< Isaiah 19 >

1 The birthun of Egipt. Lo! the Lord schal stie on a liyt cloude, and he schal entre in to Egipt; and the symilacris of Egipt schulen be mouyd fro his face, and the herte of Egipt schal faile in the myddis therof.
Uthenga onena za Igupto: Taonani, Yehova wakwera pa mtambo waliwiro, ndipo akupita ku Igupto. Mafano a ku Igupto akunjenjemera pamaso pake, ndipo mitima ya Aigupto yachokamo ndi mantha.
2 And Y schal make Egipcians to renne togidere ayens Egipcians, and a man schal fiyte ayens his brother, and a man ayens his frend, a citee ayens a citee, and a rewme ayens a rewme.
“Ine ndidzadzutsa Aigupto kuti amenyane okhaokha; mʼbale adzamenyana ndi mʼbale wake, mnansi ndi mnansi wake, mzinda ndi mzinda unzake, ndiponso ufumu ndi ufumu unzake.
3 And the spirit of Egipt schal be brokun in the entrailis therof, and Y schal caste doun the councel therof; and thei schulen axe her symylacris, and her false diuinouris, and her men that han vncleene spiritis spekinge in the wombe, and her dyuynouris bi sacrifices maad on auteris to feendis.
Aigupto adzataya mtima popeza ndidzalepheretsa zolinga zawo; adzapempha nzeru kwa mafano awo ndiponso kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kwa amawula ndi kwa oyankhula ndi mizimu.
4 And Y schal bitake Egipt in to the hond of cruel lordis, and a strong kyng schal be lord of hem, seith the Lord God of oostis.
Ndidzawapereka Aigupto kwa olamulira ankhanza, ndipo mfumu yoopsa idzawalamulira,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
5 And watir of the see schal wexe drie, and the flood schal be desolat, and schal be dried.
Madzi a mu mtsinje wa Nailo adzaphwa, ndipo mʼmbali mwa mtsinje mudzangʼaluka ndi kuwuma.
6 And the floodis schulen faile, and the strondis of the feeldis schulen be maad thynne, and schulen be dried; a rehed and spier schal fade.
Ngalande zake zidzanunkha; ndipo mitsinje ya Igupto idzayamba kuchepa ndi kuwuma. Bango ndi dulu zidzafota,
7 The botme of watir schal be maad nakid, and stremys fro her welle; and the moiste place of al seed schal be dried, schal waxe drie, and schal not be.
ndiponso zomera za mʼmphepete mwa Nailo ndi ku mathiriro a mtsinjewo. Zonse zodzalidwa mʼmbali mwa Nailo zidzawuma, zidzawuluzika ndipo sizidzaonekanso.
8 And fischeris schulen morne, and alle that casten hook in to the flood, schulen weile; and thei that spreden abrood a net on the face of watris, schulen fade.
Asodzi adzabuwula ndi kudandaula, onse amene amaponya mbedza mu Nailo; onse amene amaponya makoka mʼmadzi adzalira.
9 Thei schulen be schent, that wrouyten flex, foldynge and ordeynynge sutil thingis.
Amene amagwira ntchito yopota thonje adzataya mtima, anthu oluka nsalu zofewa zabafuta adzataya chiyembekezo.
10 And the watir places therof schulen be drye; alle that maden poondis to take fischis, schulen be schent.
Akatswiri opanga nsalu adzangoti kakasi, ndipo anthu onse ogwira ntchito yolipidwa adzatheratu mphamvu.
11 The fonned princes of Tafnys, the wise counselouris of Farao, yauen vnwise counsel; hou schulen ye seie to Farao, Y am the sone of wise men, the sone of elde kyngis?
Akuluakulu a ku Zowani ndi zitsiru; aphungu a nzeru a Farao amalangiza zopusa. Kodi mungathe kunena bwanji kwa Farao kuti, “Ine ndine mmodzi mwa anthu anzeru, wophunzira wa mafumu akale?”
12 Where ben now thi wise men? Telle thei to thee, and schewe thei, what the Lord of oostis thouyte on Egipt.
Iwe Farao, anthu ako anzeru ali kuti? Abweretu kuti akuwuze ndi kukudziwitsa zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonza kuchitira dziko la Igupto.
13 The princes of Tafnys ben maad foolis; the princes of Memphis fadiden; thei disseyueden Egipt, a corner of the puplis therof.
Akuluakulu a ku Zowani asanduka zitsiru, atsogoleri a ku Mefisi anamizidwa; atsogoleri a dziko la Igupto asocheretsa anthu a dzikolo.
14 The Lord meddlid a spirit of errour in the myddis therof; and thei maden Egipt for to erre in al his werk, as a drunkun man and spuynge errith.
Yehova wasocheretsa anthu a ku Igupto. Iwo akuchita kudzandira pa zonse zimene akuchita, ngati chidakwa choterereka pa masanzi ake.
15 And werk schal not be to Egipt, that it make an heed and tail bowynge and refreynynge.
Palibe chimene munthu wa mu Igupto angachite, mtsogoleri kapena wotsatira, nthambi ya kanjedza kapena bango.
16 In that dai Egipt schal be as wymmen, and thei schulen be astonyed, and schulen drede of the face of the mouynge of the hoond of the Lord of oostis, which he mouede on it.
Tsiku limenelo Aigupto adzakhala ngati amayi. Adzanjenjemera ndi kuchita mantha akadzaona Yehova Wamphamvuzonse, atakweza dzanja lake kufuna kuwalanga.
17 And the lond of Juda schal be to Egipt in to drede; ech that schal thenke on it, schal drede of the face of the counsel of the Lord of oostis, whiche he thouyte on it.
Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa dziko la Aigupto. Aliyense amene adzamve dzina la Yuda adzaopsedwa chifukwa cha zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonzekera kuchitira dziko la Igupto.
18 In that dai fyue citees schulen be in the lond of Egipt, and schulen speke with the tunge of Canaan, and schulen swere bi the Lord of oostis; the citee of the sunne schal be clepid oon.
Tsiku limenelo ku dziko la Igupto kudzakhala mizinda isanu yoyankhula chiyankhulo cha Akanaani, ndipo anthu ake adzalumbira kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti adzamutumikira. Umodzi mwa mizindayo udzatchedwa Mzinda Wachilungamo.
19 In that dai the auter of the Lord schal be in the myddis of the lond of Egipt, and the title of the Lord schal be bisidis the ende therof;
Tsiku limenelo mʼkati mwa dziko la Igupto mudzakhala guwa lansembe la Yehova, ndipo mʼmalire mwake adzayikira Yehova mwala wachikumbutso.
20 and it schal be in to a signe and witnessyng to the Lord of oostis, in the lond of Egipt. For thei schulen crie to the Lord fro the face of the troblere, and he schal sende a sauyour to hem, and a forfiytere, that schal delyuere hem.
Zimenezo zidzakhala umboni wozindikiritsa kuti Yehova Wamphamvuzonse alimo mʼdziko la Igupto. Pamene Aigupto adzalirira Yehova chifukwa cha owapondereza, Iye adzawatumizira mpulumutsi ndi mtetezi ndipo adzawalanditsa.
21 And the Lord schal be knowun of Egipt, and Egipcians schulen knowe the Lord in that dai; and thei schulen worschipe hym in sacrifices and yiftis, and thei schulen make vowis to the Lord, and thei schulen paie.
Kotero Yehova adzadziulula yekha kwa Aigupto, ndipo tsiku limenelo adzadziwa Yehova. Adzapembedza Yehova popereka nsembe ndi popereka zopereka zachakudya; Adzalumbira kwa Yehova ndipo adzachita zimene alumbirazo.
22 And the Lord schal smyte Egipt with a wounde, and schal make it hool; and Egipcians schulen turne ayen to the Lord, and he schal be plesid in hem, and he schal make hem hool.
Yehova adzakantha Aigupto ndi mliri. Iye adzawakanthadi ndipo kenaka adzawachiritsa. Aigupto adzatembenukira kwa Yehova ndipo Iye adzamva madandawulo awo ndi kuwachiritsa.
23 In that dai a wei schal be fro Egipt in to Assiriens, and Egipcians schulen serue Assur; and Assur schal entre in to Egipt, and Egipt in to Assiriens.
Tsiku limenelo kudzakhala msewu waukulu wochoka ku Igupto kupita ku Asiriya. Aasiriya adzapita ku Igupto ndi Aigupto ku Asiriya. Aigupto ndi Aasiriya adzapembedza pamodzi.
24 In that dai Israel schal be the thridde to Egipt and to Assur, the blessyng in the myddil of erthe;
Tsiku limenelo Israeli adzakhala pamodzi ndi Igupto ndi Asiriya, mayiko atatuwa adzakhala dalitso pa dziko lapansi.
25 whom the Lord of oostis blesside, seiynge, Blessid be my puple of Egipt, and the werk of myn hondis be to Assiriens; but myne eritage be to Israel.
Yehova Wamphamvuzonse adzawadalitsa, ndi mawu awa, “Adalitsike anthu anga Aigupto, Aasiriya, ntchito ya manja anga, ndi Aisraeli osankhidwa anga.”

< Isaiah 19 >