< Ezekiel 38 >
1 And the word of the Lord was maad to me,
Yehova anandiyankhula kuti:
2 and he seide, Thou, sone of man, Sette thi face ayens Gog, and ayens the lond of Magog, the prince of the heed of Mosoch and of Tubal; and profesie thou of hym.
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu.
3 And thou schalt seie to hym, The Lord God seith these thingis, A! Gog, lo! Y to thee, prince of the heed of Mosoch and of Tubal;
Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala.
4 and Y schal lede thee aboute, and Y schal sette a bridil in thi chekis, and Y schal leede out thee, and al thin oost, horsis, and horsmen, alle clothid with haburiouns, a greet multitude of men, takynge spere, and scheeld, and swerd.
Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola.
5 Perseis, Ethiopiens, and Libiens with hem, alle ben araied with scheeldis and helmes.
Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo.
6 Gomer, and alle the cumpenyes of hym, the hous of Togorma, the sidis of the north, and al the strengthe therof, and many puplis ben with thee.
Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.
7 Make redi, and araye thee, and al thi multitude which is gaderid to thee, and be thou in to comaundement to hem.
“‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo.
8 Aftir many daies thou schalt be visitid, in the laste of yeeris thou schalt come to the lond, that turnede ayen fro swerd, and was gaderid of many puplis, to the hillis of Israel that weren desert ful ofte; this was led out of puplis, and alle men dwellide tristili ther ynne.
Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere.
9 Forsothe thou schalt stie, and schalt come as a tempest, and as a cloude, for to hile the lond, thou, and alle thi cumpanyes, and many puplis with thee.
Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.
10 The Lord God seith these thingis, In that dai wordis schulen stie on thin herte, and thou schalt thenke the worste thouyt;
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa.
11 and schalt seie, Y schal stie to the lond with out wal, and Y schal come to hem that resten and dwellen sikirli; alle these dwellen with out wal, barris and yatis ben not to hem;
Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo.
12 that thou rauysche spuylis, and asaile prei; that thou brynge in thin hond on hem that weren forsakun, and afterward restorid, and on the puple which is gaderid of hethene men, that bigan to welde, and to be enhabitere of the nawle of erthe.
Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’
13 Saba, and Dedan, and the marchauntis of Tharsis, and alle the liouns therof schulen seie to thee, Whether thou comest to take spuylis? Lo! to rauysche prey thou hast gaderid thi multitude, that thou take awei gold and siluer, and do awei purtenaunce of houshold and catel, and that thou rauysche preyes with out noumbre.
Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’”
14 Therfor profesie thou, sone of man; and thou schalt seie to Gog, The Lord God seith these thingis, Whether not in that dai, whanne my puple Israel schal dwelle tristili, thou schalt wite;
“Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka.
15 and schalt come fro thi place, fro the sidis of the north, thou, and many puplis with thee, alle stieris of horsis, a greet cumpany, and an huge oost;
Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu.
16 and thou as a cloude schalt stie on my puple Israel, that thou hile the erthe? Thou schalt be in the laste daies, and Y schal brynge thee on my lond, that my folkis wite, whanne Y schal be halewid in thee, thou Gog, bifor the iyen of them.
Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.
17 The Lord God seith these thingis, Therfor thou art he of whom Y spak in elde daies, in the hond of my seruauntis, profetis of Israel, that profesieden in the daies of tho tymes, that Y schulde bringe thee on hem.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli.
18 And it schal be, in that dai, in the dai of the comyng of Gog on the lond of Israel, seith the Lord God, myn indignacioun schal stie in my strong veniaunce, and in my feruour;
Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.
19 Y spak in the fier of my wraththe.
Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli.
20 For in that dai schal be grete mouyng on the lond of Israel; and fischis of the see, and beestis of erthe, and briddis of the eir, and ech crepynge beeste which is mouyd on erthe, and alle men that ben on the face of erthe, schulen be mouyd fro my face; and hillis schulen be vndurturned, and heggis schulen falle doun, and ech wal schal falle doun in to erthe.
Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi.
21 And Y schal clepe togidere a swerd ayens hym in alle myn hillis, seith the Lord God; the swerd of ech man schal be dressid ayens his brother.
Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga.
22 And thanne Y schal deme hym bi pestilence, and blood, and greet reyn, and bi greet stoonys; Y schal reyn fier and brymstoon on hym, and on his oost, and on many puplis that ben with hym.
Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye.
23 And Y schal be magnefied, and Y shal be halewid, and Y shal be knowun bifore the iyen of many folkis; and thei schulen wite, that Y am the Lord.
Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’”