< Hosea 9 >

1 Israel, nyle thou be glad, nyle thou make ful out ioie as puplis; for thou hast do fornicacioun fro thi God. Thou louedist meede on alle the cornflooris of wheete.
Iwe Israeli, usakondwere; monga imachitira mitundu ina. Pakuti wakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wako; umakonda malipiro a chiwerewere pa malo aliwonse opunthira tirigu.
2 The cornfloor and pressour schal not feede hem, and wyn schal lie to hem.
Malo opunthira tirigu ndi malo opsinyira mphesa sadzadyetsa anthu; adzasowa vinyo watsopano.
3 Thei schulen not dwelle in the lond of the Lord. Effraym turnede ayen in to Egipt, and eet defoulid thing among Assiriens.
Sadzakhalanso mʼdziko la Yehova. Efereimu adzabwerera ku Igupto ndipo mudzadya chakudya chodetsedwa ku Asiriya.
4 Thei schulen not offre wyn to the Lord, and thei schulen not plese hym. The sacrificis of hem ben as breed of mourneris; alle that schulen ete it schulen be defoulid. For the breed of hem is to the lijf of hem; thei schulen not entre in to the hous of the Lord.
Iwo sadzaperekanso chopereka cha chakumwa kwa Yehova, kapena nsembe zawo kuti akondweretse Yehovayo. Nsembe zotere zidzakhala kwa iwo ngati chakudya cha anamfedwa; onse akudya chakudya chimenechi adzakhala odetsedwa. Chakudya ichi chidzakhala chodya okha, sichidzalowa mʼnyumba ya Yehova.
5 What schulen ye do in the solempne dai, in the dai of the feeste of the Lord?
Kodi mudzachita chiyani pa tsiku la maphwando anu oyikika; pa masiku a zikondwerero za Yehova?
6 For lo! thei ben goon out fro distriyng. Egipt schal gadere hem togidere, Memphis schal birie hem. A nettle schal enherite the desirable siluer of hem, a clote schal be in the tabernaclis of hem.
Ngakhale iwo atathawa chiwonongeko, Igupto adzawasonkhanitsa, ndipo Mefisi adzawayika mʼmanda. Khwisa adzamera pa ziwiya zawo zasiliva, ndipo minga idzamera mʼmatenti awo.
7 Daies of visitacioun ben comun, daies of yeldyng ben comun. Knowe ye, that Israel is a fool, a wood profete, a spiritual man, for the multitude of thi wickidnesse is also the multitude of woodnesse.
Masiku achilango akubwera, masiku obwezera ali pafupi. Israeli adziwe zimenezi. Chifukwa machimo anu ndi ochuluka kwambiri ndipo udani wanu pa Mulungu ndi waukulu kwambiri. Mneneri amamuyesa chitsiru, munthu wanzeru za kwa Mulungu ngati wamisala.
8 The biholdere of Effraym with my God is a profete; a snare of fallyng is maad now on alle the weies of hym, woodnesse is in the hous of his God.
Mneneri pamodzi ndi Mulungu wanga ndiwo alonda a Efereimu, koma mneneri amutchera misampha mʼnjira zake zonse, ndipo udani ukumudikira mʼnyumba ya Mulungu wake.
9 Thei synneden deepli, as in the daies of Gabaa. The Lord schal haue mynde on the wickidnesse of hem, and schal visite the synnes of hem.
Iwo azama mu zachinyengo monga masiku a Gibeya. Mulungu adzakumbukira zolakwa zawo ndipo adzawalanga chifukwa cha machimo awo.
10 Y foond Israel as grapis in desert, Y siy the fadris of hem as the firste applis of a fige tree, in the cop therof; but thei entriden to Belfegor, and weren alienyd in confusioun, and thei weren maad abhomynable as tho thingis whiche thei louyden.
“Pamene ndinamupeza Israeli zinali ngati kupeza mphesa mʼchipululu. Nditaona makolo anu, zinali ngati ndikuona nkhuyu zoyambirira kupsa. Koma atafika ku Baala Peori, anadzipereka ku fano lija lochititsa manyazi ndipo anakhala onyansa ngati chinthu chimene anachikondacho.
11 Effraym as a brid fley awei; the glorye of hem is of childberyng, and of the wombe, and of conseyuyng.
Ulemerero wa Efereimu udzawuluka ngati mbalame. Sipadzakhalanso kubereka ana, kuyembekezera kapena kutenga pathupi.
12 That if thei nurschen her sones, Y schal make hem with out children among men. But also wo to hem, whanne Y schal go awei fro hem.
Ngakhale atalera ana ndidzachititsa kuti mwana aliyense amwalire. Tsoka kwa anthuwo pamene Ine ndidzawafulatira!
13 Y siy that Effraym was as Tire, foundid in fairnesse; and Effraym schal lede out hise sones to the sleere.
Ndaona Efereimu ngati Turo, atadzalidwa pa nthaka ya chonde. Koma Efereimu adzatsogolera ana ake kuti akaphedwe.”
14 Lord, yyue thou to hem; what schalt thou yyue to hem? yyue thou to hem a wombe with out children, and drie tetis.
Inu Yehova, muwapatse. Kodi mudzawapatsa chiyani? Apatseni mimba yomangopita padera ndi mawere owuma.
15 Alle the wickidnessis of hem ben in Galgal, for there Y hadde hem hateful; for the malice of her fyndyngis. Y schal caste hem out of myn hous; Y schal not leie to, that Y loue hem. Alle the princes of hem goen awei.
“Chifukwa cha zoyipa zawo zonse ku Giligala, Ine ndinawada kumeneko. Chifukwa cha machitidwe awo auchimo, ndidzawapirikitsa mʼnyumba yanga. Sindidzawakondanso; atsogoleri awo onse ndi owukira.
16 Effraym is smyten, the roote of hem is dried vp; thei schulen not make fruyt. That thouy thei gendren, Y schal sle the moost louyd thingis of her wombe.
Efereimu wathedwa, mizu yake yauma sakubalanso zipatso. Ngakhale atabereka ana, Ine ndidzapha ana awo okondedwawo.”
17 My God schal caste hem awey, for thei herden not hym; and thei schulen be of vnstable dwellyng among naciouns.
Mulungu wanga adzawakana chifukwa sanamumvere Iye; adzakhala oyendayenda pakati pa anthu a mitundu ina.

< Hosea 9 >