< Exodus 9 >

1 Forsothe the Lord seide to Moises, Entre thou to Farao, and speke thou to hym, The Lord God of Ebrews seith these thingis, Delyuere thou my puple, that it make sacrifice to me;
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Pita kwa Farao ndipo ukamuwuze kuti Yehova, Mulungu wa Ahebri akuti alole anthu anga apite kuti akandipembedze.
2 that if thou forsakist yit, and withholdist hem, lo!
Koma ngati ukana kuti apite ndi kupitiriza kuwaletsa,
3 myn hond schal be on thi feeldis, on horsis, and assis, and camels, and oxun, and scheep, a pestilence ful greuous;
dzanja la Yehova lidzakantha ziweto zako zimene zili ku munda, pamodzi ndi akavalo, abulu, ngamira, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi ndi mliri woopsa kwambiri.
4 and the Lord schal make a merueilous thing bitwixe the possessiouns of Israel and the possessiouns of Egipcians, that outirli no thing perische of these thingis that perteynen to the sones of Israel.
Koma Yehova adzasiyanitsa pakati pa ziweto za Israeli ndi ziweto za Igupto, kotero kuti palibe chiweto nʼchimodzi chomwe cha Aisraeli chimene chidzafe.”
5 And the Lord ordeinede a tyme, and seide, To morewe the Lord schal do this word in the lond.
Yehova anayika nthawi ndipo anati, “Yehova adzachita zimenezi mmawa mʼdziko muno.”
6 Therfor the Lord made this word in the tother dai, and alle the lyuynge beestis of Egipcians weren deed; forsothe outirli no thing perischide of the beestis of the sones of Israel.
Ndipo mmawa mwake Yehova anachitadi zimenezi. Ziweto zonse za Aigupto zinafa, koma palibe chiweto ndi chimodzi chomwe cha Aisraeli chomwe chinafa.
7 And Farao sente to se, nether ony thing was deed of these thingis whiche Israel weldide; and the herte of Farao was maad greuouse, and he delyuerede not the puple.
Farao anatuma anthu kuti akafufuze ndipo anapeza kuti palibe chiweto chilichonse cha Aisraeli chomwe chinafa. Komabe mtima wake sunagonje ndipo iye sanalole kuti anthu apite.
8 And the Lord seide to Moises and Aaron, Take ye the hondis ful of askis of the chymeney, and Moises sprynge it in to heuene bifore Farao;
Kenaka Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Tapani phulusa la pa moto lodzaza dzanja ndipo Mose aliwaze mmwamba pamaso pa Farao.
9 and be there dust on al the lond of Egipt; for whi botchis schulen be in men and in werk beestis, and bolnynge bladdris schulen be in al the lond of Egipt.
Phulusalo lidzasanduka fumbi pa dziko lonse la Igupto. Tsono fumbilo lidzasanduka zithupsa zomaphulika nʼkukhala zilonda pa munthu aliyense ndi pa nyama zomwe mʼdziko lonse la Igupto.”
10 And thei token askis of the chymney, and stoden bifore Farao; and Moises spreynt it into heuene; and woundis of bolnynge bladdris weren maad in men, and in werk beestis;
Kotero anatenga phulusa la pa moto ndi kuyima pamaso pa Farao. Mose analiwaza mmwamba, ndipo panabuka zotupa zophulika zokha pa munthu aliyense ndi pa ziweto.
11 and the witchis myyten not stonde bifor Moises, for woundis that weren in hem, and in al the lond of Egipt.
Amatsenga sanathe kumuyandikira Mose chifukwa nawonso anali ndi zithupsa monga mmene analili Aigupto ena onse.
12 And the Lord made hard the herte of Farao, and he herde not hem, as the Lord spak to Moises.
Koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao ndipo iye sanamvere Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova anamuwuzira Mose.
13 Also the Lord seide to Moises, Rise thou eerli, and stonde bifore Farao, and thou schalt seie to hym, The Lord God of Ebrews seth these thingis, Delyuere thou my puple, that it make sacrifice to me;
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mawa mmawa upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso ndipo ukamuwuze kuti Yehova Mulungu wa Ahebri akuti ulole anthu anga apite kuti akandipembedze.
14 for in this tyme Y schal sende alle my veniauncis on thin herte, and on thi seruauntis, and on thi puple, that thou wite, that noon is lijk me in al erthe.
Ngati suwalola, tsopano ndidzagwetsa miliri yanga yonse pa iwe ndi nduna zako ndiponso pa anthu ako, kuti udziwe kuti palibe wina wofanana nane pa dziko lonse lapansi.
15 For now Y schal holde forth the hond, and Y schal smyte thee and thi puple with pestilence, and thou schalt perische fro erthe;
Pakuti ndikanakhala nditatukula kale dzanja langa ndikupheratu iwe pamodzi ndi anthu ako onse pa dziko lapansi.
16 forsothe herfor Y haue set thee, that Y schewe my strengthe in thee, and that my name be teld in ech lond.
Koma ndakuyika kukhala mfumu ndi cholinga choti ndionetse mphamvu zanga kwa iwe ndiponso kuti dzina langa litchuke pa dziko lonse lapansi.
17 Yit thou withholdist my puple, and nylt delyuere it?
Komabe iwe ukudzitukumula pa anthu anga osawalola kuti atuluke.
18 Lo! to morewe in this same our Y schal reyne ful myche hail, which maner hail was not in Egipt, fro the dai in which it was foundid, til in to present tyme.
Nʼchifukwa chake mawa, nthawi ngati ino, ndidzagwetsa matalala amphamvu amene sanagwepo pa Igupto, kuyambira pachiyambi mpaka lero.
19 Therfor sende thou `riyt now, and gadere thi werk beestis, and alle thingis whiche thou hast in the feeld; for men and werk beestis and alle thingis that ben in feeldis with outforth, and ben not gaderid fro the feeldis, and haile falle on tho, schulen die.
Tsopano lamula kuti ziweto zanu zonse ndi zinthu zonse zomwe zili ku minda kuti zilowetsedwe mʼkhola, chifukwa matalala adzagwera munthu aliyense ndi chiweto chilichonse chimene sichidzalowetsedwa mʼkhola ndipo zimene zidzakhala zili ku munda zidzafa.”
20 He that dredde `the Lordis word, of the seruauntis of Farao, made his seruauntis and werk beestis fle in to housis;
Nduna za Farao zinachita mantha ndi mawu a Yehova, ndipo zinalowetsa antchito awo ndi ziweto zawo mʼnyumba.
21 sotheli he that dispiside the `Lordis word, lefte his seruauntis and werk beestis in the feeldis.
Koma iwo amene ananyozera mawu a Yehova anasiya akapolo ndi ziweto zawo panja.
22 And the Lord seide to Moises, Holde forth thin hond in to heuene, that hail be maad in al the lond of Egipt, on men, and on werk beestis, and on ech eerbe of the feeld in the lond of Egipt.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kweza dzanja lako kumwamba kuti matalala agwe pa dziko lonse la Igupto, pa munthu aliyense, pa ziweto ndi pa zonse zomera mʼminda ya Igupto.”
23 And Moises held forth the yerde in to heuene; and the Lord yaf thundris, and hail, and leitis rennynge aboute on the lond; and the Lord reynede hail on the lond of Egipt;
Mose ataloza ndodo yake kumwamba, Yehova anatumiza mabingu ndi matalala ndi ziphaliwali zongʼanima pa nthaka. Kotero Yehova anagwetsa matalala pa dziko la Igupto.
24 and hail and fier meddlid togidere weren borun forth; and it was of so myche greetnesse, how greet apperide neuere bifore in al the lond of Egipt, sithen thilke puple was maad.
Matalala anagwa ndipo ziphaliwali zinangʼanima. Inali mphepo ya mkuntho yoopsa kwambiri imene sinakhaleponso mʼdziko lonse la Igupto chiyambire pamene Aigupto anakhala mtundu woyima pa okha.
25 And the hail smoot in the lond of Egipt alle thingis that weren in the feeldis, fro man til to werk beeste; and the hail smoot al the eerbe of the feeld, and brak al the flex of the cuntrey;
Matalala anawononga dziko lonse la Igupto, munthu aliyense pamodzi ndi ziweto. Matalala aja anawononga zomera zonse za mʼmunda ndi kukhadzula mtengo uliwonse.
26 oonli the hail felde not in the lond of Gessen, where the sones of Israel weren.
Ku malo kokhako kumene matalala sanafikeko ndi dera la Goseni kumene kunali Aisraeli.
27 And Farao sente, and clepide Moises and Aaron, and seide to hem, Y haue synned also now; the Lord is iust, Y and my puple ben wickid;
Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati kwa iwo, “Tsopano ndachimwa, Yehova ndi wolungama, ine ndi anthu anga ndife olakwa.
28 preye ye the Lord, that the thundris and hail of God ceesse, and Y schal delyuere you, and dwelle ye no more here.
Upemphere kwa Mulungu chifukwa mabingu ndi matalala atikwana. Ine ndidzakulolani kuti mupite. Simuyenera kukhalabe kuno.”
29 Moyses seide, Whanne Y schal go out of the citee, Y schal holde forth myn hondis to the Lord, and leitis and thundris schulen ceesse, and hail schal not be, that thou wite, that the lond is the Lordis;
Mose anayankha, “Ndikangotuluka mu mzinda muno, ine ndidzakweza manja anga kwa Yehova ndi kupemphera. Mabingu ndi matalalawa adzaleka ndipo inu mudzadziwa kuti Yehova ndiye akulamulira dziko lapansi.
30 forsothe Y knowe, that thou and thi seruauntis dreden not yit the Lord.
Koma ine ndikudziwa kuti inu ndi nduna zanu simukuopabe Yehova Mulungu.”
31 Therfor the flex and barli was hirt, for the barli was greene, and the flex hadde buriounned thanne knoppis;
Thonje ndi barele zinawonongeka, popeza barele anali atakhwima ndi thonje linali ndi maluwa.
32 forsothe wheete and beenys weren not hirt, for tho weren late.
Koma tirigu ndi mchewere sizinawonongeke chifukwa zimakhwima mochedwa.
33 And Moyses yede out fro Farao, and fro the citee, and helde forth the hondis to the Lord, and thundris and hail ceessiden, and reyn droppide no more on the erthe.
Mose anasiyana ndi Farao natuluka mu mzindawo. Iye anakweza manja ake kwa Yehova. Mabingu ndi matalala zinaleka, ndipo mvula inalekeratu kugwa mʼdzikolo.
34 Sotheli Farao siy that the reyn hadde ceessid, and the hail, and thundris, and he encreesside synne;
Farao ataona kuti mvula, matalala ndi mabingu zaleka, anachimwanso. Iye ndi nduna zake anawumitsanso mitima yawo.
35 and the herte of hym and of hise seruauntis was maad greuouse, and his herte was maad hard greetli; nethir he lefte the sones of Israel, as the Lord comaundide bi `the hond of Moises.
Choncho Farao sanalole kuti Aisraeli apite monga momwe Yehova anamuwuzira Mose.

< Exodus 9 >