< Exodus 2 >

1 Aftir these thingis a man of `the hows of Leuy yede out, and took a wijf of his kyn,
Ndipo munthu wina wa fuko la Levi anakwatira mkazi wa fuko lomwelo.
2 which conseyuede, and childide a sone. And sche seiy hym wel farynge, and hidde him bi thre monethis.
Mkaziyo anatenga pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Ataona kuti mwanayo anali wokongola, anamubisa kwa miyezi itatu.
3 And whanne sche myyte not hele, thanne sche took a `leep of segge, and bawmede it with tar and pitch, and puttide the yong child with ynne, and puttide hym forth in a `place of spier of the brenke of the flood,
Koma mwanayo atafika pa msinkhu woti sakanathanso kubisidwa, amayi ake anatenga kadengu kopangidwa ndi bango nakamata phula. Kenaka anayika mwanayo mʼmenemo ndi kukamuyika pa mabango mu mtsinje wa Nailo.
4 the while his sistir stood afer, and bihelde the bifalling of the thing.
Mlongo wake wa mwanayo anayima pataliko kuti aone chimene chidzamuchitikira mwanayo.
5 Lo! forsothe the douytir of Farao cam doun to be waischun in the flood, and hir damysels walkiden bi the brenke of the flood. And whanne sche hadde seyn a leep in the `place of spier, sche sente oon of hir seruauntessis,
Mwana wamkazi wa Farao anapita ku mtsinje wa Nailo kukasamba ndipo adzakazi ake ankayenda mʼmbali mwa mtsinjewo. Tsono mwana wa Farao uja anaona kadenguko pakati pa mabango ndipo anatuma mdzakazi wake kuti akakatenge.
6 and sche openyde the leep brouyt to hir, and seiy a litil child wepynge ther ynne. And sche hadde mercy on the child, and seide, It is of the yonge children of Ebrews.
Iye atavundukula anaona mwana wamwamuna akungolira. Iye anamva naye chisoni mwana uja, nati, “Ameneyu ndi mmodzi mwa ana a Chihebri.”
7 To whom the `sister of the child seide, Wolt thou that Y go, and clepe to thee an Ebrew womman, that may nurische the yong child?
Kenaka mlongo wake wa mwanayo anafunsa mwana wa Farao kuti, “Ndingapite kukakupezerani mmodzi mwa amayi a Chihebri kuti azikakulererani mwanayu?”
8 She answeride, Go thou. The damysel yede, and clepide the `modir of the child.
Iye anayankha kuti, “Inde, pita.” Ndipo mtsikanayo anapita nakayitana amayi a mwanayo.
9 To whom `the douytir of Farao spak, and seide, Take thou this child, and nurische to me; Y schal yyue to thee thi mede. The womman took, and nurischide the child, and bitook hym woxun to `the douytir of Farao,
Mwana wa Farao anati, “Tengani mwanayu mukandilerere, ndidzakulipirani.” Mayiyo anatenga mwanayo kukamulera.
10 whom sche purchaside `in to the place of sone; and sche clepide his name Moises, and seide, For Y took hym fro the watir.
Mwanayo atakula anakamupereka kwa mwana wa Farao ndipo anakhala mwana wake. Iye anamutcha dzina lake Mose, popeza anati, “Ndinamuvuwula mʼmadzi.”
11 In tho daies, aftir that Moises encreesside, he yede out to hise britheren, and seiy the turment of hem, and a man Egipcian smytynge `oon of Ebrews, hise britheren.
Tsiku lina, Mose atakula, anapita kumene kunali anthu a mtundu wake ndipo anawaona akugwira ntchito yowawa. Iye anaona Mwigupto akumenya Mhebri, mmodzi mwa anthu a mtundu wake.
12 And whanne he hadde biholdun hidur and thidir, and hadde seyn, that no man was present, he killide the Egipcian, and hidde in soond.
Atayangʼana uku ndi uku, naona kuti panalibe wina aliyense, Mose anamupha Mwiguptoyo ndipo anamukwirira mu mchenga.
13 And he yede out in another dai, and seiy tweyne Ebrews chidynge, and he seide to hym that dide wrong, Whi smytist thou thi brother?
Mmawa mwake Mose anapita ndipo anaona anthu awiri a Chihebri akumenyana. Iye anafunsa amene anali wolakwa kuti, “Chifukwa chiyani ukumenya Mhebri mnzako?”
14 Which answeride, Who ordeynede thee prince, ether iuge on vs? Whether thou wolt sle me, as thou killidist yisterdai the Egipcian? Moises dredde, and seide, Hou is this word maad opun?
Munthu uja anati, “Kodi ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza? Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja?” Mose anachita mantha ndipo anati mu mtima mwake, “Chimene ndinachita chija chadziwika.”
15 And Farao herde this word, and souyte to sle Moyses, which fledde fro his siyt, and dwellide in the lond of Madian, and sat bisidis a pit.
Farao atamva zimenezi anafuna kuti aphe Mose, koma Mose anathawa ndipo anapita kukakhala ku Midiyani. Ali kumeneko, tsiku lina anakhala pansi pafupi ndi chitsime.
16 Forsothe seuene douytris weren to the preest of Madian, that camen to drawe watir; and whanne the trouyis weren fillid, thei coueitiden to watere `the flockis of her fadir.
Wansembe wa ku Midiyaniko anali ndi ana aakazi asanu ndi awiri. Iwowa anabwera kudzatunga madzi ndi kudzaza mu zomwera kuti amwetse nkhosa za abambo awo.
17 Scheepherdis camen aboue, and dreuen hem awei; and Moises roos, and defendide the dameselis; and he watride `the scheep of hem.
Koma kunabwera abusa ena amene anathamangitsa atsikana aja. Ndiye Mose anayimirira nawathandiza atsikana aja ndi kumwetsa nkhosa zawo.
18 And whanne thei hadden turned ayen to Jetro, her fadir, he seide to hem, Whi camen ye swiftliere than ye weren wont?
Atsikana aja atabwerera kwa abambo awo Reueli, iye anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani lero mwabwera msanga?”
19 Thei answeriden, A man of Egipt delyuerede vs fro the hond of scheepherdis; ferthermore and he drow watir with vs, and yaf drynk to the scheep.
Atsikanawo anayankha kuti, “Mwigupto wina ndiye watilanditsa kwa abusa. Ndiponso anatitungira madzi ndi kumwetsa ziweto zathu.”
20 And he seide, Where is that man? whi leften ye the man? clepe ye hym, that he ete breed.
Tsono Reueli anafunsa ana ake kuti, “Ndiye ali kuti munthuyo? Chifukwa chiyani mwamusiya? Kamuyitaneni kuti adzadye.”
21 Therfor Moises swoor, that he wolde dwelle with Jetro; and he took a wijf, Sefora, `the douyter of Jetro.
Mose anavomera kukhala ndi Reueli, ndipo anamupatsa Zipora kuti akhale mkazi wake.
22 And sche childide a sone to hym, whom he clepide Gersan, and seide, Y was a comelyng in an alyen lond. Forsothe sche childide an othir sone, whom he clepide Eliezer, and seide, For God of my fadir is myn helpere, and delyuerede me fro the hond of Farao.
Zipora anabereka mwana wa mwamuna amene Mose anamutcha Geresomu, popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko la eni.”
23 Forsothe aftir myche tyme the kyng of Egipt diede, and the sones of Israel inwardli weiliden for werkis, and crieden, and the cry of hem for werkis stiede to God.
Nthawi yonseyo nʼkuti ana a Israeli akulira chifukwa cha ukapolo wawo uja. Iwo anafuwula kupempha thandizo, ndipo kulira kwawoko kunafika kwa Mulungu.
24 And he herde the weilyng of hem, and he hadde mynde of the boond of pees, which he hadde maad with Abraham, Ysaac, and Jacob; and he bihelde the sones of Israel,
Mulungu anamva kubuwula kwawo ndipo anakumbukira pangano lake ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
25 and knewe hem.
Mulungu ataona Aisraeli aja ndi masautso awo, Iye anawamvera chifundo.

< Exodus 2 >