< Exodus 27 >

1 Also thou schalt make an auter of the trees of Sechym, which schal haue fyue cubitis in lengthe, and so many in brede, that is, sqware, and thre cubitis in heiythe.
“Upange guwa lansembe lamatabwa amtengo wa mkesha. Likhale lofanana mbali zonse, msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi mwake masentimita 229.
2 Forsothe hornes schulen be bi foure corneris therof; and thou schalt hile it with bras.
Upange nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo kuti nyangazo ndi guwalo zikhale chinthu chimodzi, ndipo ulikute guwalo ndi mkuwa.
3 And thou schalt make in to the vsis of the auter pannes, to resseyue aischis, and tongis, and fleisch hookis, and resettis of fyris; thou schalt make alle vessilis of bras.
Upange ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika yochotsera phulusa, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
4 And thou schalt make a brasun gridele in the maner of a net, and bi four corneris therof schulen be foure brasun ryngis,
Upange sefa yachitsulo chamkuwa ndipo mʼngodya zake zinayizo upangiremo mphete zamkuwa.
5 whiche thou schalt putte vndur the yrun panne of the auter; and the gridele schal be til to the myddis of the auter.
Uyike sefayo mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, ndipo ilekezere pakati pa guwa lansembelo.
6 And thou schalt make twey barris of the auter, of the trees of Sechym, whiche barris thou schalt hile with platis of bras;
Upange nsichi zamtengo wa mkesha ndipo uzikutire ndi mkuwa.
7 and thou schalt lede yn `the barris bi the cerclis, and tho schulen be on euer eithir side of the auter, to bere.
Pamene mukunyamula guwalo, muzilowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo.
8 Thou schalt make that auter not massif, but voide, and holowe with ynne, as it was schewid to thee in the hil.
Guwalo likhale lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake. Ulipange monga momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
9 Also thou schalt make a large street of the tabernacle, `in the maner of a chirche yeerd, in whos mydday coost ayens the south schulen be tentis of bijs foldid ayen; o side schal holde an hundrid cubitis in lengthe,
“Upange bwalo la chihema. Mbali yakummwera ikhale yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
10 and twenti pileris, with so many brasun foundementis, whiche pileris schulen haue silueren heedis with her grauyngis.
Upangenso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa, ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
11 In lijk maner in the north side, bi the lengthe, schulen be tentis of an hundrid cubitis, twenti pileris, and brasun foundementis of the same noumbre; and the heedis of tho pileris with her grauyngis schulen be of siluer.
Mbali yakumpoto ikhalenso yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga. Pakhalenso mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
12 Forsothe in the breede of the large street, that biholdith to the west, schulen be tentis bi fifti cubitis, and ten pileris schulen be, and so many foundementis.
“Mbali yakumadzulo ya bwalolo ikhale yotalika mamita 23 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga, nsichi khumi ndi matsinde khumi.
13 In that breede of the large street, that biholdith to the eest, schulen be fifti cubitis,
Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, kutalika kwa bwalo kukhale mamita 23.
14 in whiche the tentis of fiftene cubitis schulen be assigned to o side, and thre pileris, and so many foundementis;
Mbali imodzi yachipata kukhale nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu.
15 and in the tother side schulen be tentis holdynge fiftene cubitis, and thre pileris, and so many foundementis.
Ndipo ku mbali inayo kukhale nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
16 Forsothe in the entryng of the `greet strete schal be maad a tente of twenti cubitis, of iacynt, and purpur, and of reed selk twies died, and of bijs foldid ayen bi broideri werk; it schal haue four pileris, with so many foundementis.
“Pa chipata cha bwalolo pakhale nsalu yotchinga yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira ndiponso yofewa yosalala. Nsaluyo ikhale yotalika mamita asanu ndi anayi, yopangidwa ndi anthu aluso. Pakhalenso mizati yake inayi ndi matsinde akenso anayi.
17 Alle the pileris of the grete street bi cumpas schulen be clothid with platis of siluer, with hedis of siluer, and with foundementis of bras.
Mizati yonse yozungulira bwalolo ilumikizidwe ndi zingwe zasiliva. Ngowe zake zikhale zasiliva, koma matsinde ake akhale amkuwa.
18 The greet street schal ocupie an hundrid cubitis in lengthe, fifti in breede; the hiyenesse of the tente schal be of fiue cubitis; and it schal be maad of bijs foldid ayen; and it schal haue brasun foundementis.
Kutalika kwa bwalolo kukhale mamita 46, mulifupi mwake mamita 23, msinkhu wake masentimita 230. Nsalu ya katani ikhale yofewa ndi yosalala bwino. Matsinde ake akhale amkuwa.
19 Thou schalt make of bras alle the vesselis of the tabernacle, in to alle vsis and cerymonyes, as wel stakis therof, as of the greet street.
Zipangizo zonse zogwiritsa ntchito zosiyanasiyana pa chihemacho, zikhomo za chihema ndi zabwalolo zikhale zamkuwa.
20 Comaunde thou to the sones of Israel, that thei brynge to thee the clenneste oile of `the trees of olyues, and powned with a pestel, that a lanterne
“Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
21 brenne euere in the tabernacle of witnessyng with out the veil, which is hangid in the tabernacle of witnessyng; and Aaron and hise sones schulen sette it, that it schyne bifore the Lord til the morewtid; it schal be euerlastynge worschiping bi her successiouns of the sones of Israel.
Mʼchihema cha msonkhano, koma kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, Aaroni ndi ana ake azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pakati pa Aisraeli pa mibado yonse.”

< Exodus 27 >