< Exodus 28 >

1 Also applie thou to thee Aaron, thi brother, with hise sones, fro the myddis of the sones of Israel, that Aaron, Nadab, and Abyu, Eleazar, and Ythamar, be set in preesthod to me.
“Aaroni mʼbale wako ndi ana ake aamuna, Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara uwapatule pakati pa Aisraeli. Abwere kwa iwe kuti anditumikire monga ansembe.
2 And thou schalt make an hooli clooth to Aaron, thi brother, in to glorie and fairenesse.
Umusokere mʼbale wako, Aaroni, zovala zopatulika kuti azioneka mwaulemerero ndi molemekezeka.
3 And thou schalt speke to alle wise men in herte, whiche Y haue fillid with the spirit of prudence, that thei make clothis to Aaron, in whiche he schal be halewid, and schal mynystre to me.
Uwawuze anthu onse aluso amene Ine ndawapatsa nzeru pa ntchito yosoka kuti apange zovala za Aaroni za pa mwambo womupatula, kuti iye anditumikire monga wansembe.
4 Forsothe these schulen be the clothis, whiche thei schulen make; `thei schulen make racional, and a clooth on the schuldris, a coote, and a streyt lynnun clooth, a mytre, and a girdil; hooli cloothis to Aaron, thi brother, and to hise sones, that thei be set in preesthod to me.
Zovala zoti apange ndi izi: chovala chapachifuwa, efodi, mkanjo, mwinjiro wolukidwa, nduwira ndi lamba. Apangire mʼbale wako Aaroni ndi ana ake aamuna zovala zopatulikazi kuti iwo anditumikire monga ansembe.
5 And thei schulen take gold, and iacynt, and purpur, and `reed selk twies died, and bijs;
Iwo agwiritse ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira ndi yosalala yofewa.
6 forsothe thei schulen make the clooth on the schuldris of gold, and of iacynt, and purpur, and of `reed selk twies died, and of bijs foldid ayen, bi broyderi werk of dyuerse colours.
“Apange efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yolukidwa mwaluso.
7 It schal haue twey hemmes ioyned in euer either side of hiynessis, that tho go ayen in to oon.
Efodiyo ikhale ndi timalamba tiwiri ta pa mapewa tosokerera ku msonga zake ziwiri kuti azitha kumanga.
8 Thilke weuyng, and al dyuersite of the werk schal be of gold, and iacynt, and purpur, and of `reed selk twies died, and bijs foldis ayen.
Lamba womangira efodi akhale wolukidwa mwaluso ngati efodiyo. Akhale wopangidwa ndi golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala.
9 And thou schalt take twei stoonys of onychym, and thou schalt graue in tho the names of the sones of Israel,
“Utenge miyala iwiri ya onikisi ndipo uzokotepo mayina a ana a Israeli.
10 sixe names in o stoon, and sixe othere in the tother stoon, bi the ordre of her birthe;
Mayina asanu ndi limodzi akhale pa mwala umodzi, ndipo mayina asanu ndi limodzi pa mwala winawo motsata mabadwidwe awo.
11 bi the werk of a grauere, and bi the peyntyng of a man that ourneth with gemmes thou schalt graue tho stoonys, with the names of the sones of Israel; and thou schalt enclose and cumpasse in gold.
Mayina a ana a Israeli uwazokote pa miyala iwiriyo, monga momwe amachitira mmisiri wozokota miyala. Ndipo uyike miyalayo mu zoyikamo zake zagolide.
12 And thou schalt sette tho stoonus in euer either side of the cloth on the schuldris, a memorial to the sones of Israel; and Aaron schal bere the names of hem bifor the Lord on euer either schuldre, for remembryng.
Umangirire miyala iwiriyi pa tinsalu ta mʼmapewa ta efodi tija ngati miyala ya chikumbutso cha ana a Israeli. Aaroni azinyamula mayinawo mʼmapewa ake kuti akhale chikumbutso pamaso pa Yehova.
13 And thou schalt make hookis of gold,
Upange zoyikamo za maluwa agolide,
14 and twey litil chaynes of clenneste gold, cleuynge to hem silf togidere, whiche litil chaynes thou schalt sette in the hookis.
ndiponso maunyolo awiri a golide wabwino kwambiri, wopetedwa ngati zingwe ndipo uwalumikize ku zoyikamozo.
15 Also thou schalt make the racional of doom by werk of dyuerse colours, bi the weuyng of the cloth on the schuldre, of gold, iacynt, and purpur, of `reed silk twies died, and of bijs foldid ayen.
“Upange chovala chapachifuwa chogwiritsa ntchito poweruza mlandu ndipo uchipange mwaluso kwambiri. Uchipange ngati efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala ndi yolukidwa bwino.
16 It schal be foure cornerid, and double; it schal haue the mesure of a pawme of the hond, as wel in lengthe, as in breede.
Kutalika kwake kukhale kofanana mbali zonse, mulitali masentimita 23, mulifupi masentimita 23, ndipo chikhale chopinda pawiri.
17 And thou schalt sette ther ynne foure ordris of stoonys; in the firste ordre schal be the stoon sardius, and topazyus, and smaragdus;
Uyikepo mizere inayi ya miyala yokongola kwambiri. Mzere woyamba ukhale ndi miyala ya rubi, topazi ndi berili.
18 in the secunde ordre schal be charbuncle, safir, and iaspis; in the thridde ordre schal be ligurie,
Mzere wachiwiri pakhale miyala ya emeradi, safiro ndi dayimondi;
19 achates, and ametiste;
mzere wachitatu pakhale miyala ya opera, agate ndi ametisiti.
20 in the fourthe ordre schal be crisolitus, onochyn, and berille; tho schulen be closid in gold, bi her ordris,
Mzere wachinayi pakhale miyala ya topazi, onikisi ndi yasipa. Miyalayi uyiike mu zoyikamo zagolide.
21 and schulen haue the names of the sones of Israel: tho schulen be graven with twelue names; al stonus bi hem silf, with the names of the sones `of Israel bi hem silf, bi twelue lynagis.
Miyalayo ikhalepo khumi ndi iwiri, uliwonse kuyimira dzina limodzi la ana a Israeli. Mwala uliwonse uzokotedwe ngati chidindo dzina limodzi la mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
22 Thou schalt make in the racional chaynes cleuynge to hem silf togidere of pureste gold,
“Upange timaunyolo tagolide wabwino kwambiri ta pa chovala chapachifuwa, topota ngati chingwe.
23 and thou schalt make twei goldun ryngis, whiche thou schalt sette in euer either hiynesse of racional.
Upangenso mphete ziwiri zagolide ndipo uzimangirire pa ngodya ziwiri za pa chovala chapachifuwa.
24 And thou schalt ioyne the goldun chaynes with the ryngis that ben in the brynkis therof,
Umangirire timaunyolo tiwiri tagolide tija pa mphete za pa ngodya pa chovala chapachifuwacho.
25 and thou schalt couple the `last thingis of tho chaynes to twey hookis in euer either side of the `cloth on the schuldur, that biholdith the racional.
Ndipo mbali ina ya timaunyoloto umangirire pa zoyikapo zake ziwiri zija ndi kulumikiza pa tinsalu takutsogolo kwa mapewa a efodi.
26 And thou schalt make twei goldun ryngis, whiche thou schalt sette in the hiynesses of the racional, and in the hemmes of the cloth on the schuldur, that ben euene ayens, and biholden the lattere thingis therof.
Upangenso mphete ziwiri zagolide, ndipo uzilumikize ku ngodya ziwiri zamʼmunsi mwa chovala chapachifuwa, champhepete mwake, mʼkati pafupi ndi efodi ija.
27 Also and thou schalt make tweyne othere goldun ryngis, that schulen be set in euer either side of the clooth on the schuldur bynethe, that biholdith ayens the face of the lowere ioynyng, that it may be set couenabli with the `cloth on the schuldre.
Upangenso mphete zina ziwiri zagolide ndipo uzilumikize kumunsi kwa tinsalu takutsogolo kwa efodi, pafupi ndi msoko, pamwamba pangʼono pa lamba wamʼchiwuno wa efodi.
28 And the racional be boundun bi hise ryngis with the ryngis of the `cloth on the schuldre, with a lace of iacynt, that the ioyning maad craftili dwelle, and that the racional and `cloth on the schuldre moun not be departid ech fro other.
Tsono umangirire mphete za pa chovala chapachifuwa zija ku mphete za efodi ndi chingwe chamtundu wa mtambo, kulumikiza lamba ndi chovala chapachifuwacho kuti chovala chapachifuwacho chisalekane ndi efodi.
29 And Aaron schal bere the names of the sones of Israel in the racional of doom on his brest, whanne he entrith in to the seyntuarie, a memorial bifor the Lord with outen ende.
“Pamene Aaroni akulowa kumalo opatulika azivala chovala chapachifuwa cha zoweruzira chija chimene chalembedwa mayina a ana a Israeli kuti Yehova awakumbukire nthawi zonse.
30 Forsothe thou schalt sette in the racional of doom, techyng, and treuthe, whiche schulen be in the brest of Aaron, whanne he entrith bifor the Lord, and he schal bere the doom of the sones of Israel in his brest in the siyt of the Lord euere.
Ndiponso uyike Urimu ndi Tumimu mu chovala chapachifuwa cha zoweruziracho, kuti zikhale pamtima pa Aaroni. Choncho Aaroniyo adzakhala akutenga nthawi zonse zida zomuthandizira kuweruza ana a Israeli pamene adzafika pamaso pa Yehova.
31 And thou schalt make the coote of the `cloth on the schuldre al of iacynt,
“Uyipangire efodiyo mkanjo wamtundu wa mtambo.
32 in whos myddil aboue schal be an hood, and a wouun hemme `bi cumpas therof, as it is wont to be don in the hemmes of clothis, lest it be brokun liytli.
Mkanjowo ukhala ndi malo opisapo mutu pakati pakepo. Pa chibowopo pakhale chibandi chosokedwa mochita ngati kuluka monga muja akhalira malaya kuti chibowocho chilimbe, chisangʼambike.
33 Forsothe bynethe at the feet of the same coote, bi cumpas, thou schalt make as `piyn applis, of iacynt, and purpur, of `reed selk twies died, and of biis foldid ayen; while smale bellis ben medlid in the myddis,
Pa mpendero wamʼmunsi wa mkanjowo, upange mphonje zokhala ngati makangadza za nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira zokhala ndi maberu agolide pakati pake.
34 so that a litil `belle of gold be and a `piyn appil, and eft another litel belle of gold and a `pyn appil.
Choncho pazikhala mphonje imodzi kenaka belu limodzi, kuzungulira mpendero wa mkanjo wonse.
35 And Aaron schal be clothid with that coote in the office of seruyce, that sown be herd, whanne he entrith in to the seyntuarie, and goith out, in the siyt of the Lord; and that he die not.
Aaroni azivala mkanjowo pamene akutumikira ngati wansembe. Kulira kwa maberu kuzimveka pamene akulowa mʼmalo opatulika pamaso pa Yehova ndiponso pamene akutuluka, kuti asafe.
36 And thou schalt make a plate of pureste gold, in which thou schalt graue bi the werk of a grauere, the holi to the Lord.
“Upange duwa lagolide wabwino kwambiri kukhala ngati chidindo ndipo uzokotepo mawu akuti, Cohoperekedwa kwa Yehova.
37 And thou schalt bynde that plate with a lace of iacynt, and it schal be on the mytre,
Ulimange ndi chingwe cha nsalu yamtundu wa mtambo pa nduwira ya Aaroni, ndipo duwalo likhale kutsogolo kwa nduwirayo.
38 and schal neiye the forheed of the bischop. And Aaron schal bere the wickidnessis of hem whiche the sones of Israel `offeriden, and halewiden in alle her yiftis and fre yiftis; forsothe the plate schal euere be in `his forhed, that the Lord be plesid to him.
Lidzakhala pa mphumi ya Aaroni, motero iye adzasenza cholakwa chilichonse cha pa zopereka zilizonse zimene Aisraeli amazipatulira Yehova. Aaroni azivala chikwangwanichi pa mphumi pake nthawi zonse kuti Yehova alandire zopereka za anthu ake.
39 And thou schalt bynde the coot of biis, and the myter of bijs, and thou schalt make also a girdil, `bi werk of broiderye.
“Uluke mwinjiro wa nsalu yofewa yosalala ndiponso upange nduwira ya nsalu yofewa yosalala. Lamba wake akhale wolukidwa bwino ndi munthu waluso.
40 Forsothe thou schalt make redi to `the sones of Aaron linnun cootis, and girdlis, and mytris, in to glorie and fairnesse.
Upangirenso ana a Aaroni mwinjiro, malamba ndi nduwira kuti azioneka mwaulemu ndi molemekezeka.
41 And thou schalt clothe Aaron, thi brother, with alle these, and hise sones with hym. And thou schalt sacre the hondis of alle; and thou schalt halewe hem, that thei be set in preesthood to me.
Zovala zimenezi umuveke Aaroni, mʼbale wako ndi ana ake. Kenaka uwadzoze, uwapatse udindo ndi kuwapatula kuti anditumikire ngati ansembe anga.
42 Also thou schalt make lynnun brechis, that thei hile the fleisch of her filthe fro the reynes `til to the hipis.
“Uwapangire akabudula a nsalu yofewa oyambira mʼchiwuno kulekeza mʼntchafu kuti asamaonetse maliseche.
43 And Aaron and hise sones schulen vse tho, whanne thei schulen entre in to the tabernacle of witnessyng, ether whanne thei neiyen to the auter, that thei mynystren in the seyntuarie, lest thei ben gilti of wickidnesse, and dien; it schal be a lawful thing euerlastynge to Aaron, and to his seed after hym.
Aaroni ndi ana ake ayenera kuvala akabudulawo pamene akulowa mu tenti ya msonkhano kapena pamene akupita ku guwa lansembe kukatumikira malo oyera kuopa kuti angachimwe ndi kufa. “Ili likhale lamulo la nthawi zonse kwa Aaroni ndi zidzukulu zake.”

< Exodus 28 >