< Colossians 2 >

1 But Y wole that ye wite, what bisynesse Y haue for you, and for hem that ben at Laodice, and whiche euere saien not my face in fleisch,
Ndikufuna mudziwe kuti ndikukuvutikirani kwambiri, inuyo pamodzi ndi anzanu a ku Laodikaya, ndi ena onse amene sitinaonane maso ndi maso.
2 that her hertis ben coumfortid, and thei ben tauyt in charite, in to alle the richessis of the plente of the vndurstondyng, in to the knowyng of mysterie of God, the fadir of Jhesu Crist,
Cholinga changa nʼchakuti alimbikitsidwe ndi kuyanjana pamodzi mʼchikondi, akhale odzaza ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndi kuti azindikire chinsinsi cha Mulungu, chimene ndi Khristu.
3 in whom alle the tresouris of wisdom and of science ben hid.
Mwa Iyeyu muli chuma chonse chobisidwa cha nzeru ndi chidziwitso.
4 For this thing Y seie, that no man disseyue you in heiythe of wordis.
Ndikukuwuzani zimenezi kuti wina aliyense asakunamizeni ndi kukukopani ndi mawu ake.
5 For thouy Y be absent in bodi, bi spirit Y am with you, ioiynge and seynge youre ordre and the sadnesse of youre bileue that is in Crist.
Pakuti ngakhale sindili pakati panu mʼthupi, ndili nanu pamodzi mu mzimu, ndipo ndikukondwa kuona kuti mukulongosola bwino zonse ndiponso kuti chikhulupiriro chanu mwa Khristu ndi chokhazikika ndithu.
6 Therfor as ye han takun Jhesu Crist oure Lord,
Tsono popeza munavomereza Khristu Yesu kukhala Ambuye anu, mupitirire kukhala mwa Iyeyo.
7 walke ye in hym, and be ye rootid and bieldid aboue in hym, and confermyd in the bileue, as ye han lerud, aboundinge in hym in doynge of thankyngis.
Mukhale ozikika mizu mwa Iye, ndipo moyo wanu umangike pa Iye. Mulimbike mʼchikhulupiriro monga momwe munaphunzirira, ndipo kuyamika kwanu kusefukire.
8 Se ye that no man disseyue you bi filosofie and veyn fallace, aftir the tradicioun of men, aftir the elementis of the world, and not aftir Crist.
Musalole kuti wina aliyense akutengeni ukapolo ndi mʼnzeru zachinyengo zolongosola zinthu zozama, zomwe zimachokera ku miyambo ya anthu ndi ku maganizo awo okhudza za dziko lapansi osati kwa Khristu.
9 For in hym dwellith bodilich al the fulnesse of the Godhed.
Pakuti mʼthupi la Khristu mumakhala umulungu wonse wathunthu.
10 And ye ben fillid in hym, that is heed of al principat and power.
Ndipo inunso ndinu athunthu mwa Khristu. Iye ndiye mtsogoleri wa pamwamba pa maufumu onse ndi maulamuliro wonse.
11 In whom also ye ben circumcidid in circumcisioun not maad with hoond, in dispoyling of the bodi of fleisch, but in circumcisioun of Crist;
Mwa Iye inunso munachita mdulidwe mʼthupi lanu, osati mdulidwe ochitidwa ndi manja a anthu ayi, koma ochitidwa ndi Khristu pamene anavula khalidwe lanu lauchimo lija.
12 and ye ben biried togidere with hym in baptim, in whom also ye han rise ayen bi feith of the worching of God, that reiside hym fro deth.
Mu ubatizo, munayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Khristu ndi kuukitsidwa naye pamodzi, pokhulupirira mphamvu za Mulungu amene anamuukitsa kwa akufa.
13 And whanne ye weren deed in giltis, and in the prepucie of youre fleisch, he quikenyde togidere you with hym;
Pamene munali akufa chifukwa cha machimo anu ndi osachita mdulidwe mʼmitima mwanu, Mulungu anakupatsani moyo mwa Khristu. Iye anatikhululukira machimo athu onse.
14 foryyuynge to you alle giltis, doynge awei that writing of decre that was ayens vs, that was contrarie to vs; and he took awei that fro the myddil, pitchinge it on the cros;
Anafafaniza kalata ya ngongole yathu, pomwe panali milandu yotitsutsa ife. Iye anayichotsa, nayikhomera pa mtanda.
15 and he spuylide principatis and poweris, and ledde out tristili, opynli ouercomynge hem in hym silf.
Ndipo atalanda zida maufumu ndi maulamuliro, Iye anawachititsa manyazi powayendetsa pamaso pa anthu onse atawagonjetsa ndi mtanda.
16 Therfor no man iuge you in mete, or in drink, or in part of feeste dai, or of neomenye,
Nʼchifukwa chake musalole wina aliyense kukuzengani mlandu chifukwa cha zimene mumadya kapena kumwa, kapena za masiku achikondwerero cha chipembedzo, za chikondwerero cha mwezi watsopano, kapena za tsiku la Sabata.
17 or of sabatis, whiche ben schadewe of thingis to comynge; for the bodi is of Crist.
Zimenezi ndi chithunzithunzi chabe cha zinthu zimene zikubwera, koma choonadi chenicheni chikupezeka mwa Khristu.
18 No man disseyue you, willynge to teche in mekenesse, and religioun of aungelis, tho thingis whiche he hath not seyn, walkinge veynli, bolnyd with wit of his fleisch,
Musalole kuti wina aliyense amene amakonda kudzichepetsa mwachiphamaso ndi kumapembedza angelo akulepheretseni kukalandira mphotho. Munthu woteroyu amayankhulanso mwatsatanetsatane zinthu zimene akuti anaziona mʼmasomphenya. Anthuwa ndi odzitukumula ndi fundo zopanda pake zochokera mʼmaganizo mwawo amene si auzimu.
19 and not holdynge the heed, of which al the bodi, bi boondis and ioynyngis togidere vndur mynystrid and maad, wexith in to encreessing of God.
Iwo sakulumikizananso ndi mutu, kumene kumachokera thupi lonse, logwirizidwa ndi kumangiriridwa pamodzi ndi mʼmitsempha yake ndi mnofu, limene limakula monga mmene Mulungu afunira kuti likulire.
20 For if ye ben deed with Crist fro the elementis of this world, what yit as men lyuynge to the world demen ye?
Popeza munafa pamodzi ndi Khristu kusiyana nayo miyambo ya dziko lapansi lino, nʼchifukwa chiyani mukukhalanso ngati a dziko lapansi lino? Bwanji mukumvera malamulo monga awa:
21 That ye touche not, nether taaste,
“Usagwire chakuti,” “Usalawe chakuti,” “Usakhudze chakuti?”
22 nether trete with hoondis tho thingis, whiche alle ben in to deth bi the ilke vss, aftir the comaundementis and the techingis of men;
Malamulo amenewa amakhudza zinthu zimene zimatha zikamagwiritsidwa ntchito, ndipo malamulo ndi zophunzitsa za anthu chabe.
23 whiche han a resoun of wisdom in veyn religioun and mekenesse, and not to spare the bodi, not in ony onour to the fulfillyng of the fleisch.
Ndithu malamulo oterewa amaoneka ngati anzeru, pakuti amalamulira anthu ambiri pa zachipembedzo ndi pa zakudzichepetsa kwa chiphamaso, ndi pa zakuzunza thupi lawo, koma alibe mphamvu zoletsa kuchita zofuna za thupilo.

< Colossians 2 >