< Daniel 12 >

1 Forsothe in that tyme Miyhel, the greet prince, schal rise, that stondith for the sones of thi puple. And tyme schal come, what maner tyme was not, fro that tyme fro which folkis bigunnen to be, `vn to that tyme. And in that tyme thi puple schal be saued, ech that is foundun writun in the book of life.
“Pa nthawi imeneyo Mikayeli, mngelo wamkulu amene amateteza anthu a mtundu wako, adzabwera. Imeneyi idzakhala nthawi ya mavuto aakulu omwe sanaonekepo kuyambira pachiyambi cha mitundu ya anthu mpaka nthawi ikudzayo. Komatu pa nthawiyi anthu a mtundu wako, aliyense amene dzina lake lidzapezeke lolembedwa mʼbuku adzapulumutsidwa.
2 And many of hem that slepen in the dust of erthe, schulen awake fulli, summe in to euerlastynge lijf, and othere in to schenschipe, that thei se euere.
Ambiri mwa amene akugona mʼnthaka adzadzuka: ena adzapita ku moyo wosatha, ena ku malo amanyazi ndi chilango chosatha.
3 Forsothe thei that ben tauyt, schulen schyne as the schynyng of the firmament, and thei that techen many men to riytfulnesse, schulen schyne as sterris in to euerlastynge euerlastyngnessis.
Amene ali anzeru mʼnjira ya chilungamo adzawala ngati kuwala kwa mlengalenga, ndipo amene alondolera ambiri ku njira yolungama, adzawala ngati nyenyezi ku nthawi zosatha.
4 But thou, Danyel, close the wordis, and aseele the book, til to the tyme ordeyned; ful many men schulen passe, and kunnyng schal be many fold.
Koma iweyo, Danieli, sungitsa mawuwa, umate bukuli kufikira nthawi ya chimaliziro. Anthu ambiri adzapita uku ndi uko ndipo nzeru zidzanka zikukulirakulira.”
5 And Y, Danyel, siy, and lo! as tweyne othere men stood; oon stood on this side, on the brenk of the flood, and another on that side, on the tother part of the flood.
Kenaka ine Danieli poyangʼana ndinaona anthu ena awiri atayima, wina tsidya lino la mtsinje, wina tsidya linalo.
6 And Y seide to the man, that was clothid in lynnun clothis, that stood on the watris of the flood, Hou long schal be the ende of these merueils?
Mmodzi mwa awiriwo anafunsa munthu wovala chovala chosalala amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja kuti, “Kodi padzapita nthawi yayitali bwanji kuti zodabwitsazi zidzakwaniritsidwe?”
7 And Y herde the man, that was clothid in lynnun clothis, that stood on the watris of the flood, whanne he hadde reisid his riythond and lefthond to heuene, and hadde sworun by hym that lyueth with outen ende, For in to a tyme, and tymes, and the half of tyme. And whanne the scateryng of the hoond of the hooli puple is fillid, alle these thingis schulen be fillid.
Munthu wovala chovala chosalala, amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja, anakweza dzanja lake lamanja ndi lamanzere kumwamba, ndipo ndinamumva akulumbira mʼdzina la Wamoyo ku nthawi zonse uja kuti, “Zidzachitika patapita zaka zitatu ndi theka. Zinthu zonsezi zidzachitika akadzatha masautso amene agwera anthu olungama.”
8 And Y herde, and vndurstood not; and Y seide, My lord, what schal be aftir these thingis?
Ndinamva, koma sindinamvetsetse. Choncho ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, nanga matsiriziro a zonsezi adzakhala chiyani?”
9 And he seide, Go thou, Danyel, for the wordis ben closid and aseelid, til to the tyme determyned.
Ndipo anandiyankha kuti, “Pita iwe Danieli, pakuti mawuwa ndi osungidwa ndi omatidwa kufikira nthawi ya chimaliziro.
10 Many men schulen be chosun, and schulen be maad whijt, and schulen be preued as fier, and wickid men schulen do wickidli, nether alle wickid men schulen vndurstonde; certis tauyt men schulen vndurstonde.
Anthu ambiri adzayeretsedwa nakhala olungama wopanda chodetsa, koma oyipa adzakhala chiyipire. Palibe mmodzi wa anthu oyipa amene adzamvetsetsa koma okhawo amene ali anzeru adzamvetsetsa.
11 And fro the tyme whanne contynuel sacrifice is takun awei, and abhomynacioun is set in to discoumfort, schulen be a thousynde daies two hundrid and nynti.
“Kuyambira pamene nsembe ya tsiku ndi tsiku idzathetsedwa ndi kukhazikitsa kwa chonyansa chobweretsa chisokonezo chija, padzapita masiku 1,290.
12 He is blessid, that abideth, and cometh fulli, til a thousynde daies thre hundrid and fyue and thritti.
Wodala munthu amene adikirabe nadzafika pa mapeto a masiku 1,335.
13 But go thou, Danyel, to the tyme determyned; and thou schalt reste, and stonde in thi part, in the ende of daies.
“Koma iweyo Danieli, pitiriza ndipo ulimbikire mpaka matsiriziro. Kenaka udzamwalira. Koma mʼmasiku otsiriza udzauka kuti ulandire gawo lako.”

< Daniel 12 >