< Ecclesiastes 11 >

1 Sende thi breed on watris passynge forth, for aftir many tymes thou schalt fynde it.
Ponya chakudya chako pa madzi, udzachipezanso patapita masiku ambiri.
2 Yyue thou partis seuene, and also eiyte; for thou woost not, what yuel schal come on erthe.
Ndalama zako uzisungitse kwa anthu asanu ndi awiri, inde kwa anthu asanu ndi atatu, pakuti sudziwa ndi tsoka lanji limene likubwera pa dziko.
3 If cloudis ben filled, tho schulen schede out reyn on the erthe; if a tre fallith doun to the south, ether to the north, in what euer place it fallith doun, there it schal be.
Ngati mitambo yadzaza ndi madzi, imagwetsa mvula pa dziko lapansi. Mtengo ukagwera cha kummwera kapena cha kumpoto, ndiye kuti udzagonera kumene wagwerako.
4 He that aspieth the wynd, sowith not; and he that biholdith the cloudis, schal neuere repe.
Amene amayangʼana mphepo sadzadzala; amene amayangʼana mitambo sadzakolola.
5 As thou knowist not, which is the weye of the spirit, and bi what resoun boonys ben ioyned togidere in the wombe of a womman with childe, so thou knowist not the werkis of God, which is makere of alle thingis.
Momwe sudziwira mayendedwe a mphepo, kapena momwe mzimu umalowera mʼthupi la mwana mʼmimba mwa amayi, momwemonso sungathe kudziwa ntchito za Mulungu, Mlengi wa zinthu zonse.
6 Eerli sowe thi seed, and thin hond ceesse not in the euentid; for thou woost not, what schal come forth more, this ethir that; and if euer eithir cometh forth togidere, it schal be the betere.
Dzala mbewu zako mmawa ndipo madzulo usamangoti manja lobodo, pakuti sudziwa chimene chidzapindula, mwina ichi kapena icho, kapena mwina zonse ziwiri zidzachita bwino.
7 The liyt is sweet, and delitable to the iyen to se the sunne.
Kuwala nʼkwabwino, ndipo maso amasangalala kuona dzuwa.
8 If a man lyueth many yeeris, and is glad in alle these, he owith to haue mynde of derk tyme, and of many daies; and whanne tho schulen come, thingis passid schulen be repreued of vanyte.
Munthu akakhala wa zaka zambiri, mulekeni akondwerere zaka zonsezo, koma iye azikumbukira masiku a mdima, pakuti adzakhala ochuluka. Chilichonse chimene chikubwera ndi chopanda phindu.
9 Therfor, thou yonge man, be glad in thi yongthe, and thin herte be in good in the daies of thi yongthe, and go thou in the weies of thin herte, and in the biholdyng of thin iyen; and wite thou, that for alle these thingis God shal brynge thee in to doom.
Kondwera mnyamata iwe, pamene ukanali wamngʼono, ndipo mtima wako usangalale pa nthawi ya unyamata wako. Tsatira zimene mtima wako ukufuna, ndiponso zimene maso ako akuona, koma dziwa kuti pa zinthu zonsezo Mulungu adzakuweruza.
10 Do thou awei ire fro thin herte, and remoue thou malice fro thi fleisch; for whi yongthe and lust ben veyne thingis.
Choncho uchotse zokusautsa mu mtima mwako, upewe zokupweteka mʼthupi mwako, pakuti unyamata ndi ubwana ndi zopandapake.

< Ecclesiastes 11 >