< Exodus 19 >
1 In the thridde monethe of the goyng `of Israel out of the lond of Egipt, in this dai thei camen in to the wildirnesse of Synai;
Ana a Israeli aja anafika ku chipululu cha Sinai pa tsiku loyamba la mwezi wachitatu chichokere mʼdziko la Igupto.
2 for thei yeden forth fro Rafidym, and camen til in to deseert of Synai, and settiden tentis in the same place; and there Israel settide tentis, euen ayens the hil.
Atachoka ku Refidimu, anafika ku Sinai, ndipo Aisraeli anamangako misasa yawo moyangʼanana ndi phirilo.
3 Forsothe Moises stiede in to the hil to God; and the Lord clepide hym fro the mount, and seide, Thou schalt seie these thingis to the hows of Jacob, and thou schalt telle to the sones of Israel,
Mose anakwera ku phiri kukakumana ndi Mulungu ndipo Yehova anamuyitana nati, “Ukawuze zidzukulu za Yakobo, ana onse a Israeli kuti,
4 Ye silf han seyn what thingis Y haue do to Egipcians, how Y bar you on the wengis of eglis, and took to me.
‘Inu eni munaona zimene ndinawachitira Aigupto ndiponso mmene ndinakunyamulirani, monga mmene chiwombankhanga chimanyamulira ana ake pa mapiko,’ ndikukubweretsani kwa Ine.
5 Therfor if ye schulen here my vois, and schulen kepe my couenaunt, ye schulen be to me in to a specialte of alle puplis; for al the lond is myn;
Tsopano, ngati mumveradi mawu anga ndi kusunga pangano langa, mudzakhala chuma changa chapamtima pakati pa mitundu yonse. Ngakhale kuti dziko lonse lapansi ndi langa,
6 and ye schulen be to me in to a rewme of preesthod, and `ye schulen be an hooli folk; these ben the wordis whiche thou schalt speke to the sones of Israel.
inu mudzakhala ansembe achifumu ndi mtundu woyera mtima. Awa ndi mawu amene uyenera kuwawuza Aisraeli.”
7 Moyses cam, and whanne the gretter men in birthe of the puple weren clepid to gidere, he expownede alle the wordis whiche the Lord comaundide.
Ndipo Mose anabwerera ndi kuyitanitsa akuluakulu. Atabwera anawafotokozera mawu amene Yehova anamulamulira kuti adzanene.
8 And alle the puple answeride to gidere, We schulen do alle thingis whiche the Lord spak. And whanne Moises hadde teld the wordis of the puple to the Lord,
Anthu onse anayankha pamodzi kuti, “Ife tidzachita zonse zimene Yehova wanena.” Choncho Mose anabweza yankho lawo kwa Yehova.
9 the Lord seide to hym, Riyt now Y schal come to thee in a derknesse of a cloude, that the puple here me spekynge to thee, and bileue to thee withouten ende. Therfor Moises telde the wordis of the puple to the Lord,
Yehova anati kwa Mose, “Ine ndibwera kwa iwe mu mtambo wakuda kuti anthu adzandimve ndikuyankhula ndi iwe. Choncho adzakukhulupirira nthawi zonse.” Kenaka Mose anawuza Yehova zimene anthu ananena.
10 which seide to Moises, Go thou to the puple, and make hem holi to dai and to morewe, and waische thei her clothis,
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Pita kwa anthu onse ndi kuwayeretsa lero ndi mawa. Achape zovala zawo
11 and be thei redi in to the thridde dai; for in the thridde dai the Lord schal come doun bifore al the puple on the hil of Synai.
ndipo akhale atakonzeka pofika tsiku lachitatu, chifukwa tsiku limenelo Yehova adzatsika pa phiri la Sinai anthu onse akuona.
12 And thou schalt sette termes to the puple, bi cumpas; and thou schalt seie to hem, Be ye war, that ye `stie not in to the hil, nether touche ye the endis therof; ech man that schal touche the hil, schal die bi deeth.
Uwalembere malire anthuwo kuzungulira phirilo ndipo uwawuze kuti, ‘Samalani musakwere phirilo kapena kukhudza tsinde lake. Aliyense wokhudza phiri adzaphedwa ndithu.
13 Hondis schulen not touche hym, but he schal be oppressid with stoonus, ethir he shall be persid with dartis; whether it schal be a beest, ethir a man, it schal not lyue; whanne a clarioun schal bigynne to sowne, thanne `stie thei in to the hil.
Aliyense wokhudza phiri adzaphedwa ndi miyala kapena kumulasa ndi mivi. Palibe amene adzamukhudze. Palibe munthu amene adzaloledwa kukhala ndi moyo ngakhale nyama. Iwo adzayenera kuphedwa.’ Koma anthu adzapita ku phirilo akadzamva kulira kwa lipenga la nyanga yankhosa.”
14 And Moises cam doun fro the hil to the puple, and halewide it; and whanne thei hadden waischun her clothis,
Tsono Mose anatsika phiri lija nafika kwa anthu aja ndi kuwayeretsa. Iwo anachapa zovala zawo.
15 he seide to hem, Be ye redi in to the thridde dai, neiye ye not to youre wyues.
Kenaka iye anati kwa anthu, “Konzekerani tsiku lachitatu, musagone pamodzi ndi mkazi.”
16 And now the thridde day was comun, and the morewetid was cleer; and, lo! thundris bigunnen to be herd, and leitis to schyne, and a moost thicke cloude to hile the mounteyn; and `the sownyng of a clarioun made noise ful greetli, and the puple dredde, that was in the castels.
Mʼmamawa wa tsiku lachitatu kunali mabingu, ziphaliwali ndi mtambo wakuda umene unaphimba phiri, ndiponso lipenga lolira kwambiri. Aliyense ku misasa kuja ananjenjemera ndi mantha.
17 And whanne Moises hadde led hem out in to the comyng of God, fro the place of castels, thei stoden at the rootis of the hil.
Ndipo Mose anatsogolera anthu kutuluka mʼmisasa kukakumana ndi Mulungu, ndipo anayima mʼmunsi mwa phiri.
18 Forsothe al the hil of Synai smokide, for the Lord hadde come doun theronne in fier; and smoke stiede therof as of a furneis, and al the hil was ferdful;
Phiri la Sinai linakutidwa ndi utsi, chifukwa Yehova anatsika ndi moto pa phiripo. Utsi unakwera ngati wochokera mʼngʼanjo yamoto ndipo phiri lonse linagwedezeka kwambiri.
19 and the `sown of a clarioun encreesside litil and litil, and was holdun forth lengere. Moises spak, and the Lord answeride to hym,
Liwu la lipenga linkakulirakulira. Tsono Mose anayankhula ndipo Yehova anamuyankha ndi mabingu.
20 and the Lord cam doun on the hil of Synay, in thilke cop of the hil, and clepide Moises to the cop therof. And whanne he hadde stied thidur,
Yehova anatsika nafika pamwamba pa phiri la Sinai, ndipo anayitana Mose kuti apite pa phiripo. Choncho Mose anakwera,
21 the Lord seide to hym, Go thou doun, and witnesse thou to the puple, lest perauenture it wole passe the termes to se the Lord, and ful greet multitude therof perische;
ndipo Yehova anati kwa iye, “Tsika ukawachenjeze anthu kuti asayesere kudutsa malire kuti adzandione chifukwa ambiri a iwo adzafa.
22 also preestis, that neiyen to the Lord, be halewid, lest Y smyte hem.
Ngakhale ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova ayenera kudziyeretsa kuopa kuti ndingadzawalange.”
23 And Moises seide to the Lord, The comyn puple may not stie in to the hil of Synai; for thou hast witnessid, and hast comaundid, seiyinge, Sette thou termes aboute the hil, and halewe it.
Mose anati kwa Yehova, “Anthu sangakwere phiri la Sinai chifukwa inu munatichenjeza. Lembani malire kuzungulira phiri ndipo mulipatule kuti likhale loyera.”
24 To whom the Lord seide, Go thou doun, and thou schalt stie, and Aaron with thee; forsothe the preestis and the puple passe not the termes, nethir stie thei to the Lord, lest perauenture he sle hem.
Yehova anayankha, “Tsika ukamutenge Aaroni. Koma ansembe ndi anthu asayesere kubzola malire kuti abwere kwa Yehova chifukwa Iye adzawalanga.”
25 Moises yede doun to the puple, and telde alle thingis to hem.
Ndipo Mose anatsika ndi kukawawuza anthuwo.