< Deuteronomy 13 >

1 If a prophete risith in the myddis of thee, ethir he that seith hym silf to haue seyn a dreem, and he biforseith a signe and a wondur to comynge aftir,
Ngati mneneri kapena wina aliyense amene amanena zamʼtsogolo mwa maloto atuluka pakati panu, nalengeza za chizindikiro chozizwitsa kapena chodabwitsa,
2 and this that he spak bifallith, and he seith to thee, Go we, and sue alien goddis, whiche thou knowist not, and serue we hem,
chinthu nʼkuchitikadi, tsono iyeyo nʼkunena kuti, “Tiyeni titsatire milungu ina, tiyeni tiyipembedze,” (kunena milungu imene simunayidziwe),
3 thou schalt not here the wordis of that prophete, ether of dremere; for youre Lord God assaieth you, that he wite opynli whether ye louen hym ether nay, in al youre herte, and in al youre soule.
musamumvere mneneriyo kapena wolotayo. Yehova Mulungu wanu afuna akuyeseni kuti aone ngati mumamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
4 Sue ye youre Lord, and `drede ye hym; kepe ye his comaundementis, and here ye `the vois of hym; ye schulen serue hym, and ye schulen cleue to hym.
Muyenera kutsatira Yehova Mulungu wanu, ndipo ndi Iyeyo amene muyenera kumuopa. Muzisunga malamulo ake ndi kumamumvera, muzimutumikira ndipo kumukangamira Iyeyo.
5 Forsothe thilke prophete, ether the feynere of dremes, schal be slayn; for he spak that he schulde turne you awei fro youre Lord God, that ladde you out of the lond of Egipt, and ayenbouyte you fro the hous of seruage, that `thilke prophete schulde make thee to erre fro the weie which thi Lord God comaundide to thee; and thou schalt do awey yuel fro the myddis of thee.
Mneneri kapena wolotayo ayenera kuphedwa, popeza analalikira zopandukira Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo. Wolalikirayo anafuna kukupatutsani pa njira imene Yehova Mulungu wanu anakulamulirani kuti muyitsatire. Muzichotsa choyipa pakati panu.
6 If thi brothir, the sone of thi modir, ether thi sone, ethir thi douyter, ether the wijf which is in thi bosum, ethir thi freend whom thou louest as thi soule, wole counsele thee, and seith priueli, Go we and serue alien goddis, whiche thou knowist not,
Ngati mʼbale wanu weniweni kapena mwana wanu wamwamuna kapena wamkazi, kapena mkazi wanu wokondedwa, kapena mnzanu wapamtima akukakamizani mwachinsinsi, nʼkumati, “Tiyeni tipite tikapembedze milungu ina” (milungu imene inuyo kapena makolo anu sanayidziwe,
7 and thi fadris, of alle the folkis `in cumpas, that ben niy ether fer, fro the bigynnyng `til to the ende of the lond,
milungu ya anthu okuzungulirani, kaya ndi apafupi kapena akutali, kuchokera kumapeto mpaka kumapeto kwina kwa dziko lapansi),
8 assente thou not to hym, nether here thou, nether thin iyen spare hym, that thou haue mercy,
musamugonjere kapena kumumvera. Musamumvere chisoni. Musamuleke kapena kumutchinjiriza.
9 and hide hym, but anoon thou schalt sle hym. Thin hond be fyrst on him and aftir thee al the puple putte to hond.
Mumuphe ndithu. Dzanja lanu likhale loyambirira kumupha, kenaka manja a anthu ena onse.
10 He schal be oppressid with stoonus, and `schal be slayn; for he wolde drawe thee awei fro thi Lord God, that ledde thee out of the lond of Egipt, fro the hous of seruage,
Mumuponye miyala mpaka kumupha, chifukwa anafuna kukupatutsani pa njira ya Yehova Mulungu amene anakutulutsani ku Igupto, dziko la ukapolo.
11 that al Israel here and drede, and do no more ony thing lijk this thing.
Tsono Aisraeli onse adzamva nachita mantha, ndipo palibe mmodzi pakati panu amene adzachitenso choyipa chotere.
12 If thou herist ony men seiynge in oon of thi citees, whiche thi Lord God schal yyue to thee to enhabite,
Ngati mumvetsedwa kuti ku umodzi mwa mizinda imene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mukhalemo,
13 The sones of Belial yeden out fro the myddis of thee, and turneden awei the dwelleris of the citee, and seiden, Go we, and serue alien goddis whiche ye knowen not,
kwapezeka anthu ena oyipa pakati panu ndipo asocheretsa anthu ambiri mʼmizinda yanu, pomanena kuti, “Tiyeni tikapembedze milungu ina” (milungu imene simunayidziwe),
14 enquere thou bisili, and whanne the treuthe of the thing is biholdun diligentli, if thou fyndist that this thing is certeyn, which is seid, and that this abhominacioun is doon in werk,
mukuyenera kufunsa, kulondola ndi kufufuza bwino nkhaniyo. Ndipo ngati zitatsimikizikadi kuti ndi zoona kuti chinthu chonyansa chotere chachitikadi pakati panu,
15 anoon thou schalt smyte the dwelleris of that citee bi the scharpnesse of swerd, and thou schalt `do it awey, and alle thingis that ben ther ynne, `til to beestis.
muyenera kuwapha onse okhala mu mzinda umenewo. Muwonongeretu kwathunthu mzindawo, anthu ake ndi ziweto zake zomwe.
16 Also what euer thing of purtenaunce of houshold is, thou schalt gadere in the myddis of the stretis therof, and thou schalt brenne with that citee, so that thou waste alle thingis to thi Lord God, and it be a biriel euerlastynge; it schal no more be bildid.
Katundu yense wa anthu mu mzindawo mumuwunjike pamodzi pakatikati pa bwalo losonkhanako ndipo mutenthe mzindawo pamodzi ndi katundu wake yense monga nsembe yathunthu yopsereza ya kwa Yehova Mulungu wanu. Mzinda umenewo ukhale bwinja mpaka muyaya, usadzamangidwenso.
17 And no thing of that cursyng schal cleue in thin hond, that the Lord be turned awei fro the yre of his strong veniaunce, and haue mercy on thee, and multiplie thee, as he swoor to thi fadris.
Musapezeke ndi kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa kuti Yehova abweze mkwiyo wake wochititsa manthawu. Adzakuchitirani chifundo ndi kukumverani chisoni, ndipo adzakuchulukitsani monga analonjeza mwa lumbiro kwa makolo anu,
18 Whanne thou hast herd the vois of thi Lord God, thou schalt kepe alle hise heestis whiche Y comaunde to thee to day, that thou do that that is plesaunt in the siyt of thi Lord God.
chifukwa mumamvera Yehova Mulungu wanu, kusunga malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino ndi kuchita zoyenera pamaso pake.

< Deuteronomy 13 >