< Deuteronomy 18 >

1 Preestis and dekenes, and alle men that ben of the same lynage, schulen `not haue part and eritage with the tother puple of Israel, for thei schulen ete the sacrifices of the Lord, and the offryngis of hym;
Ansembe Achilevi amene ndi fuko lonse la Alevi, asapatsidwe malo kapena cholowa pakati pa Aisraeli. Iwowa azidzadya zoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe, popeza zimenezo ndiye cholowa chawo.
2 and thei schulen not take ony othir thing of the possessioun of her britheren; for the Lord hym silf is the `eritage of hem, as he spak to hem.
Iwowa sadzakhala ndi cholowa pakati pa abale awo pakuti Yehova ndiye cholowa chawo monga anawalonjezera.
3 This schal be the doom of preestis of the puple, and of hem that offren sacrifices; whether `thei offren an oxe, ether a scheep, thei schulen yyue to the preest the schuldre, and the paunche, the firste fruytis of wheete,
Anthu amene abwera kudzapereka nsembe ya ngʼombe kapena nkhosa, azipereka kwa wansembe gawo lake motere: mwendo wakutsogolo, nyama yamʼmasaya ndi zamʼkati.
4 and of wyn, and of oile, and a part of wollis of the scheryng of scheep.
Muziwapatsa zamasika zoyamba za tirigu wanu, vinyo watsopano ndi mafuta, ndi ubweya woyamba pometa nkhosa zanu,
5 For thi Lord God chees hym of alle thi lynagis, that he stonde and mynystre to `the name of the Lord, he and hise sones, with outen ende.
pakuti Yehova Mulungu wanu wawasankha iwowa ndi ana awo pakati pa mafuko anu onse kuti aziyimirira ndi kutumikira mʼdzina la Yehova nthawi zonse.
6 If a dekene goith out of oon of thi citees of al Israel, in which he dwellith, `and wole come and desirith the place which the Lord chees,
Ngati Mlevi asuntha achoka ku mzinda wake ndi kupita kumalo kwina kumene Yehova wasankha mu Israeli momwemo ndi mtima wake wonse,
7 he schal mynystre in the name of his Lord God as alle hise britheren dekenes, that schulen stonde in that tyme byfore the Lord.
kumeneko akhoza kukatumikirako mʼdzina la Yehova Mulungu wake monga Alevi anzake onse amene akutumikira pamaso pa Yehova.
8 He schal take the same part of meetis, `which and othere dekenes schulen take; outakun that that is due to hym in his citee, bi `successioun ethir eritage `of fadir.
Iye ayenera kulandira zogawana zawo mofanana ndi anzakewo ngakhale kuti iye anagulitsa kale cholowa cha pa banja pawo.
9 Whanne thou hast entrid in to the lond which thi Lord God schal yyue to thee, be thou war lest thou wole sue abhomynaciouns of tho folkis;
Mukafika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musakaphunzire makhalidwe onyansa a anthu a mʼdzikolo.
10 noon be foundun in thee that clensith his sone, ether his douytir, `and ledith bi the fier, ethir that axith questiouns of dyuynouris `that dyuynen aboute the auteris, and that taketh hede to dremes and chiteryng of bryddis; nethir ony wicche be,
Pasapezeke pakati panu munthu wootcha pa moto mwana wake wamwamuna kapena wamkazi ngati nsembe. Asapezekenso pakati panu munthu wowombeza kapena wochita mawula, wolosera, wochita za ufiti,
11 nethir an enchauntere, `that is, that disseyueth mennus iyen that a thing seme that is not; nether a man take counsel at hem that han a feend spekynge `in the wombe, nether take counsel at false dyuynouris nethir seke of deed men the treuthe.
wolodza, kapena woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndi kumafunsira nzeru kwa anthu akufawo.
12 For the Lord hath abhomynacioun of alle these thingis, and for siche wickidnessis he schal do awei hem in thin entryng.
Aliyense wochita zinthu zotere ndi wonyansa pamaso pa Yehova, ndipo chifukwa cha zonyansa zimenezi Yehova adzakupirikitsirani mitundu ya anthu imeneyi.
13 Thou schalt be perfit and without filthe, with thi Lord God.
Muzikhala angwiro pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
14 These hethen men, `the lond of whiche thou schalt welde, heren hem that worchen bi chiteryng of briddis, and false dyuynouris; forsothe thou art tauyt in other maner of thi Lord God.
Mitundu ya anthu imene mudzayipirikitseyo imamvera anyanga kapena owombeza mawula. Koma inu Yehova Mulungu wanu sanakuvomerezeni kutero.
15 Thi Lord God schal reise a prophete of thi folk and of thi britheren as me, thou schalt here hym;
Yehova Mulungu wanu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine. Muyenera kumumvera ameneyo.
16 as thou axidist of thi Lord God in Oreb, whanne the cumpany was gaderid, and thou seidist, Y schal no more here the vois of my Lord God, and Y schal no more se `this grettiste fier, lest Y die.
Pakuti izi ndi zimene munapempha kwa Yehova Mulungu wanu ku Horebu pa tsiku la msonkhano lija pamene munati, “Ife tisamvenso mawu a Yehova Mulungu wathu kapena kuona moto woopsawu, kuopa kuti tingafe.”
17 And the Lord seide to me, Thei spaken wel alle thingis.
Yehova anati kwa ine, “Zimene akunenazi ndi zabwino.
18 Y schal reise to hem a prophete, lijk thee, of the myddis of her britheren, and Y schal putte my wordis in his mouth, and he schal speke to hem alle thingis, whiche I schal comaunde to him.
Ndidzawawutsira mneneri ngati iwe pakati pa abale awo ndipo ndidzayika mawu anga mʼkamwa mwake ndipo adzawawuza chilichonse chimene ndidzamulamula.
19 Forsothe Y schal be vengere of `that man, that nyle here the wordis `of hym, whiche he schal speke in my name.
Ine mwini ndidzaweruza aliyense amene sadzamvera mawu anga amene mneneriyo adzayankhula mʼdzina langa.
20 `Sotheli a prophete `schal be slayn, which is bischrewid with pride, and wole speke in my name tho thingis, whiche Y comaundide not to hym, that he schulde seie, ethir bi the name of alien goddis.
Koma mneneri wonena zinthu mʼdzina langa ndisanamulamulire kutero, kapena mneneri wonenera mʼdzina la milungu ina, ayenera kuphedwa.”
21 That if thou answerist bi pryuy thouyt, Hou may Y vndirstonde the word, which the Lord spak not? thou schalt haue this signe,
Mwina mukhoza kumadzifunsa kuti, “Kodi tingadziwe bwanji kuti uthengawu sanayankhule ndi Yehova?”
22 `The Lord spak not this thing which thilke prophete biforseid in the name of the Lord, `and it bifallith not, but `the prophete feynede bi the pride of his soule, and therfor thou schalt not drede hym.
Ngati zimene mneneriyo wanenera mʼdzina la Yehova sizinachitike kapena kukwaniritsidwa, ndiye kuti umenewo si uthenga umene Yehova wayankhula. Mneneri ameneyo amangoyankhula za mʼmutu mwake ndiye musadzidzimuke naye.

< Deuteronomy 18 >