< Hosea 3 >

1 And the Lord seide to me, Yit go thou, and loue a womman loued of a frend, and a womman auoutresse, as the Lord loueth the sones of Israel; and thei biholden to alien goddis, and louen the draffis of grapis.
Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”
2 And Y dalf it to me bi fiftene pens, and bi a corus of barli, and bi half a corus of barli.
Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele.
3 And Y seide to it, Bi many daies thou shalt abide me; thou schalt not do fornycacioun, and thou schalt not be with an hosebonde, but also Y schal abide thee.
Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”
4 For bi many daies the sones of Israel schulen sitte with out kyng, with out prince, and with out sacrifice, and with out auter, and with out prestis cloth, and with out terafyn, that is, ymagis.
Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano.
5 And after these thingis the sones of Israel schulen turne ayen, and schulen seke her Lord God, and Dauid, her king; and thei schulen drede at the Lord, and at the good of him, in the laste of daies.
Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.

< Hosea 3 >