< Deuteronomy 17 >

1 Thou schalt not offre to thi Lord God an oxe and a scheep in which is a wem, ether ony thing of vice, for it is abhominacioun to thi Lord God.
Musapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ngʼombe kapena nkhosa imene ili ndi chilema kapena cholakwika chilichonse, pakuti zimenezi zimamunyansa.
2 And whanne a man ether a womman, that doon yuel in the siyte of thi Lord God, ben foundun at thee, with ynne oon of thi yatis whiche thi Lord God schal yyue to thee, and thei breken the couenaunt of God,
Ngati mwamuna kapena mkazi pakati panu, mʼmizinda imene Yehova akukupatsani apezeka akuchita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu pophwanya pangano lake,
3 that thei go and serue alien goddis, and worschipe hem, the sunne, and moone, and al the knyythod of heuene, whiche thingis Y comaundide not;
ndipo ngati motsutsana ndi lamulo langa wapembedza milungu ina, kuyigwadira milunguyo, kaya ndi dzuwa kapena mwezi kapena nyenyezi zakumwamba,
4 and this is teld to thee, and thou herist, and `enquerist diligentli, and fyndist that it is soth, and abhomynacioun is doon in Israel;
ndipo inu nʼkuwuzidwa zimenezi, mufufuze bwinobwino. Ngati ndi zoona, ndipo ngati zatsimikizika kuti chonyansa choterechi chachitikadi mu Israeli,
5 thou schalt lede out the man and the womman, that diden a moost cursid thing, to the yatis of thy citee, and thei schulen be oppressid with stoonus.
mumutengere mwamuna kapena mkazi amene wachita chonyansa choterechi ku chipata cha mzinda wanu ndi kumupha pomugenda miyala.
6 He that schal be slayn, schal perische in the mouth of tweyne, ethir of thre witnessis; no man be slayn, for o man seith witnessyng ayens hym.
Munthu aziphedwa pakakhala mboni ziwiri kapena zitatu koma osati mboni imodzi yokha ayi.
7 The hond of witnessis schal first sle hym, and the last hond of the tothir puple schal be sent, that thou do awei yuel fro the myddis of thee.
Wochitira umboniwo ndiwo aziyamba kumupha munthuyo, ndipo kenaka anthu onse. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
8 If thou perseyuest, that hard and douteful doom is at thee, bitwixe blood and blood, cause and cause, lepre and not lepre, and thou seest that the wordis of iugis with ynne thi yatis ben dyuerse; rise thou, and stie to the place which thi Lord God hath choose;
Ngati akubweretserani milandu mʼmabwalo anu imene ili yovuta kuweruza kaya ndi yokhetsa magazi, kaya ndi yophwanyirana ufulu, kaya ndi yovulazana, muyitengere kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
9 and thou schalt come to the preestis of the kyn of Leuy, and to the iuge which is in that tyme, and thou schalt axe of hem, whiche schulen schewe to thee the treuthe of doom.
Mudzapite kwa ansembe Alevi ndi kwa woweruza wa pa nthawi imeneyo. Kawafunseni ndipo iwowo adzakuwuzani zoyenera kuchita.
10 And thou schalt do, what euer thing thei seien, that ben souereyns in the place which the Lord chees, and techen thee bi the lawe of the Lord;
Kachiteni zimene adzakuwuzenizo kuchokera ku malo amene Yehova adzasankhe. Kaonetsetseni kuti mukutsatira zonse zimene akuwuzanizo.
11 thou schalt sue the sentence of hem; thou schalt not bowe to the riyt side, ether to the lefte.
Kachiteni motsatira malamulo ndi malangizo amene adzakuwuzeni; osawanyoza, potembenukira kumanja kapena kumanzere.
12 Forsothe that man schal die, which is proud, and nyle obeie to the comaundement of the preest, `that mynystrith in that tyme to thi Lord God, and to the sentence of iuge, and thou schalt do awei yuel fro the myddis of Israel;
Munthu aliyense amene adzanyoza woweruza kapena wansembe amene akutumikira kumeneko mʼmalo mwa Yehova Mulungu wanu, aphedwe ndithu. Muzichotsa choyipa pakati pa Israeli.
13 and al the puple schal here, and drede, that no man fro thennus forth bolne with pride.
Anthu onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha, choncho sadzadzikuzanso.
14 Whanne thou hast entrid in to the lond, which thi Lord God schal yyue to thee, and weldist it, and dwellist therynne, and seist, Y schal ordeyne a kyng on me, as alle naciouns `bi cumpas han;
Mukalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mulitenge, ndipo mukakakhazikika mʼmenemo nimunena kuti, “Tiyeni tisankhe mfumu yoti izitilamulira monga imachitira mitundu yonse yotizungulirayi,”
15 thou schalt ordeyne hym, whom thi Lord God chesith of the noumbre of thi brethren. Thou schalt not mow make king a man of anothir folk, which man is not thi brother.
mudzakhazikitse mfumu yoti izikakulamulirani, mfumu imene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati panu. Mudzasankhe mfumuyo kuchokera pakati pa abale anu. Osasankha mlendo, munthu amene sachokera pakati pa abale anu Aisraeli.
16 And whanne the king is ordeyned, he schal not multiplie horsis to hym, nethir he schal lede ayen the puple in to Egipt, nethir he schal be reisid bi the noumbre of knyytis, moost sithen the Lord comaundide to you, that ye turne no more ayen bi the same weie.
Komatu mfumuyo isadzikundikire akavalo, kapena kutuma anthu kupita ku Igupto kukayipezera akavalo ena, pakuti Ambuye akuti, “Simuyenera kubweranso ku Igupto mʼnjira yomweyo.”
17 The kyng schal not haue ful many wyues, that drawen his soule `to ouer myche fleischlynesse, nether `he schal haue grete burthuns of siluer and of gold.
Asadziwunjikire akazi kuopa kuti mtima wake ungamusocheretse. Asadziwunjikirenso golide ndi siliva wambiri.
18 Forsothe after that he hath sete in the trone of his rewme, he schal write to himsilf the deuteronomy of this lawe in a `volym ether book, and he schal take `a saumpler at preestis of `the kyn of Leuy;
Akakhala pa mpando waufumuwo, ayenera kulemba za iye mwini mʼbuku la malamuloli, kuchokera kwa ansembe Alevi.
19 and he schal haue it with hym, and he schal rede it in alle the daies of his lijf, that he lerne to drede his Lord God, and to kepe hise wordis and cerymonyes, that ben comaundid in the lawe;
Asunge zimene walembazo ndipo ayenera kumaziwerenga masiku onse a moyo wake, kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wake posunga mosamalitsa malamulo ndi malangizowa.
20 nether his herte be reisid in to pride on hise brithren, nether bowe he in to the riyt side, ether left side, that he regne long tyme, he and hise sones on Israel.
Asadzione kuti iyeyo ndi wopambana kuposa abale ake, nalekeratu kutsatira malamulo. Akasamala zimenezi iye ndi ana ake adzalamulira ufumu wa Israeli kwa nthawi yayitali.

< Deuteronomy 17 >