< Deuteronomy 22 >

1 Thou schalt not se `thi brotheris oxe, ethir scheep, errynge, and schalt passe, but thou schalt brynge ayen to thi brother.
Ngati uwona ngʼombe kapena nkhosa ya mʼbale wako ikusochera, usayilekerere koma uyesetse kuyibwezera kwa iye.
2 And if thi brother is not nyy, nether thou knowist hym, thou schalt lede tho beestis in to thin hows, and tho schulen be at thee, as long as thi brother sekith tho, and til he resseyue hem.
Ngati mʼbale wakoyo sakhala pafupi kapena sukudziwa kuti ndi yandani, uyitengere ku nyumba kwako ndi kuyisamala mpaka mwini wake atayilondola ndipo umubwezere.
3 In lijk maner thou schalt do of `the asse, and clooth, and of ech thing of thi brother, that was lost; if thou fyndist it, be thou not necgligent as of an alien thing.
Uzitero ndithu ngati upeza bulu kapena mkanjo kapena chilichonse chimene chatayika. Osachilekerera.
4 If thou seest that the asse, ethir oxe of thi brothir felde in the weye, thou schalt not dispise, but thou schalt `reise with hym.
Ngati wapeza bulu kapena ngʼombe ya mʼbale wako itagwa panjira, usayilekerere. Ithandize kuti idzuke.
5 A womman schal not be clothid in a mannys clooth, nether a man schal vse a wommannys cloth; for he that doith thes thingis is abhomynable bifor God. If thou goist in the weie,
Akazi asavale zovala za amuna, kapena mwamuna kuvala zovala za akazi, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita izi.
6 and fyndist a `nest of a brid in a tree, ethir in the erthe, and fyndist the modir sittynge on the briddis ethir eyrun, thou schalt not holde the modir with `the children, but thou schalt suffre `the modir go,
Ukapeza chisa cha mbalame mʼmphepete mwa msewu, kaya ndi mu mtengo kapena pansi, mbalame yayikazi itafungatira ana kapena mazira, usatenge mbalameyo pamodzi ndi ana ake omwe.
7 and schalt holde the sones takun, that it be wel to thee, and thou lyue in long tyme. Whanne thou bildist a newe hows,
Anawo mukhoza kutenga koma onetsetsani kuti mayi wawo mwamutaya kuti apite, kuti zinthu zizikuyenderani bwino ndiponso kuti mukhale ndi moyo wautali.
8 thou schalt make a wal of the roof bi cumpas, lest blood be sched out in thin hows, and thou be gilti, if another man slidith, and falle in to a dich.
Mukamanga nyumba yatsopano, mutchingire khonde lake la pa denga kuti inu musapezeke ndi mlandu wopha munthu ngati wina agwa kuchokera pa khonde la pa dengalo.
9 Thou schalt not sowe thi vyner `of another seed, lest bothe the seed which thou hast sowe, and tho thingis that `comen forth of the vyner, ben halewid togidere.
Musadzale mbewu zamitundu iwiri mʼmunda wanu wa mpesa, ngati mutero, si mbewu zanu zokha zimene zidzakhale zodetsedwa, komanso zipatso za mʼmunda wamphesawo.
10 Thou schalt not ere with an oxe and asse togidere.
Musatipule pogwiritsa ntchito ngʼombe ndi bulu pa goli limodzi.
11 Thou schalt not be clothid in a cloth, which is wouun togidir of wolle and `of flex.
Musamavale chovala chopangidwa mophatikiza ubweya ndi thonje.
12 Thou schalt make litle cordis bi foure corneris in the hemmys of thi mentil, `with which thou art hilid.
Muzipanga mphonje mʼngodya za mkanjo umene mumavala.
13 If a man weddith a wijf, and aftirward hatith hir,
Ngati munthu akwatira mkazi, ndipo atagona naye nʼkusamufunanso
14 and sekith occasiouns bi which he `schal forsake hir, and puttith ayens hir `the werste name, and seith, Y haue take this wijf, and Y entride to hir, and Y foond not hir virgyn; the fadir and modir of hir schulen take
namunyoza ndi kumuyipitsira dzina nʼkumati, “Ine ndinakwatira mkazi uyu, koma pamene ndinakhala naye, sindinachione chizindikiro cha unamwali wake,”
15 hir, and thei schulen bere with hem the signes of her virgynyte to the eldre men of the citee, that ben in the yate;
zikatero abambo ndi amayi ake ayenera kubweretsa chitsimikizo chakuti anali namwali kwa akuluakulu a mzinda ku chipata.
16 and the fadir schal seie, Y yaf my douytir wijf to this man, and for he hatith hir, he puttith to hir `the werste name,
Abambo ake a mtsikanayo adzanene kwa akuluakuluwo kuti, “Ine ndinamupatsa munthu uyu mwana wanga wamkazi kuti amukwatire, koma sakumufunanso.
17 that he seye, Y foond not thi douytir virgyn; and lo! these ben the signes of virgynyte of my douytir; thei schulen sprede forth a cloth bifor the eldre men of the citee. And the eldere men of that citee schulen
Tsopano wamunyoza ndipo wanena kuti, ‘Ine sindinapeze kuti mwana wanu wamkaziyu ndi namwali.’ Koma tsopano onani chitsimikizo ichi cha unamwali wa mwana wanga wamkazi.” Kenaka makolo a mtsikanayo adzaonetse kansalu kwa akuluakulu aja,
18 take the man, and schulen bete hym,
ndipo akuluakuluwo adzamugwire munthuyo namupatsa chilango.
19 and ferthermore thei schulen condempne hym in an hundrid siclis of siluer, whiche he schal yyue to the `fadir of the damysel, for he diffamide the werste name on a virgyn of Israel; and he schal haue hir wijf, and he schal not mowe forsake hir, in al `the tyme of his lijf.
Iwo adzamulipitse ndalama zasiliva zokwana 100 nazipereka kwa abambo a mtsikana, chifukwa munthu uyu wayipitsa dzina la mtsikana wa Chiisraeli. Ayenera kukhalabe mkazi wake ndipo asadzamuleke moyo wake wonse.
20 That if it is soth, that he puttith ayens hir, and virgynyte is not foundun in the damysel, thei schulen caste hir `out of `the yatis of
Koma ngati zomunenerazo ndi zoona, ndipo kuti chitsimikizo cha unamwali wa mtsikanayo sichinapezeke,
21 the hous of hir fadir; and men of that citee schulen oppresse hir with stoonys, and sche schal die, for sche dide vnleueful thing in Israel, that sche dide fornycacioun in `the hows of hir fadir; and thou schalt do awey yuel fro the myddis of thee.
iyeyu ayenera kumutengera pa khomo pa abambo ake pamene anthu a mu mzinda wake akamuphere ndi miyala. Iyeyo wachita chinthu chochititsa manyazi mu Israeli pochita chiwerewere akanali pa khomo pa abambo ake. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu.
22 If a man slepith with `the wijf of another man, euer eithir schal die, that is, auowter and auowtresse; and thou schalt do awey yuel fro Israel.
Ngati munthu apezeka akugona ndi mkazi wa mwini wake, ayenera kuphedwa munthuyo pamodzi ndi mkazi yemwe wagona nayeyo. Muyenera kuchotsa zoyipa mu Israeli.
23 If a man spousith a damysel virgyn, and a man fyndith hir in the citee, and doith letcherie with hir,
Ngati munthu mu mzinda akumana ndi mkazi yemwe anachita kale chinkhoswe nagona naye,
24 thou schalt lede euer eithir to the yate of that citee, and thei schulen be oppressid with stoonus; the damysel schal be stonyd, for sche criede not, whanne sche was in the citee; the man schal `be stonyd, for he `made low the wijf of his neiybore; and thou schalt do awei yuel fro the myddis of thee.
muwatengere awiriwo ku chipata cha mzinda ndi kuwapha ndi miyala. Aphedwe chifukwa mtsikanayo anali pafupi ndi anthu ndipo sanakuwe kuti ena amuthandize ndipo mwamunayo chifukwa anayipitsa mkazi wa mwini. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
25 Forsothe if a man fyndith in the feeld a `damysel, which is spousid, and he takith, and doith letcherie with hir, he aloone schal die;
Koma ngati munthu akumana ndi mkazi kutchire yemwe anachita kale chinkhoswe namugwiririra, mwamuna yekhayo ndiye woyenera kuphedwa.
26 the damysel schal suffre no thing of yuel, nethir is gilti of deeth; for as a theef risith ayens his brothir, and sleeth `his lijf, so and the damysel suffride; sche was aloone in the feeld,
Mtsikanayo musamuchite chilichonse, palibe tchimo limene wachita loti ayenera kuphedwa. Mlandu uwu ufanana ndi wa munthu amene alimbana ndi kupha mnzake woyandikana naye,
27 sche criede, and noon was present, that schulde delyuer hir.
pakuti mwamunayo anamupeza mtsikanayo kutchire, ndipo ngakhale mtsikana wachinkhosweyo anakuwa, panalibe anamulanditsa.
28 If a man fyndith a damysel virgyn that hath no spowse, and takith, and doith letcherie with hir, and the thing cometh to the doom,
Ngati munthu apezana ndi namwali woti sanachite chinkhoswe, namugwiririra, munthuyo nʼkupezeka,
29 he that slepte with hir schal yyue to `the fadir of the damysel fifti siclis of siluer, and he schal haue hir wijf, for he `made hir low; he schal not mow forsake hir, in alle the daies of his lijf.
ayenera kuwalipira abambo ake a namwaliyo ndalama za siliva makumi asanu. Iye ayenera kumukwatira mkaziyo chifukwa wamuyipitsa, ndipo sadzamulekanso moyo wake wonse.
30 A man schal not take `the wijf of his fadir, nethir he schal schewe `the hilyng of hir.
Munthu asakwatire mkazi wa abambo ake pakuti ayenera kuchitira ulemu pogona pa abambo ake.

< Deuteronomy 22 >