< Deuteronomy 12 >

1 These ben the heestis and domes, whiche ye owen to do, in the lond which the Lord God of thi fadrys schal yyue to thee, that thou welde it, in alle daies in whiche thou schalt go on erthe.
Awa ndi malangizo ndi malamulo amene muyenera kusamalitsanso kuti muwatsatire mʼdziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani kuti mutenge pa nthawi yonse imene muti mudzakhale mʼdzikomo.
2 Distrie ye alle the places wherynne hethen men whiche ye schulen welde, worschipiden her goddis, on hiy mounteyns, and litle hillis, and vndur ech tre ful of bowis.
Muwonongeretu kwathunthu malo onse a pamwamba pa mapiri ataliatali ndi pa mapiri angʼonoangʼono ndi pansi pa mtengo uliwonse wotambalala pamene mitundu imene muyilande dzikolo ankapembedzerapo milungu yawo.
3 Distrie ye `the auteris of hem, and `breke ye the ymagis; brenne ye the wodis with fier, and al to breke ye the idolis; destrie ye `the names of hem fro the places.
Mugumule maguwa awo ansembe, ndi kuphwanya miyala yawo yachipembedzo ndipo mutenthe pa moto mafano awo a Asera: mugwetse mafano a milungu yawo ndi kufafaniza mayina awo mʼmalo amenewo.
4 Ye schulen not do so to youre Lord God;
Musapembedze Yehova Mulungu wanu monga mmene amachitira iwowa.
5 but ye schulen come to the place which youre Lord God chees of alle youre lynagis, that he putte his name there, and dwelle therynne;
Koma inu muzifunafuna kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati pa mafuko anu kuti ayikeko dzina lake ndi kukhalako. Ku malo amenewa muyenera kupitako.
6 and ye schulen come, and schulen offre in that place youre brent sacrifices, and slayn sacrifices, the dymes, and firste fruytis of youre hondis, and avowis and yiftis, the firste gendrid thingis of oxun, and of scheep.
Kumeneko muzipititsako zopereka zanu ndi nsembe zanu zopsereza, ndi chakhumi chanu ndi mphatso zapadera zimene munalonjeza kupereka ndi zopereka zanu zaufulu ndi ana oyamba a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu.
7 And ye and youre housis schulen ete there in the siyt of youre Lord God; and ye schulen be glad in alle thingis to whiche ye putten hond, in whiche youre Lord God blesside you.
Kumeneko, pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu ndi mabanja anu mudzadya ndi kusangalalako pa china chilichonse chimene mudzakhudza, chifukwa Yehova Mulungu wanu wakudalitsani.
8 Ye schulen not do there tho thingis whiche we don here to dai, ech man that semeth riytful to `hym silf.
Musadzachite monga tikuchitira lero lino, aliyense kumachita zimene akuona kuti ndi zoyenera,
9 For `til in to present tyme ye camen not to reste and possessioun, which the Lord God schal yyue to you.
pakuti simunafike ku malo opumulirako ndi ku cholowa chimene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
10 Ye schulen passe Jordan, and ye schulen dwelle in the lond which youre Lord God schal yyue to you, that ye reste fro alle enemyes `bi cumpas, and dwelle without ony drede.
Koma mudzawoloka Yorodani ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, ndipo Iye adzakupatsani inu mpumulo ku adani anu okuzungulirani kuti mukhale motchinjirizidwa.
11 In the place which youre Lord God chees that his name be therynne. Thidur ye schulen bere alle thingis, whiche Y comaunde, brent sacrifices, and sacrifices, and the dymes, and firste fruytis of youre hondis, and what euere is the beste in yiftis, whiche ye auowiden to the Lord.
Tsono kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe kuti azikhalako muzikabweretsako chilichonse chimene ndikulamulirani inu: zopereka ndi nsembe zanu zopsereza, chakhumi chanu ndi mphatso zapadera, ndi chuma chanu chonse chosankhika chimene munalonjeza kwa Yehova.
12 Ther ye schulen ete bifor youre Lord God, ye, and youre sones and douytris, youre seruauntis, and seruauntessis, and the dekenes, that dwellen in youre citees; for thei han not other part and possessioun among you.
Ndipo kumeneko inu mukasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamodzi ndi ana anu aamuna ndi ana anu aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi a mʼmidzi yanu, amene alibe gawo kapena cholowa chawochawo.
13 Be thou war lest thou offre thi brent sacrifices in ech place which thou seest,
Musamalitse kuti musakaphere nsembe zanu zopsereza paliponse pamene mungafune.
14 but in that place which the Lord chees in oon of thi lynagis thou schalt offre sacrifices, and schalt do what euer thingis Y comaunde to thee.
Mukaphere pa malo okhawo amene Yehova adzawasankhe mwa limodzi la mafuko anu, ndipo kumeneko mukasunge chilichonse chimene ndikulamulireni.
15 Forsothe if thou wolt ete, and the etyng of fleischis delitith thee, sle thou, and ete, bi the blessyng of thi Lord God, which he yaf to thee in thi citees, whether it is vnclene, `that is, spottid ether wemmed and feble, ether clene, `that is, hool in membris and with out wem, which is leueful to be offrid, thou schalt ete as a capret and hert; oneli without etyng of blood,
Koma mukhoza kumapha ziweto zanu mʼmizinda iliyonse ndi kudya nyama yake mmene mungafunire, ngati kuti ndi agwape kapena mbawala, monga mwadalitso limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Woyeretsedwa ndi wosayeretsedwa akhoza kuyidya.
16 which thou schalt schede out as watir on the erthe.
Koma musamadye magazi. Muziwathira pansi ngati madzi.
17 Thou schalt not mowe ete in thi citees the tithis of thi wheete, wyn, and oile, the firste gendrid thingis of droues, and of scheep, and alle thingis whiche thou hast avowid and wolt offre bi fre wille, and the firste fruytis of thin hondis;
Musamadyere mʼmizinda yanu chakhumi cha tirigu wanu ndi vinyo watsopano ndi mafuta, kapena za ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu, kapena chilichonse chimene mwalonjeza kuchipereka, nsembe zanu zaufulu, kapena mphatso zapadera,
18 but thou schalt ete tho bifor thi Lord God, in the place which thi Lord God chees, thou, and thi sone, and douyter, seruaunt, and seruauntesse, and the dekene that dwellith in thi citees; and thou schalt be glad, and schalt be fillid bifor thi Lord God in alle thingis to whiche thou holdist forth thin hond.
mʼmalo mwake, muzidya pamaso pa Yehova Mulungu wanu, kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhira inu, ana anu aamuna ndi aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi ochokera mʼmizinda yanu, ndipo mudzasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa chilichonse chimene mudzachikhudza.
19 Be thou war lest thou forsake the dekene in al tyme, `in which thou lyuest in erthe.
Muonetsetse kuti musawataye Alevi pa masiku onse amene mukhale mʼdziko lanumo.
20 Whanne thi Lord God hath alargid thi termes, as he spak to thee, and thou wolt ete fleischis, whiche thi soule desirith,
Yehova Mulungu wanu akadzakulitsa dziko lanu monga anakulonjezerani, ndipo mukapukwa nyama mumanena kuti, “Ndikufuna nyama,” pamenepo mudzadya mmene mungafunire.
21 forsothe if the place is fer, which thi Lord God chees, that his name be there, thou schalt sle of thin oxun, and scheep, whiche thou hast, as `the Lord comaundide to thee; and thou schalt ete in thi citees as it plesith thee.
Ngati malo amene Yehova Mulungu wanu awasankha kuti ayike Dzina lake ali kutali kwambiri ndi inu, mukhoza kupha ziweto pakati pa ngʼombe ndi nkhosa zimene Yehova wakupatsani, monga ndinakulamulani, ndipo mʼmizinda yanuyanu mukhoza kuzidya mmene mungafunire.
22 As a capret and hert is etun, so thou schalt ete tho; bothe a cleene man and vncleene schulen ete therof in comyn.
Muzidye ngati mukudya gwape kapena mbawala. Onse oyeretsedwa monga mwa mwambo ndi osayeretsedwa omwe akhoza kudya.
23 Oneli eschewe thou this, that thou ete not blood; for the blood `of tho beestis is for the lijf, and therfor thou owist not ete the lijf with fleischis,
Koma muonetsetse kuti musadye magazi, chifukwa magazi ndi moyo, ndipo musamadye moyo pamodzi ndi nyama.
24 but thou schalt schede as watir `the blood on the erthe,
Inu musamadye magazi, muziwathira pansi ngati madzi.
25 that it be wel to thee, and to thi sones after thee, whanne thou hast do that, that plesith in the siyt of the Lord.
Musamadye magazi kuti zikuyendereni bwino inu pamodzi ndi ana anu a pambuyo panu, popeza mudzakhala mukuchita zoyenera pamaso pa Mulungu.
26 Sotheli thou schalt take that that thou `auowidist, and halewidist to the Lord, and thou schalt come to the place which the Lord chees;
Koma mutenge zinthu zanu zoyeretsedwa ndi china chilichonse chimene munalumbira kupereka, ndi kupita kumalo kumene Yehova adzasankhe.
27 and thou schalt offre thin offryngis, fleischis, and blood, on the auter of thi Lord God; thou schalt schede in the auter the blood of sacrifices; forsothe thou schalt ete the fleischis.
Mupereke nsembe zanu zopsereza pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, nyama pamodzi ndi magazi omwe. Magazi a nsembe zanu athiridwe pambali pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, koma nyamayo mukhoza kudya.
28 Kepe thou and here alle thingis whiche Y comaunde to thee, that it be wel to thee, and to thi sones after thee, with outen ende, whanne thou hast do that, that is good and plesaunt in the siyt of thi Lord God.
Onetsetsani kuti muzimvera mawu onsewa amene ndikukupatsani kuti zinthu zizikuyenderani bwino nthawi zonse inu ndi ana anu chifukwa mudzakhala mukuchita zabwino ndi zoyenera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
29 Whanne thi Lord God hath distryed bifor thi face folkis, to whiche thou schalt entre to welde, and thou hast weldid tho folkis, and hast dwellid in `the lond of hem,
Yehova Mulungu wanu adzachotsa pamaso panu mitundu ya anthu amene mukufuna kuwathira nkhondo ndi kuwalanda dzikolo. Koma mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼdziko lawo,
30 be thou war lest thou sue hem, aftir that thei ben distried, whanne thou entrist, and thou seke `the cerymonyes of hem, and seie, As these folkis worschipyden her goddis, so and Y schal worschipe.
ndipo pamene iwo awonongeka pamaso panu, samalirani kuti musakodwe mu msampha pa kufufuza za milungu yawo, nʼkumati, “Kodi anthu a mitunduwa amatumikira bwanji milungu yawo? Ifenso tichita momwemo.”
31 Thou schalt not do in lijk manere to thi Lord God; for thei diden to her goddis alle abhomynaciouns whiche the Lord wlatith, and offriden her sones and douytris, and brenten with fier.
Musapembedze Yehova Mulungu wanu momwe amachitira iwowo, chifukwa popembedza milungu yawoyo amachita zonyansa zamitundumitundu zimene Yehova amadana nazo. Amatentha ngakhale ana awo aamuna ndi aakazi pa moto ngati nsembe za kwa milungu yawo.
32 Do thou to the Lord this thing oneli which Y comaunde to thee, nethir adde thou ony thing, nether abate.
Onetsetsani kuti mukuchita zimene ndikukulamulirani. Musawonjezerepo kapena kuchotserapo.

< Deuteronomy 12 >