< Habakkuk 2 >

1 On my kepyng Y schal stonde, and schal pitche a grees on wardyng; and Y schal biholde, that Y se what thing schal be seid to me, and what Y schal answere to hym that repreuith me.
Ndidzakhala pa malo anga aulonda, ndi kuyima pa mitumbira ya nkhondo; ndidzadikira kuti ndimve zimene Iye adzandiwuze, ndi yankho limene ndidzapatsidwe pa madandawulo anga.
2 And the Lord answeride to me, and seide, Write thou the reuelacioun, and make it pleyn on tablis, that he renne, that schal rede it.
Tsono Yehova anandiyankha, nati: “Lemba masomphenyawa ndipo uwalembe mooneka bwino pa mapale kuti wowerenga awawerenge mosavuta.
3 For yit the visioun is fer, and it schal appere in to ende, and schal not lie; if it schal make dwellyng, abide thou it, for it comynge schal come, and schal not tarie.
Pakuti masomphenyawa akudikira nthawi yake; masomphenyawa akunena zamʼtsogolo ndipo sizidzalephera kuchitika. Ngakhale achedwe kukwaniritsidwa, uwayembekezere; zidzachitika ndithu ndipo sadzachedwa.
4 Lo! the soule of hym, that is vnbileueful, schal not be riytful in hym silf; forsothe the iust man schal lyue in his feith.
“Taona, mdani wadzitukumula; zokhumba zake sizowongoka, koma wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.
5 And as wyn disseyueth a man drynkynge, so schal the proude man be, and he schal not be maad feir; for as helle he alargide his soule, and he is as deth, and he is not fillid; and he schal gadere to hym alle folkis, and he shal kepe togidere to hym alle puplis. (Sheol h7585)
Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo; ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika. Pakuti ngodzikonda ngati manda, ngosakhutitsidwa ngati imfa, wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse. (Sheol h7585)
6 Whether not alle these puplis schulen take a parable on hym, and the speking of derk sentencis of hym? And it schal be seid, Wo to hym that multiplieth thingis not his owne; hou longe, and he aggreggith ayens hym silf thicke clei?
“Kodi onse ogwidwawo sadzamunyoza ndi kumunyogodola ponena kuti, “Tsoka kwa amene amadzikundikira katundu amene si wake ndipo amadzilemeretsa ndi chuma cholanda! Kodi izi zidzachitika mpaka liti?
7 Whether not sudeynli thei schulen rise to gidere, that schulen bite thee? And thei schulen be reisid to-teerynge thee, and thou schalt be in to raueyn to hem; and thin aspieris in yuel schulen wake.
Kodi angongole ako sadzakuwukira mwadzidzidzi? Kodi sadzadzuka ndi kukuchititsa mantha? Pamenepo iwe udzalandidwa kalikonse.
8 For thou robbidist many folkis, alle schulen robbe thee, whiche schulen be left of puplis, for blood of man, and for wickidnesse of lond of the citee, and of alle men dwellynge in it.
Pakuti unafunkha mitundu yambiri ya anthu, mitundu ina imene inatsala idzakufunkha iweyo. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
9 Wo to hym that gaderith yuel coueitise to his hous, that his nest be in hiy, and gessith hym for to be delyuered of the hond of yuel.
“Tsoka kwa amene amalemera ndi chuma chochipeza mwachinyengo, kukweza malo ake okhalapo, kuthawa mavuto!
10 Thou thouytist confusioun to thin hous; thou hast slayn many puplis, and thi soule synnede.
Wakonzekera kuwononga mitundu yambiri ya anthu, kuchititsa manyazi nyumba yako yomwe ndi kuwononga moyo wako.
11 For a stoon of the wal schal crie, and a tree that is bitwixe ioynturis of bildyngis schal answere.
Mwala pa khoma udzafuwula, ndipo mitanda ya matabwa idzavomereza zimenezi.
12 Wo to hym that bildith a citee in bloodis, and makith redi a citee in wickidnesse.
“Tsoka kwa amene amanga mzinda pokhetsa magazi ndi kukhazikitsa mzinda pochita zoyipa!
13 Whether not these thingis ben of the Lord of oostis? For puplis schulen trauele in myche fier, and folkis in veyn, and thei schulen faile.
Kodi Yehova Wamphamvuzonse sanatsimikize kuti ntchito za anthu zili ngati nkhuni pa moto, ndi kuti mitundu ya anthu imadzitopetsa popanda phindu?
14 For the erthe schal be fillid, that it knowe the glorie of the Lord, as watris hilynge the see.
Pakuti dziko lapansi lidzadzaza ndi chidziwitso cha ulemerero wa Yehova, monga momwe madzi amadzazira nyanja.
15 Wo to hym that yyueth drynk to his frend, and sendith his galle, and makith drunkun, that he biholde his nakidnesse.
“Tsoka kwa amene amamwetsa anzake zakumwa zoledzeretsa, kutsanula mʼbotolo mpaka ataledzera, kuti aone umaliseche wawo.
16 He is fillid with yuel fame for glorie; and thou drynke, and be aslept; the cuppe of the riythalf of the Lord schal cumpasse thee, and `castynge vp of yuel fame on thi glorie.
Udzachita manyazi mʼmalo mokhala ndi ulemerero. Tsopano ino ndi nthawi yako! Imwa mpaka umaliseche wako uwonekere! Chikho chochokera mʼdzanja lamanja la Yehova chikubwera kwa iwe, ndipo manyazi adzaphimba ulemerero wako.
17 For the wickidnesse of Liban schal kyuere thee, and distruccioun of beestis schal make hem aferd, of bloodis of man, and of wickidnesse of lond, and of the citee, and of alle men dwellynge ther ynne.
Udzathedwa nzeru ndi chiwawa chimene unachita ku Lebanoni, ndiponso udzachita mantha ndi nyama zimene unaziwononga. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
18 What profitith the `grauun ymage, for his makere grauyde it, a wellid thing togidere and fals ymage? for the makere therof hopide in makyng, that he made doumbe symylacris.
“Kodi fano lili ndi phindu lanji, poti analisema ndi munthu, kapena chifanizo chimene chimaphunzitsa mabodza? Pakuti munthu amene walipanga amakhulupirira ntchito ya manja ake; amapanga mafano amene samatha kuyankhula.
19 Wo to hym that seith to a tre, Wake thou; Rise thou, to a stoon beynge stille; whether he schal mow teche? Lo! this is kyuerid with gold and siluer, and no spirit is in his entrails.
Tsoka kwa amene amawuza mtengo kuti, ‘Khala wamoyo!’ Kapena mwala wopanda moyo kuti, ‘Dzuka!’ Kodi zimenezi zingathe kulangiza? Ndi zokutidwa ndi golide ndi siliva; mʼkati mwake mulibe mpweya.
20 Forsothe the Lord is in his hooli temple, al erthe be stille fro his face.
Koma Yehova ali mʼNyumba yake yopatulika; dziko lonse lapansi likhale chete pamaso pake.”

< Habakkuk 2 >