< Daniel 11 >

1 Forsothe fro the firste yeer of Darius of Medei Y stood, that he schulde be coumfortid, and maad strong.
Ndipo chaka choyamba cha Dariyo Mmedi ine Mikayeli ndinabwera kumuthandiza ndi kumuteteza Gabrieli.
2 And now Y schal telle to thee the treuthe. And lo! thre kyngis schulen stonde yit in Persis, and the fourthe schal be maad riche with ful many richessis ouer alle. And whanne he hath woxe strong bi hise richessis, he schal reise alle men ayens the rewme of Greece.
“Ndipo tsopano ndikuwuza zoona: Mafumu ena atatu adzalamulira ku Peresiya, ndipo kenaka padzadzuka mfumu yachinayi imene idzakhala yolemera kwambiri kuposa onsewo. Popeza kuti idzakhala ndi mphamvu chifukwa cha chuma chake, idzadzutsa onse kuti alimbane ndi ufumu wa Grisi.
3 Forsothe a strong kyng schal rise, and shal be lord in greet power, and schal do that, that schal plese hym.
Kenaka mfumu yamphamvu idzafika imene idzalamulira ndi ufumu waukulu ndi kuchita zimene ifuna.
4 And whanne he schal stonde, his rewme schal be al to-brokun, and it schal be departid in to foure wyndis of heuene, but not in to hise eiris, nether bi the power of hym in which he was lord; for his rewme schal be to-rente, yhe, in to straungeris, outakun these.
Koma ufumu wake ukadzafika pachimake, udzawonongedwa ndi kugawidwa mʼzigawo zinayi. Ufumuwo sudzaperekedwa kwa zidzukulu zake, ndipo olowa mʼmalo mwake sadzakhala ndi mphamvu monga anali nazo, chifukwa ufumu wake udzazulidwa ndi kuperekedwa kwa ena.
5 And the kyng of the south schal be coumfortid; and of the princes of hym oon schal haue power aboue hym, and he schal be lord in power; for whi his lordschipe schal be myche.
“Mfumu ya kummwera idzakhala yamphamvu, koma mmodzi mwa akalonga ake adzakhala ndi mphamvu kuposa iyo; adzalamulira ufumu wake waukulu kwambiri.
6 And after the ende of yeeris `thei schulen be knyt in pees; and the douyter of the kyng of the south schal come to the kyng of the north, to make frenschipe. And sche schal not gete strengthe of arm, nether the seed of hir schal stonde; and sche schal be bitakun, and the yonglyngis of hir that brouyten hir, and he that coumfortide hir in tymes.
Patapita zaka zingapo, mfumu ya kummwera ndi mfumu ya kumpoto adzachita pangano. Mwana wamkazi wa mfumu ya kummwera adzapita nakakwatiwa ndi mfumu ya kumpoto pokhazikitsa pangano la mtendere, koma ulamuliro wake pamodzi ndi wa mwana wake sudzakhalitsa. Mʼmasiku amenewo iye, mwamuna wake, mwana wake ndi atumiki ake, onse adzaperekedwa kwa adani.
7 And a plauntyng of the seed of the rootis of hir schal stonde; and he schal come with an oost, and schal entre in to the prouynce of the kyng of the north, and he schal mysuse hem, and he schal gete;
“Mmodzi wochokera ku banja la mkaziyo adzadzuka nadzalamulira mʼmalo mwake. Iye adzamenyana ndi ankhondo a mfumu ya kumpoto ndi kulowa mʼmalo ake otetezedwa; adzachita nawo nkhondo ndi kupambana.
8 ferthir more he schal gete both the goddis of hem, and grauun ymagis. Also he schal lede into Egipt preciouse vessels of gold, and of siluer, takun in batel. He schal haue the maistrie ayens the kyng of the north;
Iye adzalandanso milungu yawo, mafano awo achitsulo, ndi ziwiya zawo zamtengowapatali zasiliva ndi golide ndi kubwerera nazo ku Igupto. Adzaleka osayithira nkhondo mfumu ya kumpoto kwa zaka zingapo.
9 and the kyng of the south schal entre in to the rewme, and schal turne ayen to his lond.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzathira nkhondo dziko la mfumu ya kummwera koma idzalephera ndi kubwerera kwawo.
10 Forsothe the sones of hym schulen be stirid to wraththe, and thei schulen gadere togidere a multitude of ful many coostis. And he schal come hastynge and flowynge, and he schal turne ayen, and schal be stirid, and schal bigynne batel with his strengthe.
Ana ake adzakonzekera nkhondo ndi kusonkhanitsa gulu lankhondo lalikulu, limene lidzathira nkhondo mfumu yakummwera ngati chigumula mpaka kumalo ake otetezedwa.
11 And the king of the south schal be stirid, and schal go out, and schal fiyte ayens the kyng of the north, and schal make redi a ful grete multitude; and the multitude schal be youun in his hond.
“Kenaka mfumu yakummwera idzatuluka mokwiya ndi kumenya nkhondo ndi mfumu yakumpoto, imene idzasonkhanitsa gulu lalikulu la nkhondo, koma idzayigonjetsa.
12 And he schal take the multitude, and his herte schal be enhaunsid; and he schal caste doun many thousyndis, but he schal not haue the maistrie.
Gulu la nkhondoli likadzagwidwa, mfumu yakummwera idzayamba kudzikuza ndipo idzapha anthu miyandamiyanda, koma kupambanaku sikudzapitirira.
13 For the kyng of the north schal turne, and schal make redi a multitude, myche more than bifore; and in the ende of tymes and of yeeris he schal come hastynge with a ful greet oost, and with ful many richessis.
Popeza mfumu ya kumpoto idzasonkhanitsa gulu lina lankhondo, lochulukirapo kuposa loyamba; ndipo patapita zaka zingapo idzabwera ndi chigulu chachikulu cha nkhondo chokonzekeratu ndi zida.
14 And in tho tymes many men schulen rise togidere ayens the kyng of the south; and the sones of trespassouris of thi puple schulen be enhaunsid, that thei fille the visioun, and thei schulen falle doun.
“Nthawi imeneyo ambiri adzawukira mfumu ya kummwera. Anthu achisokonezo pakati panu nawonso adzawukira pokwaniritsa masomphenya, koma sadzapambana.
15 And the kyng of the north schal come, and schal bere togidere erthe, he schal take strongeste citees; and the armes of the south schulen not susteyne. And the chosun men therof schulen rise togidere, to ayenstonde, and strengthe schal not be.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzafika ndikuzinga mzinda powunda nthumbira za nkhondo ndipo idzagonjetsa mzinda wotetezedwa. Gulu lankhondo la kummwera lidzasowa mphamvu; ngakhale akatswiri awo ankhondo sadzakhala ndi mphamvu zogonjetsera ankhondo a kumpoto.
16 And he schal come on hym, and schal do bi his wille; and noon schal be, that schal stonde ayens his face. And he schal stonde in the noble lond, and it schal be wastid in his hond.
Mfumu ya kumpoto idzachita zofuna zake; palibe aliyense adzayigonjetse. Idzakhazikitsa ulamuliro wake mu Dziko Lokongola. Zonse zidzakhala mu ulamuliro wa mfumu yakumpoto ija.
17 And he schal sette his face, that he come to holde al the rewme of him, and he schal do riytful thingis with hym. And he schal yyue to hym the douyter of wymmen, to distrie hym; and it schal not stonde, and it schal not be his.
Idzafika ndi mphamvu za ufumu wake wonse ndipo idzayesa kuchita pangano la mtendere ndi mfumu ya kummwera. Ndipo idzamupatsa mwana wake wamkazi kuti amukwatire ndi cholinga cholanda ufumu, koma zolinga zake sizidzatheka kapena kumuthandiza.
18 And he schal turne his face to ilis, and he schal take many ilis. And he schal make ceesse the prince of his schenschipe, and his schenschipe schal turne in to hym.
Kenaka idzatembenukira ku mayiko a mʼmbali mwa nyanja ndi kulanda mizinda yambiri, koma mtsogoleri wina wa nkhondo adzathetsa kudzikuza kwakeko ndipo adzabwezera chipongwecho kwa iye.
19 And he schal turne his face to the lordschip of his loond, and he schal snapere, and falle doun, and he schal not be foundun.
Zikadzatha izi, mfumu idzabwerera ku malo otetezedwa a dziko la kwawo koma idzapunthwa ndi kugwa osapezekanso.
20 And the vilest and vnworthi to the kyngis onour schal stonde in the place of hym, and in fewe daies he schal be al to-brokun, not in woodnesse, nether in batel.
“Mfumu imene idzatenga malo ake idzatumiza wokhometsa msonkho kuti chuma cha ufumu wake chichuluke. Komabe mʼzaka zochepa mfumuyo idzawonongedwa osati mu mkwiyo kapena ku nkhondo.
21 And a dispisid man schal stonde in the place of hym, and the onour of a kyng schal not be youun to hym; and he schal come priueli, and he schal gete the rewme bi gile.
“Mʼmalo mwake mudzalowa munthu wonyozeka amene si wa banja laufumu. Iye adzabwera pamene anthu akuganiza kuti ali pa mtendere, ndipo adzalanda ufumuwo mwa chinyengo.
22 And the armes of the fiytere schulen be ouercomun of his face, and schulen be al to-brokun, ferthermore and the duyk of boond of pees.
Kenaka adzagonetsa gulu lalikulu lankhondo kuphatikizapo Mkulu wa Ansembe wapangano.
23 And after frenschipe with hym, he schal do gile. And he schal stie, and he schal ouercome with litil puple;
Atatha kuchita naye pangano, iye adzachita monyenga, ndipo ngakhale adzakhale ndi anthu ochepa adzakhalabe ndi mphamvu.
24 and he schal entre in to grete and riche citees, and he schal do thingis which hise fadris and the fadris of hise fadris diden not. He schal distrie the raueyns, and prei, and richessis of hem, and ayens most stidfast thouytis he schal take counsel, and this `vn to a tyme.
Mwadzidzidzi, iye adzazithira nkhondo zigawo zolemera kwambiri ndipo adzachita zimene makolo ake ngakhale agogo ake sanachitepo. Iye adzagawira zolanda, zofunkha ndi chuma kwa omutsatira. Adzachita chiwembu cholanda mizinda yotetezedwa koma kwa kanthawi kochepa.
25 And the strengthe of hym, and the herte of hym schal be stirid ayens the kyng of the south with a greet oost. And the king of the south schal be stirid to batel with many helpis and ful stronge; and thei schulen not stonde, for thei schulen take counsels ayens hym.
“Mfumu ya kumpoto idzalimba mtima, ndipo idzasonkhanitsa gulu lalikulu la ankhondo kuti lithire nkhondo mfumu yakummwera. Mfumu yakummwera ndi gulu lake lankhondo lalikulu ndi lamphamvu idzathirana nkhondo ndi mfumu yakumpoto koma sidzapambana chifukwa cha ziwembu zimene adzamukonzera.
26 And thei that eeten breed with hym schulen al to-breke hym; and his oost schal be oppressid, and ful many men of hise schulen be slayn, and falle doun.
Amene amadya chakudya ndi mfumu adzamuukira; gulu lake lankhondo lidzagonjetsedwa, ndipo ambiri adzafera ku nkhondo.
27 And the herte of twei kyngis schal be, that thei do yuel, and at o boord thei schulen speke leesyng, and thei schulen not profite; for yit the ende schal be in to an other tyme.
Mafumu awiriwa mitima yawo idzalinga ku zoyipa. Azidzanamizana ali pa tebulo limodzi, koma zolinga zawo sizidzatheka chifukwa nthawi idzakhala isanakwane.
28 And he schal turne ayen in to his lond with many richessis, and his herte schal be ayens the hooli testament, and he schal do, and schal turne ayen in to his lond.
Mfumu ya kumpoto idzabwerera ku dziko la kwawo ndi chuma chambiri, koma mtima wake udzafunitsitsa pangano lopatulika. Idzawononga panganolo ndipo kenaka idzabwerera ku dziko lake.
29 In tyme ordeyned he schal turne ayen, and schal come to the south, and the laste schal not be lijk the formere.
“Patapita nthawi mfumu ya kumpoto idzabwereranso kummwera koma sidzapambana monga inachitira kale.
30 And schippis with three ordris of ooris, and Romayns, schulen come on hym, and he schal be smytun. And he schal turne ayen, and schal haue indignacioun ayens the testament of seyntuarie, and he schal do. And he schal turne ayen, and he schal thenke ayens hem that forsoken the testament of seyntuarie.
Sitima zapamadzi zochokera ku mayiko a ku madzulo zidzalimbana naye, ndipo adzataya mtima. Kenaka idzabwerera mopsa mtima ndi kudzalimbana ndi chipembedzo cha anthu opatulika. Idzabwerera ndi kuchitira chifundo amene sadzasunga pangano loyera.
31 And armes of hym schulen stonde, and schulen defoule the seyntuarie, and schulen take awei the contynuel sacrifice, and schulen yyue abhomynacioun in to desolacioun.
“Ankhondo ake adzayipitsa linga la Nyumba ya Mulungu ndipo adzathetsa nsembe za tsiku ndi tsiku. Kenaka adzakhazikitsa chonyansa chimene chabweretsa chiwonongeko.
32 And wickid men schulen feyne testament gilefuli; but the puple that knowith her God schal holde, and do.
Ndi mawu oshashalika mfumuyo idzakopa amene anaphwanya pangano, koma anthu amene amadziwa Mulungu wawo adzalimbika ndipo adzayikana mfumuyo kwathunthu.
33 And tauyt men in the puple schulen teche ful many men, and schulen falle in swerd, and in flawme, and in to caitifte, and in to raueyn of daies.
“Amene ndi anzeru adzalangiza ambiri. Koma patapita kanthawi adzaphedwa ndi lupanga kapena kutenthedwa, kapena kugwidwa kapena kulandidwa katundu.
34 And whanne thei han feld doun, thei schulen be reisid bi a litil help; and ful many men schulen be applied to hym gilefuli.
Pa nthawi yozunzikayi ena adzawathandiza pangʼono, koma ambiri othandizawo adzakhala achinyengo.
35 And of lerud men schulen falle, that thei be wellid togidere, and be chosun, and be maad whijt til to a tyme determyned; for yit another tyme schal be.
Ena mwa anzeruwo adzaphedwa ndi cholinga chakuti ayengedwe, otsala mwa iwo ayeretsedwe ndi kukhala wopanda banga kufikira nthawi yomaliza, popeza idzafika ndithu nthawi imene Mulungu wayika.
36 And the kyng schal do bi his wille, and he schal be reisid, and magnefied ayens ech god, and ayens God of goddis he schal speke grete thingis; and he schal be dressid, til wrathfulnesse be fillid. For the determynynge is perfitli maad.
“Mfumu ya kumpoto idzachita zimene ikufuna. Idzadzikweza ndi kudziyesa yopambana mulungu aliyense ndipo idzanenera za mwano Mulungu wa milungu. Iyo idzapambana mpaka nthawi yoti Mulungu ayilange mwa mkwiyo itakwana popeza chimene chatsimikizika chiyenera kuchitika.
37 And he schal not arette the God of hise fadris, and he schal be in the coueitisis of wymmen, and he schal not charge ony of goddis, for he schal rise ayens alle thingis.
Mfumuyo idzanyoza milungu ya makolo ake ndiponso mulungu wokondedwa ndi akazi, sidzachitiranso ulemu mulungu aliyense, koma idzadzikweza yokha pamwamba pa onse.
38 Forsothe he schal onoure god of Maosym in his place, and he schal worschipe god, whom hise fadris knewen not, with gold, and siluer, and preciouse stoon, and preciouse thingis.
Mʼmalo mwa onsewo, idzachitira ulemu mulungu wachitetezo; mulungu wosadziwika ndi makolo ake. Iyo idzapereka kwa mulunguyo golide ndi siliva, ndi miyala yokongola, ndiponso mphatso za pamwamba kwambiri.
39 And he schal do that he make strong Moosym, with the alien god which he knew. And he schal multiplie glorie, and schal yyue power to hem in many thingis, and schal departe the lond at his wille.
Anthu opembedza mulungu wachilendo adzakhala ngati linga lake. Idzalemekeza iwowa kwambiri, ndipo idzawayika kuti alamulire anthu ambiri. Idzawagawira dziko ngati malipiro awo.
40 And in the tyme determyned the kyng of the south schal fiyte ayens hym, and the kyng of the north schal come as a tempest ayens hym, in charis, and with knyytis, and in greet nauei.
“Pa nthawi yomaliza mfumu yakummwera idzachita nkhondo ndi mfumu yakumpoto. Koma mfumu yakumpotoyi idzayikantha ndi magaleta ndi akavalo ndi sitima zapamadzi zambiri ngati mphepo yamkokomo. Idzalowa mʼmayiko ambiri ndikuwakokolola onse ngati madzi osefukira.
41 And he schal entre in to londis, and schal defoule hem; and he schal passe, and schal entre in to the gloriouse lond, and many schulen falle. Forsothe these londis aloone schulen be sauyd fro his hond, Edom, and Moab, and princes of the sones of Amon.
Idzalowanso mʼDziko Lokongola ndipo anthu ambiri adzaphedwa. Koma Edomu, Mowabu ndi olamulira a Amoni adzapulumuka.
42 And he schal sende his hond in to londis, and the lond of Egipt schal not ascape.
Idzathira nkhondo mayiko ambiri ndipo ngakhale Igupto sadzapulumuka.
43 And he schal be lord of tresouris of gold, and of siluer, and in alle preciouse thingis of Egipt; also he schal passe bi Libie and Ethiopie.
Idzalanda chuma cha golide, siliva, ndi zonse za mtengowapatali za ku Igupto, ndiponso anthu a ku Libiya ndi Akusi adzagonja kwa iwo.
44 And fame fro the eest and fro the north schal disturble hym; and he schal come with a greet multitude, to al to-breke, and to sle ful many men.
Koma uthenga wochokera kummawa ndi kumpoto udzayiopsa, ndipo idzapita ndi ukali kukawononga ndi kutheratu anthu ambiri.
45 And he schal sette his tabernacle in Apheduo, bitwixe the sees, on the noble hil and hooli; and he schal come til to the heiythe therof, and no man schal helpe hym.
Mfumuyo idzayimika matenti ake aufumu, pakati pa nyanja ndi phiri lokongola. Komabe mapeto ake mfumuyo idzaphedwa, ndipo palibe amene adzayithandize.”

< Daniel 11 >