza, kuopa kuti angatekedzeke. Ngakhale kuti amapuntha tiriguyo poyendetsapo mikombero ya galeta, koma akavalo ake satekedza tiriguyo.
29 And this thing yede out of the Lord God of oostis, that he schulde make wondirful councel, and magnefie riytfulnesse.
Izinso zimachokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, wa uphungu wodabwitsa ndi wa nzeru zopambana.

< Isaiah 28 >