< Isaiah 16 >

1 Lord, sende thou out a lomb, the lordli gouernour of erthe, fro the stoon of desert to the hil of the douyter of Sion.
Anthu a ku Mowabu atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa, kuchokera ku Sela kudutsa chipululu mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.
2 And it schal be as a foule fleynge, and briddis fleynge awei fro the nest, so schulen be the douytris of Moab in the passyng ouer of Arnon.
Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku akazimwaza mʼchisa, momwemonso akazi a ku Mowabu akuyendayenda ku madooko a Arinoni.
3 Take thou councel, constreyne thou councel; sette thou as niyt thi schadewe in myddai, hide thou hem that fleen, and bitraye thou not men of vnstidfast dwellyng.
Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti, “Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite. Inu mutiteteze kwa adani anthu. Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo. Mutibise, musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.
4 My fleeris awei schulen dwelle at thee. Moab, be thou the hidyng place of hem fro the face of distriere. For whi dust is endid, the wretchid is wastid; he that defoulide the lond failude.
Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu; mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.” Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso, kuwononga kudzaleka; waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.
5 And the kyngis seete schal be maade redi in merci, and he schal sitte on it in treuthe, in the tabernacle of Dauid, demynge, and sekynge doom, and yeldynge swiftli that that is iust.
Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi; mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika. Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.
6 We han herd the pride of Moab, he is ful proud; his pride, and his boost, and his indignacioun is more than his strengthe.
Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri. Kunyada kwawo ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo, zonse ndi zopanda phindu.
7 Therfor Moab schal yelle to Moab, al Moab shal yelle to hem that ben glad on the wallis of bakun tijl stoon; speke ye her woundis.
Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri; iwo akulirira dziko lawo. Akubuma momvetsa chisoni chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.
8 For whi the subarbis of Esebon and the vyner of Sabama ben forsakun. The lordis of hethene men han kit doun the siouns therof; thei camen `til to Jaser, thei erriden in desert. The bowis therof ben forsakun, thei passiden the see.
Minda ya ku Hesiboni yauma, minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga. Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda minda ya mpesa wabwino, imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri, mpaka kutambalalira ku chipululu. Mizu yake inakafika mpaka ku tsidya la nyanja.
9 On this thing Y schal wepe in the weping of Jaser, and on the vyner of Sabama. Esebon and Eleale, Y schal fille thee with my teer; for the vois of defouleris fellen on thi vyndage, and on thi heruest.
Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri, chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima. Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali, ndikukunyowetsani ndi misozi! Mwalephera kupeza zokolola, chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.
10 And gladnesse and ful out ioiyng schal be takun awei fro Carmele; and noon schal make ful out ioye, nether schal synge hertli song in vyneris. He that was wont to wringe out, schal not wrynge out wyn in a pressour; Y haue take awei the vois of wryngeris out.
Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso; palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa; palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa, pakuti ndathetsa kufuwula.
11 On this thing my wombe schal sowne as an harpe to Moab, and myn entrails to the wal of bakun tiel stoon.
Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu, mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.
12 And it schal be, whanne it schal appere, that Moab hath trauelid on hise places, it schal entre to hise hooli thingis, that it biseche, and it schal not be worth.
Ngakhale anthu a ku Mowabu apite ku malo awo achipembedzo koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe chifukwa sizidzatheka.
13 This is the word which the Lord spak to Moab fro that tyme.
Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu.
14 And now the Lord spak, seiynge, In thre yeer that weren as the yeeris of an hirid man, the glorie of Moab schal be takun awei on al the myche puple; and ther schal be left in it as a litil rasyn, and a litil, and not myche.
Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”

< Isaiah 16 >