< Deuteronomy 5 >

1 And Moises clepide al Israel, and seide to hym, Here, thou Israel, the cerymonyes and domes, whiche Y speke to dai in youre eeris; lerne ye tho, and `fille ye in werk.
Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati: Tamverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuwuzeni lero. Muwaphunzire ndi kuonetsetsa kuti mukuwatsata.
2 Oure Lord God made a boond of pees with vs in Oreb;
Yehova Mulungu wathu anachita pangano ndi ife ku Horebu.
3 he made not couenaunt, `that is, of lawe writun, with oure fadris, but with vs that ben present, and lyuen.
Yehova sanachite pangano ndi makolo athu koma ndi ife, tonse amene tili moyo lero.
4 Face to face he spak to vs in the hil, fro the myddis of the fier.
Yehova anayankhula nanu maso ndi maso kuchokera mʼmoto pa phiri paja.
5 Y was recouncelere and mediatour bitwixe God and you in that tyme, that Y schulde telle to you the wordis `of hym, for ye dredden the fier, and `stieden not in to the hil. And `the Lord seide,
(Pa nthawi imeneyo ine ndinayimirira pakati pa Yehova ndi inu kuti ndikuwuzeni mawu a Yehova, chifukwa inu munkachita mantha ndi moto ndipo simunakwere ku phiri). Ndipo Iye anati:
6 Y am thi Lord God, that ladde thee out of the lond of Egipt, fro the hows of seruage.
“Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo.
7 Thou schalt not haue alien Goddis in my siyt.
“Usakhale ndi milungu ina koma Ine ndekha.
8 Thou schalt not make to thee a grauun ymage, nether a licnesse of alle thingis that ben in heuene aboue, and that ben in erthe bynethe, and that lyuen in watris vndur erthe;
“Usadzipangire chofanizira chinthu chilichonse chakumwamba kapena cha pa dziko lapansi kapena cha mʼmadzi a pansi pa dziko.
9 thou schalt not herie tho, `and thou schalt not worschipe tho; for Y am thi Lord God, `God a feruent louyer; and Y yelde the wickidnesse of fadris, in to sones in to the thridde and the fourthe generacioun to hem that haten me,
Usazigwadire kapena kuzipembedza, pakuti Ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wansanje, wolanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi wa iwo amene amadana nane,
10 and Y do mersy in to many thousyndis to hem that louen me, and kepen myn heestis.
koma ndimaonetsa chikondi chosasinthika ku mibado miyandamiyanda ya anthu amene amandikonda ndi kusunga malamulo anga.
11 Thou schalt not mystake the name of thi Lord God in veyn, for he schal not be vnpunyschid, that takith the name of God on a veyn thing.
“Usagwiritse ntchito molakwika dzina la Yehova Mulungu wako, pakuti Yehova adzamutenga kukhala wochimwa aliyense amene akugwiritsa ntchito dzina lakelo molakwika.
12 Kepe thou the `day of sabat that thou halewe it, as thi Lord God comaundide to thee.
“Uzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika monga momwe Yehova Mulungu wako anakulamulira.
13 In sixe daies thou schalt worche, and thou schalt do alle thi werkis;
Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi,
14 the seventhe day is `of sabat, that is the reste of thi Lord God. Thou schalt not do therynne ony thing of werk; thou, and thi sone, and douyter, seruaunt, and handmaide, and oxe, and asse, and `al thi werk beeste, and the pilgrym which is with ynne thi yatis; that thi seruaunt reste and thin handmaide, as also thou.
koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, tsiku loperekedwa kwa Yehova Mulungu wako. Tsiku limeneli musagwire ntchito iliyonse, inuyo kapena mwana wanu wamwamuna kapena mwana wanu wamkazi kapena wantchito wanu wamwamuna kapena mdzakazi wanu kapena ngʼombe yanu kapena bulu wanu kapena ziweto zanu kapena mlendo amene akukhala mʼmudzi mwanu, motero ndiye kuti wantchito wanu wamwamuna ndi wantchito wanu wamkazi adzapumula monga inuyo.
15 Bithenke thou, that also thou seruedist in Egipt, and thi Lord God ledde thee out fro thennus, in a strong hond, and arm holdun forth; therfor he comaundide to thee, that thou schuldist kepe the `dai of sabat.
Kumbukira kuti unali kapolo ku Igupto ndipo Yehova Mulungu wako anakutulutsa kumeneko ndi dzanja lamphamvu ndi lotambasuka. Choncho Yehova Mulungu wako akukulamula kuti uzisunga tsiku la Sabata.
16 Onoure thi fadir and thi modir, as thi Lord God comaundide to thee, that thou lyue in long tyme, and that it be wel to thee, in the lond which thi Lord God schal yyue to thee.
“Lemekeza abambo ako ndi amayi ako monga Yehova Mulungu wako wakulamulira iwe kuti ukhale ndi moyo wautali ndi kuti zikuyendere bwino mʼdziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.
17 Thou schalt not sle.
“Usaphe.
18 Thou schalt not do letcherie.
“Usachite chigololo.
19 And thou schalt not do thefte.
“Usabe.
20 Thou schalt not speke fals witnessyng ayens thi neiybore.
“Usapereke umboni womunamizira mnzako.
21 Thou schalt not coueite `the wijf of thi neiybore, not hows, not feeld, not seruaunt, not handmayde, not oxe, not asse, and alle thingis that ben hise.
“Usasirire mkazi wa mnzako. Usasirire nyumba ya mnzako kapena munda wake, wantchito wake wamwamuna kapena mdzakazi wake, ngʼombe yake kapena bulu wake, kapena chilichonse cha mnzako.”
22 The Lord spak these wordis to al youre multitude, in the hil, fro the myddis of fier and of cloude and of myist, with greet vois, and addide no thing more; and he wroot tho wordis in two tablis of stoon, whiche he yaf to me.
Awa ndi malamulo amene Yehova anayankhula ndi mawu okweza kwa gulu lanu lonse pa phiri paja mʼmoto, mtambo ndi mdima woopsa, sanawonjezerepo kanthu. Ndipo anawalemba pa mapale awiri amiyala ndi kundipatsa.
23 Forsothe after that ye herden the vois fro the myddis of the derknessis, and sien the hil brenne, alle ye princis of lynagis, and the grettere men in birthe, neiyiden to me, and seiden, Lo!
Mutamva mawu kuchokera mu mdimawo, phiri lili moto lawilawi, atsogoleri onse a mafuko anu ndi akuluakulu anu anabwera kwa ine.
24 oure Lord God schewide to vs his maieste and greetnesse; we herden his vois fro the myddis of fier, and we preueden to day that a man lyuede, `while God spak with man.
Ndipo munati, “Yehova Mulungu wathu wationetsa ulemerero ndi ukulu wake, ndipo tamva mawu ake kuchokera mʼmoto. Lero taona kuti munthu akhoza kukhala ndi moyo ngakhale Mulungu atayankhula naye.
25 Whi therfor schulen we die, and schal this gretteste fier deuoure vs? For if we heren more the vois of oure Lord God, we schulen die.
Koma tsopano tife chifukwa chiyani? Moto waukuluwu utinyeketsa, ndipo tifa tikapitirirabe kumva mawu a Yehova Mulungu wathu.
26 What is ech man, that he here the vois of God lyuynge, that spekith fro the myddis of fier, as we herden, and that he may lyue?
Pakuti ndi munthu uti wolengedwa amene anamvapo mawu a Mulungu wamoyo akuyankhula kuchokera mʼmoto, monga tachitiramu, nakhala ndi moyo?
27 Rathere neiye thou, and here thou alle thingis whiche oure Lord God schal seie to thee; and thou schalt speke to vs, and we schulen here, and schulen do tho wordis.
Pita pafupi kuti ukamvetsere zonse zimene Yehova Mulungu wathu akunena. Kenaka udzatiwuze chilichonse chimene Yehova Mulungu wathu akunena ndipo tidzamvera ndi kuchita.”
28 And whanne the Lord hadde herd this, he seide to me, Y herde the vois of the wordis of this puple, whiche thei spaken to thee; thei spaken wel alle thingis.
Yehova anakumvani pamene munkayankhula kwa ine ndipo Yehova anati kwa ine, “Ndamva zimene anthuwa anena kwa iwe. Chilichonse chimene anena ndi chabwino.
29 Who schal yyue `that thei haue siche soule, that thei drede me, and kepe alle my comaundementis in al tyme, that it be wel to hem and to the sones `of hem, with outen ende?
Zikanakhala bwino akanakhala ndi mtima wondiopa ndi kusunga malamulo anga nthawi zonse kuti zinthu ziziwayendera bwino, iwowo pamodzi ndi ana awo kwamuyaya.
30 Go thou, and seye to hem, Turne ye ayen in to youre tentis.
“Pita uwawuze kuti abwerere ku matenti awo.
31 Sotheli stonde thou here with me, and Y schal speke to thee alle comaundementis, and cerymonyes, and domes, whiche thou schalt teche hem, that thei do tho in the lond which Y schal yyue to hem in to possessioun.
Koma iwe ukhale kuno ndi ine kuti ndikupatse malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene azitsatira mʼdziko limene ndiwapatse kuti alitenge.”
32 Therfor kepe ye, and `do ye tho thingis, whiche the Lord God comaundide to you; ye schulen not bowe awey, nether to the riyt side nether to the left side,
Choncho samalirani kuchita zimene Yehova Mulungu wanu akukulamulirani inu, musapatukire kudzanja lamanja kapena lamanzere.
33 but ye schulen go bi the weie whiche youre Lord God comaundide, that ye lyue, and that it be wel to you, and that youre daies be lengthid in the lond of youre possessioun.
Muyende mʼnjira yonse imene Yehova Mulungu wanu wakulamulirani kuti mukhale ndi moyo ndi kupambana, ndi kuti masiku anu achuluke mʼdziko limene mudzatengelo.

< Deuteronomy 5 >