< Hosea 4 >

1 Sones of Israel, here ye the word of the Lord, for whi doom is to the Lord with the dwelleris of erthe; for whi trewthe is not, and merci is not, and kunnyng of the Lord is not in erthe.
Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova, chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu amene mumakhala mʼdzikoli: “Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi mulibe kulabadira za Mulungu.
2 Curs, and leesyng, and manquelling, and thefte, and auowtrie flowiden, and blood touchide blood.
Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha. Kuba ndi kuchita chigololo; machimo achita kunyanya ndipo akungokhalira kuphana.
3 For this thing the erthe schal mourne, and ech that dwellith in that lond, schal be sijk, in the beeste of the feeld, and in the brid of the eir; but also the fischis of the see schulen be gaderid togidere.
Chifukwa chake dziko likulira ndipo onse amene amakhalamo akuvutika; zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
4 Netheles ech man deme not, and a man be not repreuyd; for thi puple is as thei that ayen seien the prest.
“Koma wina asapeze mnzake chifukwa, wina aliyense asayimbe mlandu mnzake, pakuti anthu ako ali ngati anthu amene amayimba mlandu wansembe.
5 And thou schalt falle to dai, and the profete also schal falle with thee; in the niyt Y made thi modir to be stille.
Mumapunthwa usana ndi usiku ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi. Choncho ndidzawononga amayi anu.
6 My puple was stille, for it hadde not kunnyng; for thou hast putte awei kunnyng, Y schal putte thee awei, that thou vse not presthod to me; and for thou hast foryete the lawe of thi God, also Y schal foryete thi sones.
Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa. “Pakuti mwakana kudziwa, Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga; chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu, Inenso ndidzayiwala ana anu.
7 Bi the multitude of hem, so thei synneden ayens me. Y schal chaunge the glorie of hem in to schenschipe.
Ansembe ankati akachuluka iwo ankandichimwiranso kwambiri; iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
8 Thei schulen ete the synnes of my puple, and thei schulen reise the soulis of hem to the wickidnesse of hem.
Amalemererapo pa machimo a anthu anga ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
9 And it schal be, as the puple so the prest; and Y schal visite on hym the weies of hym, and Y schal yelde to him the thouytis of hym.
Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe. Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo, ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
10 And thei schulen ete, and thei schulen not be fillid; thei diden fornicacioun, and ceessiden not, for thei forsoken the Lord in not kepynge.
“Iwo azidzadya koma sadzakhuta; azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana, chifukwa anasiya Yehova kuti adzipereke
11 Fornycacioun, and wiyn, and drunkenesse doen awei the herte.
ku zachiwerewere, ku vinyo wakale ndi watsopano, zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
12 My puple axide in his tre, and the staf therof telde to it; for the spirit of fornicacioun disseyuede hem, and thei diden fornicacioun fro her God.
za anthu anga. Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha. Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa; iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
13 On the heedis of mounteyns thei maden sacrifice, and on the litil hillis thei brenten encense vndur an ook, and a popeler, and terebynte, for the schadewe therof was good. Therfor youre douytris schulen do fornicacioun, and youre wyues schulen be auoutressis.
Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri ndi kufukiza lubani pa zitunda, pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi, pamene pali mthunzi wabwino. Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
14 Y schal not visite on youre douytris, whanne thei don fornicacioun, and on youre wyues, whanne thei doon auowtrie; for thei lyuyden with hooris, and maden sacrifice with men turned in to wymmens condiciouns. And the puple that vndirstondith not, schal be betun.
“Ine sindidzalanga ana anu aakazi pamene iwo adzachita zachiwerewere, kapena akazi a ana anu pamene adzachita zigololo. Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere, ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako. Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
15 If thou, Israel, doist fornicacioun, nameli Juda trespasse not; and nyle ye entre in to Galgala, and stie ye not in to Bethauen, nether swere ye, The Lord lyueth.
“Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli, Yuda asapezeke ndi mlandu wotere. “Usapite ku Giligala. Usapite ku Beti-Aveni. Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
16 For as a wielde cow Israel bowide awei; now the Lord schal fede hem as a lomb in broodnesse.
Aisraeli ndi nkhutukumve, ngosamva ngati ana angʼombe. Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
17 Effraym is the partener of idols, leeue thou him;
Efereimu waphathana ndi mafano; mulekeni!
18 the feeste of hem is departid. Bi fornicacioun thei diden fornicacioun, the defenders therof louyden to brynge schenschipe.
Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha, amapitiriza kuchita zachiwerewere; atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
19 The spirit boond hym in hise wyngis, and thei schulen be schent of her sacrifices.
Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.

< Hosea 4 >