< Hebrews 5 >

1 For ech bischop takun of men, is ordeyned for men in these thingis `that ben to God, that he offre yiftis and sacrifices for synnes.
Mkulu wa ansembe aliyense amasankhidwa kuchokera pakati pa anthu ndipo amayikidwa kuti aziwayimirira pamaso pa Mulungu, kuti azipereka mphatso ndi nsembe chifukwa cha machimo.
2 Which may togidere sorewe with hem, that beth vnkunnynge and erren; for also he is enuyrounned with infirmytee.
Popeza kuti iye mwini ali ndi zofowoka zake, amatha kuwalezera mtima amene ali osadziwa ndi osochera.
3 And therfor he owith, as for the puple, so also for hym silf, to offre for synnes.
Chifukwa cha ichi, iye amadziperekera nsembe chifukwa cha machimo ake omwe ndiponso chifukwa cha machimo a anthu ena.
4 Nethir ony man taketh to hym onour, but he that is clepid of God, as Aaron was.
Palibe amene amadzipatsa yekha ulemu wotere, koma amachita kuyitanidwa ndi Mulungu monga momwe anayitanidwira Aaroni.
5 So Crist clarifiede not hym silf, that he were bischop, but he that spak to hym, Thou art my sone, to dai Y gendride thee.
Nʼchifukwa chake Khristu sanadzipatse yekha ulemu wokhala Mkulu wa ansembe. Koma Mulungu anamuwuza kuti, “Iwe ndiwe Mwana wanga; Ine lero ndakhala Atate ako.”
6 As `in anothere place he seith, Thou art a prest with outen ende, aftir the ordre of Melchisedech. (aiōn g165)
Ndipo penanso anati, “Iwe ndiwe wansembe mpaka muyaya, monga mwa unsembe wa Melikizedeki.” (aiōn g165)
7 Which in the daies of his fleisch offride, with greet cry and teeris, preieris and bisechingis to hym that myyte make hym saaf fro deth, and was herd for his reuerence.
Yesu, pa nthawi imene anali munthu pa dziko lapansi pano, anapereka mapemphero ake ndi zopempha mofuwula ndi misozi kwa Iye amene akanamupulumutsa ku imfa, ndipo anamumvera chifukwa anagonjera modzipereka.
8 And whanne he was Goddis sone, he lernyde obedience of these thingis that be suffride;
Ngakhale Iye anali Mwana wa Mulungu anaphunzira kumvera pomva zowawa.
9 and he brouyt to the ende is maad cause of euerlastinge heelthe to alle that obeischen to hym, (aiōnios g166)
Atasanduka wangwiro kotheratu, anakhala gwero la chipulumutso chosatha kwa onse omvera Iye. (aiōnios g166)
10 and is clepid of God a bischop, bi the ordre of Melchisedech.
Ndipo Mulungu anamuyika kukhala Mkulu wa ansembe, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.
11 Of whom ther is to vs a greet word for to seie, and able to be expowned, for ye ben maad feble to here.
Tili ndi zambiri zoti tinganene pa zimenezi, koma ndi zovuta kukufotokozerani chifukwa ndinu ochedwa kuphunzira.
12 For whanne ye ouyten to be maistris for tyme, eftsoone ye neden that ye be tauyt, whiche ben the lettris of the bigynnyng of Goddis wordis. And ye ben maad thilke, to whiche is nede of mylk, and not sad mete.
Ngakhale kuti pa nthawi ino munayenera kukhala aphunzitsi, pakufunikabe munthu wina kuti abwerezenso kudzakuphunzitsani maphunziro oyambira a choonadi cha Mulungu. Ndinu ofunika mkaka osati chakudya cholimba!
13 For ech that is parcenere of mylk, is with out part of the word of riytwisnesse, for he is a litil child.
Aliyense amene amangodya mkaka okha, akanali mwana wakhanda, sakudziwa bwino chiphunzitso cha chilungamo.
14 But of perfit men is sad mete, of hem that for custom han wittis exercisid to discrecioun of good and of yuel.
Koma chakudya cholimba ndi cha anthu okhwima msinkhu, amene pogwiritsa ntchito nzeru zawo, aphunzira kusiyanitsa chabwino ndi choyipa.

< Hebrews 5 >