< Deuteronomy 29 >

1 These ben the wordis of boond of pees, which the Lord comaundide to Moyses, that he schulde smyte with the sones of Israel in the lond of Moab, outakun that bond of pees, which he couenauntide with hem in Oreb.
Awa ndiwo mawu a mʼpangano limene Yehova analamula Mose kuti achite ndi Aisraeli ku Mowabu, powonjezera pa pangano limene anapangana nawo ku Horebu.
2 And Moises clepid al Israel, and seide to hem, Ye sien alle thingis whiche the Lord dide bifor you in the lond of Egipt, to Farao and alle hise seruauntis, and to al his lond;
Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati kwa iwo: Inu munaona zonse zimene Yehova anachita kwa Farao, nduna zake ndi dziko lake lonse ku Igupto.
3 the greet temptaciouns whiche thin iyen sien, `tho signes, and grete wondris.
Ndi maso anu munaona mayesero onse aja, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zazikulu zija.
4 And the Lord yaf not to you an herte vndurstondynge, and iyen seynge, and eeris that moun here, til in to present dai.
Koma mpaka lero Yehova sanakupatseni mtima wozindikira kapena maso openya kapena makutu akumva.
5 He ledde you bi fourti yeer thoruy deseert; youre clothis weren not brokun, nether the schoon of youre feet weren waastid bi eldnesse;
Mʼzaka makumi anayi zimene ndinakutsogolerani mʼchipululu, zovala zanu ndiponso nsapato za ku mapazi anu sizinangʼambike.
6 ye eetun not breed, ye drunken not wyn and sidur, that ye schulden wite that he is youre Lord God.
Inu simunadye buledi ndi kumwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa. Ndinachita izi kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
7 And ye camen to this place; and Seon, the kyng of Esebon yede out, and Og, the kyng of Basan, and camen to us to batel. And we han smyte hem,
Pamene munafika malo ano, Sihoni mfumu ya ku Hesiboni ndi Ogi mfumu ya ku Basani anabwera kudzamenyana nafe koma tinawagonjetsa iwo.
8 and we token awey the lond `of hem, and we yauen `the lond to possessioun, to Ruben, and to Gad, and to the half lynage of Manasses.
Tinatenga dziko lawo ndi kulipereka ngati cholowa cha fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase.
9 Therfor kepe ye the wordis of this couenaunt, and fille ye tho, that ye vndirstonde all thingis whiche ye schulen do.
Tsatirani mosamalitsa mawu a mʼpangano ili kuti zinthu zizikuyenderani bwino pa zochitika zanu zonse.
10 Alle ye stonden to day bifor youre Lord God, youre princes, and lynagis, and the grettere men in birthe, and techeris, al the puple of Israel,
Lero lino nonse mukuyima pamaso pa Yehova Mulungu wanu, atsogoleri a mafuko anu, akuluakulu ndi nduna zanu, ndi amuna ena onse a mu Israeli,
11 fre children, and youre wyues, and comelyngis that dwellen with thee in castels, outakun the heweris of stonus, and outakun hem that beren watris;
pamodzi ndi ana ndi akazi anu, kudzanso alendo amene akukhala pakati panu omwe amakuwazirani nkhuni ndi kukutungirani madzi.
12 that thou go in the boond of pees of thi Lord God, and in the ooth which thi Lord God smytith with thee,
Mukuyimirira pano kuti mulowe mʼpangano ndi Yehova Mulungu wanu, pangano limene Yehova akuchita ndi inu lero ndi kulisindikiza ndi malumbiro,
13 that he reise thee in to a puple to hym silf, and that he be thi Lord God, as he spak to thee, and as he swoor to thi fadris, to Abraham, Ysaac, and Jacob.
kukukhazikitsani lero lino ngati anthu ake, ndi kuti Iye akhale Mulungu wanu monga anakulonjezani inu ndiponso monga analumbira kwa makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
14 And not to you aloone Y smyte this loond of pees, and conferme these othis,
Ndikupanga pangano ili ndi malumbiro ake osati kwa inu nokha,
15 but to alle men, present and absent.
amene muli pano pamaso pa Yehova Mulungu wathu, koma ndi iwonso amene sali pano lero.
16 For ye witen hou we dwelliden in the lond of Egipt, and how we passiden bi the myddis of naciouns; whiche ye passiden,
Inu nomwe mukudziwa mmene tinkakhalira ku Igupto ndi mmene tinadutsira mayiko pa ulendo wobwera kuno.
17 and siyen abhomynaciouns and filthis, that is, idols `of hem, tre and stoon, siluer and gold, whiche thei worschipiden.
Ife tinaona pakati pawo mafanizo ndi mafano awo onyansa, amtengo ndi amiyala, asiliva ndi agolide.
18 Lest perauenture among you be man ether womman, meyne ether lynage, whos herte is turned away to dai fro youre Lord God, that he go, and serue the goddis of tho folkis; and a roote buriounnynge galle and bitternesse be among you;
Onetsetsani kuti pasapezeke mwamuna kapena mkazi, banja kapena fuko pakati panu lero amene mtima wawo udzapandukira Yehova Mulungu wanu ndi kupita kukapembedza milungu ya mitundu iyo. Onetsetsani kuti pasapezeke muzu pakati panu wotulutsa mankhwala akupha otere.
19 and whanne he hath herd the wordis of this ooth, he blesse hym silf in his herte, and seie, Pees schal be to me, and Y schal go in the schrewidnesse of myn herte; and lest the drunkun take the thirsti,
Munthu wotere akamva mawu a lumbiro ili, asadzidalitse yekha mʼmaganizo mwake namati, “Ine ndidzapulumuka ngakhale nditapitiriza kuyenda njira yanga.” Zoterezi zidzadzetsa masautso pa nthaka ya chinyontho ndi yowuma yomwe.
20 and the Lord forgyue not to hym, but thanne ful greetli his strong veniaunce be feers, and the feruour ayens that man, and alle the cursis that ben writun in this book `sitte on hym; and `the Lord do away his name vndur heuene,
Yehova sadzamukhululukira. Mkwiyo ndi nsanje ya Yehova zidzamuyakira munthuyo. Matemberero onse wolembedwa mʼbukuli adzamugwera iye ndipo Yehova adzafafaniza dzina lake pa dziko lapansi.
21 and waaste hym in to perdicioun fro alle the lynagis of Israel, bi the cursis that ben conteyned in the book of this lawe and of boond of pees.
Yehova adzasankha pakati pa Aisraeli anthu oyenera masautso monga mwa matemberero onse a mʼpangano olembedwa Mʼbuku la Malamulo.
22 And the generacioun suynge schal seie, and the sones that schulen be borun aftirward, and pilgrimys that schulen come fro fer, seynge the veniauncis of that lond, and the sikenessis bi whiche the Lord turmentide that lond,
Ana anu a mibado yakutsogolo ndi alendo amene adzachokera kutali adzaona matsoka amene adzakugwerani mʼdziko muno ndiponso matenda amene Yehova adzabweretsa pa dzikoli.
23 brennynge `that lond with brymston and heete of the sunne, so that it be no more sowun, nether bringe forth ony grene thing, in to ensaumple of destriyng of Sodom and of Gommorre, of Adama and of Seboym, whiche the Lord destriede in his ire and stronge veniaunce.
Dziko lonse lidzasanduka nthaka ya mchere ndi ya sulufule. Simudzadzalamo kanthu, simudzakhala chomera chilichonse, ndi mbewu yomera mʼmenemo. Dziko lanu lidzakhala lowonongeka ngati Sodomu ndi Gomora, Adima ndi Zeboimu, mizinda imene Yehova anayiwononga ndi mkwiyo wake waukulu.
24 And alle folkis schulen seie, Whi dide the Lord so to this lond? What is the greet ire of his stronge veniaunce?
Mitundu yonse ya anthu idzafunsa kuti, “Kodi chifukwa chiyani Yehova anachita zotere mʼdziko lake? Kodi chifukwa chiyani anaonetsa mkwiyo woopsa wotere?”
25 and thei schulen answere, For thei forsoken the couenaunt of the Lord, whiche he couenauntide with her fadris, whanne he ledde hem out of the lond of Egipt,
Ndipo yankho la mafunso amenewa lidzakhala lakuti, “Chifukwa chakuti anthu awa aphwanya pangano la Yehova Mulungu wa makolo awo, pangano limene Iye anapangana nawo pamene anawatulutsa ku Igupto.
26 and thei serueden alien goddis, and worschipiden hem, whiche thei knewen not, and to whiche thei weren not youun;
Iwo anachoka ndi kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza, milungu imene sanayidziwe, milungu imene sanawapatse.
27 therfor the strong veniaunce of the Lord was wrooth ayens this lond, that he brouyte yn on it alle the cursis that ben writun in this book;
Choncho Yehova anakwiyira dziko lino, kotero anabweretsa matemberero onse amene analembedwa mʼbuku lino.
28 and he castide hem out of her lond, in ire and strong veniaunce, and in gretteste indignacioun; and he castide forth in to an alien lond, as it is preued to dai.
Ndi mkwiyo komanso ukali wake woopsa Yehova anawazula mʼdziko lawo ndi kuwaponyera mʼdziko lina, monga mmene zilili lero lino.”
29 Thingis ben hid of oure Lord God, `that is, in his biforknowing, whiche thingis ben schewid to us, and to oure sones with outen ende, that we do alle the wordis of this lawe.
Zinsinsi ndi za Yehova Mulungu wathu koma zinthu zimene zaululidwa ndi zathu ndi ana athu kwamuyaya, kuti titsatire mawu onse a mʼmalamulowa.

< Deuteronomy 29 >