< Isaiah 11 >

1 And a yerde schal go out of the roote of Jesse, and a flour schal stie of the roote of it.
Padzatuluka mphukira pa tsinde la Yese ndipo nthambi idzaphukira kuchokera ku mizu yake.
2 And the Spirit of the Lord schal reste on hym, the spirit of wisdom and of vndurstondyng, the spirit of counsel and of strengthe, the spirit of kunnyng and of pitee;
Mzimu wa Yehova udzakhala pa iye Mzimu wanzeru ndi wa kumvetsa zinthu, Mzimu wauphungu ndi wamphamvu, Mzimu wachidziwitso ndi wakuopa Yehova.
3 and the spirit of the drede of the Lord schal fille him. He schal deme not bi the siyt of iyen, nether he schal repreue bi the heryng of eeris;
Ndipo kuopa Yehova ndiye chidzakhale chinthu chomukondweretsa. Iye sadzaweruza potsata zooneka pamaso, kapena kugamula mlandu potsata zakumva;
4 but he schal deme in riytfulnesse pore men, and he schal repreue in equyte, for the mylde men of erthe. And he schal smyte the lond with the yerde of his mouth, and bi the spirit of his lippis he schal sle the wickid man.
koma amphawi adzawaweruza mwachilungamo, adzaweruza mwachilungamo mlandu wa anthu osauka a dziko lapansi. Iye adzakantha dziko lapansi ndi mawu ake; atalamula Iyeyu anthu oyipa adzaphedwa.
5 And riytfulnesse schal be the girdil of hise leendis, and feith schal be the girdyng of hise reynes.
Chilungamo chidzakhala ngati lamba wake ndipo kukhulupirika kudzakhala ngati chomangira mʼchiwuno mwake.
6 A wolf schal dwelle with a lombe, and a parde schal reste with a kide; a calf, and a lioun, and a scheep schulen dwelle togidere, and a litil child schal dryue hem.
Mʼmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wankhosa, kambuku adzagona pansi pamodzi ndi mwana wambuzi, mwana wangʼombe ndi mwana wa mkango adzadyera limodzi ndipo mwana wamngʼono adzaziweta.
7 A calf and a beere schulen be lesewid togidere; the whelpis of hem schulen reste, and a lioun as an oxe schal ete stre.
Ngʼombe yayikazi ndi chimbalangondo zidzadya pamodzi, ana awo adzagona pamodzi, ndipo mkango udzadya udzu ngati ngʼombe.
8 And a yonge soukyng child fro the tete schal delite on the hole of a snake, and he that is wenyd schal putte his hond in the caue of a cocatrice.
Mwana wakhanda adzasewera pa dzenje la mamba, ndipo mwana wamngʼono adzapisa dzanja lake ku phanga la mphiri osalumidwa.
9 Thei schulen not anoye, and schulen not sle in al myn hooli hil; forwhi the erthe is fillid with the kunnyng of the Lord, as watris of the see hilynge.
Sipadzakhala chilichonse chopweteka kapena chowononga pa phiri lopatulika la Yehova, pakuti anthu a dziko lapansi adzadzaza ndi nzeru yotha kudziwa Yehova monga momwe nyanja imadzazira ndi madzi.
10 In that dai the roote of Jesse, that stondith in to the signe of puplis; hethene men schulen biseche hym, and his sepulchre schal be gloriouse.
Tsiku limenelo mfumu yatsopano yochokera pa Muzu wa Yese idzakhala ngati chizindikiro kwa anthu a mitundu yonse. Mitundu ya anthu idzasonkhana kwa Iye, ndipo malo awo okhalapo adzakhala aulemerero.
11 And it schal be in that day, the Lord schal adde the secounde tyme his hond to haue in possessioun the residue of his puple that schal be left, of Assiriens, and of Egipt, and of Fethros, and of Ethiope, and of Elan, and of Sennar, and of Emath, and of ylis of the see.
Tsiku limenelo Ambuye adzatambasula dzanja lake kachiwiri kuti awombole anthu ake otsalira ku Asiriya, ku Igupto, ku Patirosi, Kusi, ku Elamu, ku Sinana, ku Hamati ndi pa zilumba za nyanja yamchere.
12 And he schal reise a sygne to naciouns, and schal gadere togidere the fleeris awei of Israel; and he schal gadere togidere the scaterid men of Juda fro foure coostis of erthe.
Adzakwezera mitundu ya anthu mbendera, ndipo adzasonkhanitsa otayika a ku Israeli; Iye adzasonkhanitsa anthu obalalika a ku Yuda kuchokera ku mbali zonse zinayi za dziko lapansi.
13 And the enuye of Effraym schal be don awei, and the enemyes of Juda schulen perische; Effraym schal not haue enuye to Juda, and Juda schal not fiyte ayens Effraym.
Nsanje ya Efereimu idzatha, ndipo adani a Yuda adzatha; Efereimu sadzachitira nsanje Yuda, ngakhale Yuda sadzamuda Efereimu.
14 And thei schulen flie in to the schuldris of Filisteis bi the see, thei schulen take prey togidere of the sones of the eest; Ydume and Moab schulen be the comaundement of the hond of hem, and the sones of Amon schulen be obedient.
Yuda ndi Efereimu adzathira nkhondo pa Afilisti mbali ya kumadzulo; ndipo onsewo pamodzi adzalanda zinthu za anthu a kummawa. Adzalimbana ndi Edomu ndi Mowabu, ndipo Aamoni adzawagonjera.
15 And the Lord schal make desolat the tunge of the see of Egipt, and he schal reise his hond on the flood in the strengthe of his spirit; and he schal smyte, ethir departe, it in seuene ryueris, so that schood men passe bi it.
Yehova adzaphwetsa mwendo wa nyanja ya Igupto; adzatambasula dzanja lake ndipo adzawombetsa mphepo yotentha pa mtsinje wa Yufurate. Iye adzawugawa mtsinjewo kukhala timitsinje tisanu ndi tiwiri kuti anthu athe kuwoloka powuma atavala nsapato.
16 And a weie schal be to my residue puple that schal be left, of Assiriens, as it was to Israel, in the dai in which it stiede fro the lond of Egipt.
Padzakhala msewu waukulu woti ayendepo anthu ake otsalira amene anatsalira ku Asiriya, monga mmene panali msewu waukulu woyendapo Israeli pamene amachokera ku Igupto.

< Isaiah 11 >