< Isaiah 13 >

1 The birthun of Babiloyne, which birthun Ysaie, the sone of Amos, siy.
Uthenga onena za Babuloni umene Yesaya mwana wa Amozi anawulandira:
2 Reise ye a signe on a myisti hil, and enhaunse ye vois; reise ye the hond, and duykis entre bi the yatis.
Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see, muwafuwulire ankhondo; muwakodole kuti adzalowe pa zipata za anthu olemekezeka.
3 Y haue comaundid to myn halewid men, and Y clepid my stronge men in my wraththe, that maken ful out ioie in my glorie.
Ine Yehova, ndalamulira ankhondo anga; ndasonkhanitsa ankhondo anga kuti akhale zida zanga zolangira amene amadzikuza ndi chipambano changa.
4 The vois of multitude in hillis, as of many puplis; the vois of sown of kyngis, of hethene men gaderit togidere. The Lord of oostis comaundide to the chyualry of batel,
Tamvani phokoso ku mapiri, likumveka ngati phokoso la gulu lalikulu la anthu! Tamvani phokoso pakati pa maufumu, ngati kuti mitundu ya anthu ikusonkhana pamodzi! Yehova Wamphamvuzonse akukhazika asilikali ake mokonzekera kuchita nkhondo.
5 to men comynge fro a fer lond. The Lord cometh fro the hiynesse of heuene, and the vessels of his strong veniaunce, that he distrie al the lond.
Iwo akuchokera ku mayiko akutali, kuchokera kumalekezero a dziko Yehova ali ndi zida zake za nkhondo kuti adzawononge dziko la Babuloni.
6 Yelle ye, for the dai of the Lord is niy; as wastyng it schal come of the Lord.
Lirani mofuwula, pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
7 For this thing alle hondis schulen be vnmyyti, and eche herte of man schal faile,
Zimenezi zinafowoketsa manja onse, mtima wa munthu aliyense udzachokamo.
8 and schal be al to-brokun. Gnawyngis and sorewis schulen holde Babiloyns; thei schulen haue sorewe, as they that trauelen of child. Ech man schal wondre at his neiybore; her cheris schulen be brent faces.
Anthu adzagwidwa ndi mantha aakulu, zowawa ndi masautso zidzawagwera; adzamva zowawa zonga amamva mayi pobereka. Adzayangʼanana mwamantha, nkhope zawo zikufiira ngati malawi amoto.
9 Lo! the dai of the Lord schal come, cruel, and ful of indignacioun, and of wraththe, and of woodnesse; to sette the lond into wildirnesse, and to al to-breke the synneris therof fro that lond.
Taonani, tsiku la Yehova likubwera, tsiku lopanda chisoni, lawukali ndi lamkwiyo; kudzasandutsa dziko kuti likhale chipululu ndi kuwononga anthu ochimwa a mʼmenemo.
10 For whi the sterris of heuene and the schynyng of tho schulen not sprede abrood her liyt; the sunne is maade derk in his risyng, and the moone schal not schine in hir liyt.
Nyenyezi zakumwamba ndiponso zonse zamlengalenga sizidzaonetsa kuwala kwawo. Dzuwa lidzada potuluka, ndipo mwezi sudzawala konse.
11 And Y schal visite on the yuels of the world, and Y schal visite ayens wickid men the wickidnesse of hem; and Y schal make the pride of vnfeithful men for to reste, and Y schal make low the boost of stronge men.
Ndidzalanga dziko lonse chifukwa cha zolakwa zake, anthu oyipa ndidzawalanga chifukwa cha machimo awo. Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza, ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.
12 A man of ful age schal be preciousere than gold, and a man schal be preciousere than pure gold and schynyng.
Ndidzasandutsa anthu kukhala ovuta kupeza kuposa mmene amasowera golide wabwino. Iwo sazidzapezekapezeka kuposa mmene amasowera golide wa ku Ofiri.
13 On this thing I schal disturble heuene, and the erthe schal be moued fro his place; for the indignacioun of the Lord of oostis, and for the dai of wraththe of his strong veniaunce.
Tsono ndidzagwedeza miyamba ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake. Izi zidzachitika chifukwa cha ukali wa Wamphamvuzonse pa tsiku la mkwiyo wake woopsa.
14 And it schal be as a doo fleynge, and as a scheep, and noon schal be that schal gadere togidere; ech man schal turne to his puple, and alle bi hem silf schulen fle to her lond.
Ngati mbawala zosakidwa, ngati nkhosa zopanda wozikusa, munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwawo, aliyense adzathawira ku dziko lake.
15 Ech man that is foundun, schal be slayn; and ech man that cometh aboue, schal falle doun bi swerd.
Aliyense amene atadzapezeke ndi kugwidwa adzaphedwa momubaya ndi lupanga.
16 The yonge children of them schulen be hurtlid doun bifore the iyen of them; her housis schulen be rauischid, and her wyues schulen be defoulid.
Ana awo akhanda adzaphwanyidwa iwo akuona; nyumba zawo zidzafunkhidwa ndipo akazi awo adzagwiriridwa.
17 Lo! Y schal reise on them Medeis, that seken not siluer, nethir wolen gold;
Taona, Ine ndidzadzutsa Amedi amene safuna siliva ndipo sasangalatsidwa ndi golide, kuti amenyane ndi Ababuloni.
18 but thei shulen sle litle children bi arowis, and thei schulen not haue merci on wombis yyuynge mylk, and the iye of them schal not spare on sones.
Adzapha anyamata ndi mauta awo; sadzachitira chifundo ana ngakhale kumvera chisoni ana akhanda.
19 And Babiloyne, thilke gloriouse citee in rewmes, noble in the pride of Caldeis, schal be destried, as God destried Sodom and Gomore.
Babuloni, ufumu wake ndi waulemerero kuposa mafumu onse. Anthu ake amawunyadira. Koma Yehova adzawuwononga ngati mmene anawonongera Sodomu ndi Gomora.
20 It shall not be enhabitid til in to the ende, and it schal not be foundid til to generacioun and generacioun; a man of Arabie schal not sette tentis there, and scheepherdis schulen not reste there.
Anthu sadzakhalamonso kapena kukhazikikamo pa mibado yonse; palibe Mwarabu amene adzayimike tenti yake, palibe mʼbusa amene adzawetamo ziweto zake.
21 But wielde beestis schulen reste there, and the housis of hem schulen be fillid with dragouns; and ostrichis schulen dwelle there, and heeri beestis schulen skippe there.
Koma nyama zakuthengo ndizo zidzakhale kumeneko, nyumba zake zidzadzaza ndi nkhandwe; mu mzindamo muzidzakhala akadzidzi, ndipo atonde akuthengo azidzalumphalumphamo.
22 And bitouris schulen answere there in the housis therof, and fliynge serpentis in the templis of lust.
Mu nsanja zake muzidzalira afisi, mʼnyumba zake zokongola muzidzalira nkhandwe. Nthawi yake yayandikira ndipo masiku ake ali pafupi kutha.

< Isaiah 13 >