< Hebrews 1 >
1 God, that spak sum tyme bi prophetis in many maneres to oure fadris, at the
Kale lija Mulungu ankayankhula ndi makolo athu pa nthawi zosiyanasiyana ndiponso mwa njira zosiyanasiyana kudzera mwa aneneri.
2 laste in these daies he hath spoke to vs bi the sone; whom he hath ordeyned eir of alle thingis, and bi whom he made the worldis. (aiōn )
Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. (aiōn )
3 Which whanne also he is the briytnesse of glorie, and figure of his substaunce, and berith alle thingis bi word of his vertu, he makith purgacioun of synnes, and syttith on the riythalf of the maieste in heuenes;
Mwanayo ndiye kuwala kwa ulemerero wa Mulungu, chithunzithunzi chenicheni cha khalidwe lake. Iyeyu amachirikiza zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu ake. Iye atayeretsa anthu kuchoka ku machimo awo, anakhala pansi kumwamba kudzanja lamanja la Mulungu waulemerero.
4 and so myche is maad betere than aungels, bi hou myche he hath eneritid a more dyuerse name bifor hem.
Mwanayu ndi wamkulu koposa angelo, monga momwe dzina limene analandira limaposa dzina la angelo.
5 For to whiche of the aungels seide God ony tyme, Thou art my sone, Y haue gendrid thee to dai? And eftsoone, Y schal be to hym in to a fadir, and he schal be to me in to a sone?
Kodi ndi kwa mngelo uti, kumene Mulungu anati, “Iwe ndiwe mwana wanga; Ine lero ndakhala Atate ako.” Kapena kunenanso kuti, “Ine ndidzakhala abambo ake; iye adzakhala mwana wanga.”
6 And whanne eftsoone he bryngith in the firste bigetun sone in to the world, he seith, And alle the aungels of God worschipe hym.
Pamene Mulungu amatuma Mwana wake woyamba kubadwa ku dziko lapansi anati, “Angelo onse a Mulungu amupembedze Iye.”
7 But he seith to aungels, He that makith hise aungels spiritis, and hise mynystris flawme of fier.
Iye ponena za angelo akuti, “Mulungu amasandutsa angelo ake mphepo, amasandutsa atumiki ake malawi amoto.”
8 But to the sone he seith, God, thi trone is in to the world of world; a yerde of equite is the yerde of thi rewme; (aiōn )
Koma za Mwana wake akuti, “Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya, ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu. (aiōn )
9 thou hast louyd riytwisnesse, and hatidist wickidnesse; therfor the God, thi God, anoyntide thee with oile of ioye, more than thi felowis.
Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; Nʼchifukwa chake, Mulungu wanu wakukwezani kuposa anzanu pokudzozani mafuta osonyeza chimwemwe.”
10 And, Thou, Lord, in the bigynnyng foundidist the erthe, and heuenes ben werkis of thin hondis; thei schulen perische,
Mulungu akutinso, “Ambuye, pachiyambi Inu munayika maziko a dziko lapansi; ndipo zakumwambako ndi ntchito za manja anu.
11 but thou schalt perfitli dwelle; and alle schulen wexe elde as a cloth, and thou schalt chaunge hem as a cloth,
Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu wachikhalire. Izo zidzatha ngati zovala.
12 and thei schulen be chaungid. But thou art the same thi silf, and thi yeeris schulen not faile.
Mudzazipindapinda ngati chofunda; ndipo zidzasinthidwa ngati chovala. Koma Inu simudzasintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.”
13 But to whiche of the aungels seide God at ony tyme, Sitte thou on my riythalf, till Y putte thin enemyes a stool of thi feet?
Kodi ndi kwa Mngelo uti kumene Mulungu ananenapo kuti, “Khala kudzanja langa lamanja mpaka nditapanga adani ako kukhale chopondapo mapazi ako.”
14 Whether thei alle ben not seruynge spiritis, sente to seruen for hem that taken the eritage of heelthe?
Kodi angelo onse si mizimu yotumikira odzalandira chipulumutso?