< Genesis 5 >

1 This is the book of generacioun of Adam, in the dai wher ynne God made man of nouyt. God made man to the ymage and licnesse of God;
Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi: Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu.
2 God formede hem male and female, and blesside hem, and clepide the name of hem Adam, in the day in which thei weren formed.
Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.”
3 Forsothe Adam lyuede an hundrid yeer and thretti, and gendride a sone to his ymage and liknesse, and clepide his name Seth.
Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti.
4 And the daies of Adam after that he gendride Seth weren maad eiyte hundrid yeer, and he gendride sones and douytris.
Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
5 And al the tyme in which Adam lyuede was maad nyne hundrid yeer and thretti, and he was deed.
Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira.
6 Also Seth lyuede an hundrid and fyue yeer, and gendride Enos.
Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi.
7 And Seth lyuede aftir that he gendride Enos eiyte hundrid and seuen yeer, and gendride sones and douytris.
Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
8 And alle the daies of Seth weren maad nyne hundrid and twelue yeer, and he was deed.
Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira.
9 Forsothe Enos lyuede nynti yeer, and gendride Caynan;
Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani.
10 aftir whos birthe Enos lyuede eiyte hundrid and fiftene yeer, and gendride sones and douytris.
Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
11 And alle the daies of Enos weren maad nyne hundrid and fyue yeer, and he was deed.
Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira.
12 Also Caynan lyuyde seuenti yeer, and gendride Malalehel.
Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli.
13 And Caynan lyuede after that he gendride Malalehel eiyte hundrid and fourti yeer, and gendride sones and douytris.
Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
14 And alle the dayes of Caynan weren maad nyn hundrid and ten yeer, and he was deed.
Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira.
15 Forsothe Malalehel lyuede sixti yeer and fyue, and gendride Jared.
Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi.
16 And Malalehel lyuede aftir that he gendride Jared eiyte hundrid and thretti yeer, and gendride sones and douytris.
Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
17 And alle the daies of Malalehel weren maad eiyte hundrid nynti and fyue yeer, and he was deed.
Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira.
18 And Jared lyuede an hundrid and two and sixti yeer, and gendride Enoth.
Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki.
19 And Jared lyuede aftir that he gendride Enoth eiyte hundrid yeer, and gendride sones and douytris.
Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
20 And alle the dayes of Jared weren maad nyn hundrid and twei and sexti yeer, and he was deed.
Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.
21 Forsothe Enoth lyuede fyue and sixti yeer, and gendride Matusalem.
Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela.
22 And Enoth yede with God; and Enoth lyuede after that he gendride Matusalem thre hundrid yeer, and gendride sones and douytris.
Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
23 And alle the daies of Enoth weren maad thre hundride and fyue and sexti yeer.
Zaka zonse za Enoki zinali 365.
24 And Enoth yeed with God, and apperide not afterward, for God took hym awei.
Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.
25 Also Matusalem lyuede an hundrid and `fourscoor yeer and seuene, and gendride Lameth.
Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki.
26 And Matusalem lyuede after that he gendride Lameth seuene hundrid and `fourscoor yeer and twei, and gendride sones and douytris.
Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
27 And alle the daies of Matusale weren maad nyn hundrid and nyn and sixti yeer, and he was deed.
Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira.
28 Forsothe Lameth lyuede an hundrid and `fourscoor yeer and two, and gendride a sone;
Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna.
29 and clepide his name Noe, and seide, This man schal comforte vs of the werkis and traueilis of oure hondis, in the loond which the Lord curside.
Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.”
30 And Lameth lyuede after that he gendride Noe fyue hundrid `nynti and fyue yeer, and gendride sones and douytris.
Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
31 And alle the daies of Lameth weren maad seuene hundrid `thre scoor and seuentene yeer, and he was deed.
Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira.
32 Forsothe Noe whanne he was of fyue hundrid yeer gendride Sem, Cham, and Jafeth.
Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.

< Genesis 5 >