< Deuteronomy 7 >
1 Whanne thi Lord God hath lad thee in to the lond, in to which thou schalt entre to welde, and hath do awey many folkis bifor thee, Ethei, and Gergesei, and Ammorrey, Canenei, and Pherezei, Euey, and Jebusei; seuene folkis, of myche gretter noumbre than thou art, and strengere than thou;
Pamene Yehova Mulungu wanu wakufikitsani mʼdziko limene mukukalowa ndi kulilanda ndi kuthamangitsa pamaso panu mitundu ya anthu iyi: Ahiti, Agirigasi, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi; yomwe ndi mitundu isanu ndi iwiri yayikulu ndi yamphamvu kuposa inu;
2 and thi Lord God hath bitake hem to thee, thou schalt smyte hem `til to deeth, thou schalt not make `with hem a boond of pees, nether thou schalt haue merci on hem,
Yehova Mulungu wanu akadzawapereka mʼmanja mwanu, ndipo inu mukadzawagonjetsa, mudzawawononge kwathunthu. Musadzachite mgwirizano ndi anthuwo ndiponso musadzawachitire chifundo.
3 nether thou schalt felowschipe mariagis with him; thou schalt not yyue thi douyter to the sone `of hym, nether thou schalt take his douytir to thi sone;
Musadzakwatirane nawo. Musadzapereke ana anu aakazi kwa ana awo aamuna kapena kutenga ana anu aamuna ndi kuwapereka kwa ana awo aakazi.
4 for sche schal disceyue thi sone, that he sue not me, and that he serue more alien goddis; and the strong veniaunce of the Lord schal be wrooth, and schal do awei thee soone.
Mukadzatero, iwo adzasocheretsa ana anu aamuna kuti asanditsatire ndi kutumikira milungu ina. Motero Yehova adzakukwiyirani ndi kukuwonongani mwachangu.
5 But rather thou schalt do these thingis to hem; destrie ye the auteris `of hem, and breke ye ymagis `of metal, and kitte ye doun wodis, and brenne ye grauun ymagis.
Koma mukachite izi: Mukagumule maguwa awo ansembe, mukaswe miyala yawo yachipembedzo, mukadule mitengo yawo ya Asera, ndi kutentha mafano awo pa moto.
6 For thou art an hooli puple to thi Lord God; thi Lord God chees thee, that thou be a special puple to hym, of alle puplis that ben on erthe.
Pakuti inu ndinu anthu opatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Yehova Mulungu wanu anakusankhani pakati pa anthu onse pa dziko lapansi kuti mukhale ake, chuma chake cha mtengo wapatali.
7 Not for ye ouercamen in noumbre alle folkis, the Lord is ioyned to you, and chees yow, sithen ye ben fewere than alle puplis;
Yehova sanakukondeni chifukwa choti munali ochuluka kuposa ena pakuti inuyo ndiye munali ochepetsetsa mwa anthu onse.
8 but for the Lord louede you, and kepte the ooth which he swoor to youre fadris; and he ledde you out in strong hond, and ayen bouyte you fro the hows of seruage, fro `the hows of Farao, kyng of Egipt.
Koma chifukwa chakuti Yehova anakukondani nasunga lumbiro lake limene analumbira kwa makolo anu. Ndi chifukwa chake anakutulutsani ndi mphamvu yake yopanda malire ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo, kuchoka mʼmanja mwa Farao mfumu ya ku Igupto.
9 And thou schalt wite, that thi Lord God hym silf is a strong God, and feithful, and kepith couenaunt and mersi to hem that louen hym, and to hem that kepen hise comaundementis, in to a thousynde generaciouns;
Choncho dziwani kuti Yehova Mulungu wanu, ndi Mulungu. Iye ndi Mulungu wokhulupirika, wosunga pangano lake la chikondi chosasinthika ku mibadomibado, kwa iwo amene amamukonda nasunga malamulo ake.
10 and yeldith anoon to hem that haten hym, so that he destrie hem, and differr no lengere; restorynge anoon to hem that that thei disseruen.
Koma iwo amene amamuda adzawabwezera powawononga pamaso pawo; sadzachedwa kuwabwezera iwo amene amadana naye.
11 Therfor kepe thou the comaundementis, and cerymonyes, and domes, whiche Y comaunde to thee to dai, that thou do.
Choncho muziyesetsa kusunga malamulo, malangizo ndi maphunziro amene ndikukulamulani lero lino kuti muchite.
12 If aftir that thou herist these domes, thou kepist, and doist tho, thi Lord God schal kepe to thee couenaunt, and mersi, which he swoor to thi fadris.
Mukamvera malamulo amenewa, ndi kusamala kuwatsata, ndiye kuti Yehova Mulungu wanu adzasunga pangano lake la chikondi chosasinthika ndi inu, monga analumbira kwa makolo anu.
13 And he schal loue thee, and schal multiplie thee, and he schal blesse the fruyt of thi wombe, and the fruyt of thi lond, thi wheete, and vindage, oile, and droues of beestis, and the flockis of thi scheep, on the lond for which he swoor to thi fadris, that he schulde yyue it to thee.
Iye adzakukondani nakudalitsani ndi kukuchulukitsani. Adzadalitsa chipatso cha mʼmimba mwanu, zokolola za mʼdziko mwanu, tirigu wanu, vinyo wanu ndi mafuta anu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu mʼdziko limene analumbirira kwa makolo anu kuti akupatseni inu.
14 Thou schalt be blessid among alle puplis; noon bareyn of euer eithir kynde schal be at thee, as well in men, as in thi flockis.
Inu mudzadalitsika kuposa mtundu wina uliwonse wa anthu ndipo palibe mwamuna kapena mkazi aliyense pakati panu amene adzakhale wosabereka. Ziweto zanu nazonso, sipadzapezeka zosabereka.
15 The Lord schal do awei fro thee all ache, `ether sorewe; and he schal not brynge to thee the worste siknessis of Egipt, whiche thou knewist, but to alle thin enemyes.
Yehova adzakupewetsani ku matenda aliwonse. Sadzakugwetserani matenda owopsa aja munawadziwa ku Igupto, koma adzawagwetsera pa odana nanu.
16 And thou schalt `deuoure, that is, distrie, alle puplis, whiche thi Lord God schal yyue to thee; thin iye schal not spare hem, nethir thou schalt serue the goddis `of hem, lest thei ben in to the fallyng of thee.
Muwononge anthu onse amene Yehova Mulungu wanu awapereka kwa inu. Musawamvere chisoni ndipo musatumikire milungu yawo pakuti umenewo udzakhala msampha kwa inu.
17 If thou seist in thin herte, These folkis ben mo than Y, hou may Y do awei hem?
Mukhoza kunena kuti, “Anthu awa ndi amphamvu kuposa ifeyo. Nanga tingawapirikitse bwanji?”
18 `nyle thou drede, but haue thou mynde, what thingis thi Lord God dide to Farao, and alle Egipcians;
Koma musachite nawo mantha, kumbukirani bwino zimene Yehova Mulungu wanu anachita ndi Farao pamodzi ndi Igupto yense.
19 `he dide the gretteste veniaunces, whiche thin iyen sien, and miraclis and grete wondris, and the strong hond, and arm `holdun forth, that thi Lord God schulde lede thee out; so he schal do to alle puplis whiche thou dredist.
Munadzionera nokha ndi maso anu mayesero aakulu, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, mphamvu yake yopanda malire imene Yehova Mulungu wanu anakutulutsirani. Yehova Mulungu adzachita zimenezo ndi anthu onse amene muwaopa tsopano.
20 Ferthermore and thi Lord God schal sende venemouse flies in to hem, til he do awei, and destrye alle men, that fledden thee, and thei schulen not mowe be hid.
Kuwonjezera apo, Yehova Mulungu wanu adzatumiza mavu pakati pawo mpaka atamaliza onse amene adzakubisalirani.
21 Thou schalt not drede hem, for thi Lord is in the myddis of thee, grete God, and ferdful.
Musaopsedwe nawo pakuti Yehova Mulungu wanu, amene ali pakati panu, ndi Mulungu wamkulu ndi woopsa.
22 He hym silf schal waste these naciouns in thi siyt, litil and litil, and bi partis; thou schalt not mow do awey `tho naciouns togidere, lest peraventure beestis of erthe be multiplied ayens thee;
Yehova Mulungu wanu adzapirikitsa anthu a mitundu yonse pamaso panu, pangʼonopangʼono. Sadzakulolani kuti muwathe nthawi imodzi, kuti nyama zakuthengo zingadzaswane mokuzungulirani.
23 and thi Lord God schal yyue hem in thi siyt, and he schal sle hem, til thei be doon awey outerly.
Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka kwa inu, adzawasokoneza kufikira atawonongedwa.
24 And he schal bitake the kyngis `of hem in to thin hondis, and thou schalt destrie the names `of hem vndur heuene; noon schal mow ayenstonde thee, til thou al to-breke hem.
Iye adzapereka mafumu awo mʼdzanja lanu, ndipo adzafafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Palibe amene adzalimbana nanu, inu mudzawawononga.
25 Thou schalt brenne in fier the grauun ymagis `of hem; thou schalt not coueite the siluer and gold, of whiche tho ymagis ben maad, nether thou schalt take of tho ony thing to thee, lest thou offende therfor, for it is abhominacioun of thi Lord God.
Muwawotche pa moto mafano a milungu yawo. Musasirire siliva ndi golide amene ali pa mafanoyo. Musamutenge kuti akhale wanu chifukwa mukatero mudzakodwa naye ngati msampha, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa nazo.
26 Nether thou schalt brynge ony thing of the idol in to thin hous, lest thou be maad cursid, as also that idol is; thou schalt wlate it as filthe, and thou schalt haue it as defoulyng, and filthis of abhomynacioun, for it is cursid.
Musabweretse chinthu chonyansa mʼnyumba mwanu kuopa kuwonongedwa ngati chonyasacho. Muziyipidwa ndi kunyansidwa nacho kwambiri pakuti chidzawonongedwanso.